< Isaïe 32 >

1 Voici, un Roi régnera en justice, et les Princes présideront avec équité.
Taonani, kudzakhala mfumu ina imene idzalamulira mwachilungamo, ndipo akalonga ake adzaweruza molungama.
2 Et ce personnage sera comme le lieu auquel on se retire à couvert du vent, et comme un asile contre la tempête; comme [sont] les ruisseaux d'eaux dans un pays sec, et l'ombre d'un gros rocher en une terre altérée.
Munthu aliyense adzakhala ngati pothawirapo mphepo ndi malo obisalirapo namondwe, adzakhala ngati mitsinje ya mʼchipululu, ngati mthunzi wa thanthwe lalikulu la mʼdziko lowuma.
3 Alors les yeux de ceux qui voient, ne seront point retenus; et les oreilles de ceux qui entendent, seront attentives.
Ndipo maso a anthu openya sadzakhalanso otseka, ndipo makutu a anthu akumva adzamvetsetsa.
4 Et le cœur des étourdis entendra la science; et la langue des bègues parlera aisément, et nettement.
Anthu a mtima wopupuluma adzadziwa ndi kuchita zinthu mofatsa, ndipo anthu ovutika kuyankhula adzayankhula mosadodoma ndi momveka.
5 Le chiche ne sera plus appelé libéral, et l'avare ne sera plus nommé magnifique.
Chitsiru sichidzatchedwanso munthu waulemu wake ndipo munthu woyipa sadzalemekezedwa.
6 Car le chiche ne prononce que chicheté, et son cœur ne machine qu'iniquité, pour exécuter son déguisement, et pour proférer des choses fausses contre l'Eternel; pour rendre vide l'âme de l'affamé, et faire tarir la boisson à celui qui a soif.
Pakuti munthu opusa amayankhula zauchitsiru, amaganiza kuchita zoyipa: Iye amachita zoyipira Mulungu, ndipo amafalitsa zolakwika zokhudza Yehova; anjala sawapatsa chakudya ndipo aludzu sawapatsa madzi.
7 Les instruments de l'avare sont pernicieux; il prend des conseils pleins de machinations, pour attraper par des paroles de mensonge les affligés, même quand le pauvre parle droitement.
Munthu woyipa njira zake ndi zoyipanso, iye kwake nʼkulingalira zinthu zoyipa. Amalingalira zakuti awononge anthu aumphawi ndi mabodza ake ngakhale kuti waumphawiyo akuyankhula zoona.
8 Mais le libéral prend des conseils de libéralité, et se lève pour user de libéralité.
Koma munthu wolemekezeka amalingaliranso kuchita zinthu zabwino, Iye amakhazikika pa zinthu zabwinozo.
9 Femmes qui êtes à votre aise, levez-vous, écoutez ma voix; filles qui vous tenez assurées, prêtez l'oreille à ma parole.
Khalani maso, inu akazi amene mukungokhala wopanda kulingalira kuti kunja kulinji ndipo imvani mawu anga. Inu akazi odzitama, imvani zimene ndikunena!
10 Dans un an et quelques jours au delà, vous qui vous tenez assurées, serez troublées; car la vendange a manqué; la récolte ne viendra plus.
Pakapita chaka ndi masiku pangʼono inu akazi amatama mudzanjenjemera; chifukwa mitengo ya mphesa idzakanika ndipo zipatso sizidzaoneka.
11 Vous qui êtes à votre aise, tremblez; vous qui vous tenez assurées, soyez troublées; dépouillez-vous, quittez vos habits, et vous ceignez [de sacs] sur les reins.
Nthunthumirani inu okhala mosatekesekanu; ndipo njenjemerani, inu akazi omadzikhulupirira nokhanu. Vulani zovala zanu, ndipo valani ziguduli mʼchiwuno mwanu.
12 On se frappe la poitrine, à cause de la vigne abondante en fruit.
Dzigugudeni pachifuwa mwachisoni chifukwa minda yachonde, ndi mphesa yawonongeka.
13 Les épines et les ronces monteront sur la terre de mon peuple; même sur toutes les maisons où il y a de la joie, et sur la ville qui s'égaye.
Mʼdziko la anthu anga mwamera minga ndi mkandankhuku. Zoona, mulilire nyumba zonse zachikondwerero ndi mzinda uno umene unali wachisangalalo.
14 Car le palais s'en va être abandonné; la multitude de la cité s'en va être délaissée; les lieux inacceccibles du pays et les forteresses seront autant de cavernes à toujours; là se joueront les ânes sauvages, et les petits y paîtront.
Nyumba yaufumu idzasiyidwa, mzinda waphokoso udzakhala wopanda anthu; malinga ndi nsanja zidzasanduka chipululu mpaka muyaya. Abulu adzasangalalamo ndipo ziweto zidzapezamo msipu.
15 Jusqu'à ce que l'Esprit soit versé d'en haut sur nous; et que le désert devienne un Carmel, et que Carmel soit réputé comme une forêt.
Yehova adzatipatsa mzimu wake, ndipo dziko lachipululu lidzasanduka munda wachonde, ndipo munda wachonde udzakhala ngati nkhalango.
16 Le jugement habitera au désert, et la justice se tiendra en Carmel.
Tsono mʼchipululu mudzakhala chiweruzo cholungama ndipo mʼminda yachonde mudzakhala chilungamo.
17 La paix sera l'effet de la justice, et le labourage de la justice sera le repos et la sûreté, jusques à toujours.
Mtendere udzakhala chipatso chachilungamo; zotsatira za chilungamo zidzakhala bata ndi kudzidalira mpaka muyaya.
18 Et mon peuple habitera en un logis paisible, et dans des pavillons assurés, et dans un repos fort tranquille.
Anthu anga adzakhala mʼmidzi yamtendere, mʼnyumba zodalirika, ndi malo osatekeseka a mpumulo.
19 Mais la grêle tombera sur la forêt, et la ville sera entièrement abaissée.
Ngakhale nkhalango idzawonongedwa ndi matalala ndipo mzinda udzagwetsedwa mpaka pansi,
20 O que vous êtes heureux, vous qui semez sur toutes les eaux, et qui y faites aller le pied du bœuf et de l'âne!
inutu mudzakhala odalitsika ndithu. Mudzadzala mbewu zanu mʼmbali mwa mtsinje uliwonse, ndipo ngʼombe zanu ndi abulu anu zidzadya paliponse.

< Isaïe 32 >