< Isaïe 34 >

1 Approchez-vous, nations, pour écouter, et vous peuples, soyez attentifs; que la terre et tout ce qui est en elle, écoute; que le monde habitable et tout ce qui y est produit, [écoute];
Inu anthu a mitundu yonse, bwerani pafupi kuti mumve: tcherani khutu, inu anthu a mitundu ina yonse: Limvetsere dziko lapansi pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo, dziko lonse pamodzi ndi zonse zochokera mʼmenemo!
2 Car l'indignation de l'Eternel est sur toutes ces nations, et sa fureur sur toute leur armée; il les a mises à l'interdit, il les a livrées pour être tuées.
Yehova wayipidwa ndi anthu a mitundu yonse; wapsera mtima magulu awo onse ankhondo. Iye adzawawononga kotheratu, nawapereka kuti aphedwe.
3 Leurs blessés à mort seront jetés là, et la puanteur de leurs corps morts se répandra, et les montagnes découleront de leur sang.
Anthu awo ophedwa adzatayidwa kunja, mitembo yawo idzawola ndi kununkha; mapiri adzafiira ndi magazi awo.
4 Et toute l'armée des cieux se fondra, et les cieux seront mis en rouleau comme un livre, et toute leur armée tombera, comme tombe la feuille de la vigne, et comme tombe celle du figuier.
Dzuwa, mwezi ndi nyenyezi zidzasungunuka ndipo mlengalenga mudzakulungidwa ngati chipepala; nyenyezi zonse zidzayoyoka ngati masamba ofota a mphesa, ngati masamba onyala a mtengo wa mkuyu.
5 Parce que mon épée est enivrée dans les cieux, voici, elle descendra en jugement contre Edom, et contre le peuple que j'ai mis à l'interdit.
Yehova akuti, “Lupanga langa lakhutiratu magazi kumwamba; taonani, likutsika kudzalanga anthu a ku Edomu, anthu amene ndawawononga kotheratu.”
6 L'épée de l'Eternel est pleine de sang; elle s'est engraissée de sa graisse et du sang des agneaux, et des boucs, et de la graisse des rognons de moutons; car il y a un sacrifice à l'Eternel dans Botsra, et une grande tuerie au pays d'Edom.
Lupanga la Yehova lakhuta magazi, lakutidwa ndi mafuta; magazi a ana ankhosa onenepa ndi ambuzi, mafuta a ku impsyo za nkhosa zazimuna. Pakuti Yehova ali ndi nsembe mu Bozira ndiko kuphedwa kwa anthu ambiri mʼdziko la Edomu.
7 Et les licornes descendront avec eux, et les veaux avec les taureaux; leur terre sera enivrée de sang, et leur poussière sera engraissée de graisse.
Pamodzi ndi anthuwo zidzaphedwanso njati, ngʼombe zazimuna zazingʼono ndi zazikulu zomwe. Dziko lawo lidzakhala magazi okhaokha, ndipo nthaka idzakutidwa ndi mafuta.
8 Car il y a un jour de vengeance à l'Eternel, et une année de rétribution pour maintenir le droit de Sion.
Iyi ndi nthawi imene Yehova adzalipsira ndi kulanga adani a Ziyoni.
9 Et ses torrents seront changés en poix, et sa poussière en soufre, et sa terre deviendra de la poix ardente.
Madzi a mʼmitsinje ya Edomu adzasanduka phula, ndipo fumbi lake lidzasanduka sulufule; dziko lake lidzasanduka phula lamoto!
10 Elle ne sera point éteinte ni nuit ni jour; sa fumée montera éternellement, elle sera désolée de génération en génération; il n'y aura personne qui passe par elle à jamais.
Motowo sudzazimitsidwa usiku ndi usana; utsi wake udzafuka kosalekeza. Dzikolo lidzakhala chipululu pa mibado ndi mibado; palibe ndi mmodzi yemwe amene adzadutsemo.
11 Et le cormoran et le butor la posséderont, le hibou et le corbeau y habiteront; et on étendra sur elle la ligne de confusion, et le niveau de désordre.
Mʼdzikomo mudzakhala akabawi ndi anungu; amantchichi ndi akhwangwala adzapanga zisa zawo mʼmenemo. Mulungu adzatambalitsa pa Edomu chingwe choyezera cha chisokonezo ndi chingwe chowongolera cha chiwonongeko.
12 Ses magistrats crieront qu'il n'y a plus là de Royaume, et tous ses gouverneurs seront réduits à rien.
Anthu olemekezeka ake sadzatchedwanso mfumu kumeneko; akalonga ake onse adzachotsedwa.
13 Les épines croîtront dans ses palais, les chardons et les buissons dans ses forteresses, et elle sera le repaire des dragons, et le parvis des chats-huants.
Minga idzamera mʼnyumba zake zankhondo zotetezedwa, khwisa ndi mitungwi zidzamera mʼmalinga ake. Ankhandwe azidzadya mʼmenemo; malo okhalamo akadzidzi.
14 [Là] les bêtes sauvages des déserts rencontreront les [bêtes sauvages des] Iles, et la chouette criera à sa compagne; là même se posera l'orfraie, et y trouvera son repos.
Avumbwe adzakumana ndi afisi, ndipo zirombo za mʼchipululu zizidzayitanizana. Kumeneko kudzafikanso mizimu yoyipa ndi kupeza malo opumulirako.
15 Là le martinet fera son nid, il y couvera, il y éclôra, et il recueillera [ses petits] sous son ombre; et là aussi seront assemblés les vautours l'un avec l'autre.
Kadzidzi adzamangako chisa chake nʼkuyikirako mazira, adzaswa ana ake ndi kusamalira ana ake mu mthunzi wa mapiko ake; akamtema adzasonkhananso kumeneko, awiriawiri.
16 Recherchez au Livre de l'Eternel, et lisez: il ne s'en est pas manqué un seul point; celle-là ni sa compagne n'y ont point manqué; car c'est ma bouche qui l'a commandé, et son Esprit est celui qui les aura assemblés.
Funafunani mʼbuku la Yehova ndi kuwerenga: mwa zolengedwazi palibe chimene chidzasowa; sipadzakhala nʼchimodzi chomwe chopanda chinzake. Pakuti Yehova walamula kuti zitero, ndipo Mzimu wake udzawasonkhanitsa pamodzi.
17 Car il leur a jeté le sort, et sa main leur a distribué cette terre au cordeau; ils la posséderont à toujours, ils y habiteront d'âge en âge.
Yehova wagawa dziko lawo; wapatsa chilichonse chigawo chake. Dziko lidzakhala lawo mpaka muyaya ndipo zidzakhala mʼmenemo pa mibado yonse.

< Isaïe 34 >