< Isaïe 35 >

1 Le désert et le lieu aride se réjouiront, et le lieu solitaire s'égayera, et fleurira comme une rose.
Chipululu ndi dziko lopanda madzi zidzasangalala; dziko lowuma lidzakondwa ndi kuchita maluwa.
2 Il fleurira abondamment, et s'égayera, s'égayant même et chantant en triomphe. La gloire du Liban lui est donnée, avec la magnificence de Carmel et de Saron, ils verront la gloire de l'Eternel, et la magnificence de notre Dieu.
Dzikolo lidzakhala ndi maluwa ochuluka lidzasangalala kwambiri ndi kufuwula mwachimwemwe. Lidzakhala ndi ulemerero monga wa ku mapiri a ku Lebanoni, maonekedwe ake wokongola adzakhala ngati a ku Karimeli ndi a ku Saroni. Aliyense adzaona ulemerero wa Yehova, ukulu wa Mulungu wathu.
3 Renforcez les mains lâches, et fortifiez les genoux tremblants.
Limbitsani manja ofowoka, limbitsani mawondo agwedegwede;
4 Dites à ceux qui ont le cœur troublé; prenez courage, et ne craignez plus; voici votre Dieu; la vengeance viendra, la rétribution de Dieu; il viendra lui-même, et vous délivrera.
nenani kwa a mitima yamantha kuti; “Limbani mtima, musachite mantha; Mulungu wanu akubwera, akubwera kudzalipsira; ndi kudzabwezera chilango adani anu; akubwera kudzakupulumutsani.”
5 Alors les yeux des aveugles seront ouverts, et les oreilles des sourds seront débouchées.
Pamenepo maso a anthu osaona adzapenyanso ndipo makutu a anthu osamva adzatsekuka.
6 Alors le boiteux sautera comme un cerf, et la langue du muet chantera en triomphe; car des eaux sourdront au désert; et des torrents, au lieu solitaire.
Anthu olumala adzalumpha ngati mbawala, ndipo osayankhula adzayimba mokondwera. Akasupe adzatumphuka mʼchipululu ndipo mitsinje idzayenda mʼdziko lowuma,
7 Et les lieux qui étaient secs, deviendront des étangs, et la terre altérée [deviendra] des sources d'eaux, et dans les repaires des dragons où ils faisaient leur gîte, il y aura un parvis à roseaux et à joncs.
mchenga wotentha udzasanduka dziwe, nthaka yowuma idzasanduka ya akasupe. Pamene panali mbuto ya ankhandwe padzamera udzu ndi bango.
8 Et il y aura là un sentier et un chemin, qui sera appelé le chemin de sainteté; celui qui est souillé n'y passera point, mais il sera pour ceux-là; celui qui va son chemin, et les fous, ne s'y égareront point.
Ndipo kumeneko kudzakhala msewu waukulu; ndipo udzatchedwa Msewu Wopatulika. Anthu odetsedwa sadzayendamo mʼmenemo; zitsiru sizidzasochera mʼmenemo.
9 Là il n'y aura point de lion, et aucune de ces bêtes qui ravissent les autres, n'y montera point, et ne s'y trouvera point; mais les rachetés y marcheront.
Kumeneko sikudzakhala mkango, ngakhale nyama yolusa sidzafikako; sidzapezeka konse kumeneko. Koma okhawo amene Yehova anawapulumutsa adzayenda mu msewu umenewu.
10 Ceux donc desquels l'Eternel aura payé la rançon, retourneront, et viendront en Sion avec chant de triomphe, et une joie éternelle sera sur leur tête; ils obtiendront la joie et l'allégresse; la douleur et le gémissement s'enfuiront.
Iwo amene Yehova anawawombola adzabwerera. Adzalowa mu mzinda wa Ziyoni akuyimba; kumeneko adzakondwa mpaka muyaya. Adzakutidwa ndi chisangalalo ndi chimwemwe, ndipo chisoni ndi kudandaula zidzatheratu.

< Isaïe 35 >