< Isaïe 27 >
1 En ce jour-là l'Eternel punira de sa dure et grande et forte épée, le Léviathan, le serpent traversant; le Léviathan, dis-je serpent tortu, et il tuera la baleine qui [est] dans la mer.
Tsiku limenelo, Yehova ndi lupanga lake lakuthwa, lalikulu ndi lamphamvu, adzalanga Leviyatani chinjoka chothawa chija, Leviyatani chinjoka chodzikulunga; adzapha chirombo choopsa cha mʼnyanja.
2 En ce jour-là chantez, vous entre-répondant l'un à l'autre, touchant la vigne [fertile] en vin rouge.
Tsiku limenelo Yehova adzati, “Tidzayimba nyimbo ya munda wamphesa wobereka bwino:
3 C'est moi l'Eternel qui la garde, je l'arroserai de moment en moment, je la garderai nuit et jour, afin que personne ne lui fasse du mal.
Ine, Yehova, ndimawuyangʼanira; ndimawuthirira nthawi zonse. Ndimawulondera usana ndi usiku kuti wina angawononge.
4 Il n'y a point de fureur en moi; qui m'opposera des ronces et des épines pour les combattre? je marcherai sur elles, je les brûlerai toutes ensemble.
Ine sindinakwiye. Ngati mkandankhuku ndi minga zikanaoneka ndikanalimbana nazo! Ndikachita nazo nkhondo; ndikanazitentha zonse ndi moto.
5 Ou forcerait-il ma force? Qu'il fasse la paix avec moi, qu'il fasse la paix avec moi.
Koma ngati apo ayi, abweretu kwa Ine adani angawo kuti ndidzawateteze; apangane nane za mtendere, ndithu, apangane nane za mtendere.”
6 Il fera ci-après que Jacob prendra racine; Israël boutonnera, et s'épanouira; et ils rempliront de fruit le dessus de la terre habitable.
Masiku akubwerawo Yakobo adzazika mizu, Israeli adzaphukira ndi kuchita maluwa, ndipo adzadzaza dziko lonse lapansi ndi zipatso.
7 L'aurait-il frappé de la même plaie dont il frappe celui qui l'a frappé? et aurait-il été tué comme ont été tués ceux qu'il a tués?
Kodi Yehova anakantha Israeli ngati momwe anakanthira anthu amene anazunza Israeli? Kapena kodi Yehova anapha Israeli ngati mmene anthu ena anaphera Israeli?
8 Tu plaideras avec elle modérément, quand tu la renverras; [même quand] il ferait retentir son vent rude, au jour du vent d'Orient.
Yehova mwawalanga powapirikitsa ndi kuwatumiza ku ukapolo, mwawachotsa ndi mpweya wanu woopsa, monga zimachitikira pa tsiku la mkuntho wochokera kummawa.
9 C'est pourquoi l'expiation de l'iniquité de Jacob sera faite par ce moyen, et ceci en sera le fruit entier, que son péché sera ôté; quand il aura mis toutes les pierres de l'autel comme des pierres de plâtre menuisées, et lorsque les bocages, et les tabernacles ne seront plus debout.
Yehova adzakhululuka kulakwa kwa Yakobo. Iwo adzaonetsa kuti alapadi pamene adzaphwanya miyala yonse ya guwa lachikunja, ngati mmene anthu amaphwanyira miyala yanjereza mpaka kukhala ngati fumbi lokhalokha. Sipadzapezekanso mafano a Asera kapena maguwa ofukiza lubani.
10 Car la ville munie sera désolée, le logement agréable sera abandonné et délaissé comme un désert, le veau y paîtra, il y gîtera, et il broutera les branches qui y seront.
Mzinda wamalinga uja wasanduka bwinja, wasanduka malo osiyidwa, ndi kutayidwa ngati chipululu; kumeneko amadyetselako ana angʼombe kumeneko zimapumulako ziweto ndi kumwetula nthambi za mitengo kotheratu.
11 Quand son branchage sera sec il sera brisé, et les femmes y venant en allumeront du feu; car ce n'est pas un peuple intelligent, c'est pourquoi celui qui l'a fait n'aura point pitié de lui, et celui qui l'a formé ne lui fera point de grâce.
Pamene nthambi za mitengoyo zauma, zimathyoka ndipo amayi amabwera nazitola ndi kuzisandutsa nkhuni. Pakuti awa ndi anthu opanda nzeru; kotero Mulungu amene anawapanga sadzachitira chisoni, ndipo Mlengi wawo sawakomera mtima.
12 Il arrivera donc en ce jour-là, que l'Eternel secouera depuis le cours du fleuve, jusqu'au torrent d'Egypte; mais vous serez glanés un à un, ô enfants d'Israël.
Tsiku limenelo Yehova adzasonkhanitsa pamodzi anthu ake mmodzimmodzi kumalo opunthira tirigu, kuchokera ku mtsinje wa Yufurate mpaka ku mtsinje wa ku Igupto.
13 Et il arrivera en ce jour-là, qu'on sonnera du grand cor, et ceux qui s'étaient perdus au pays d'Assyrie, et ceux qui avaient été chassés au pays d'Egypte, reviendront, et se prosterneront devant l'Eternel, en la sainte montagne, à Jérusalem.
Ndipo tsiku limenelo lipenga lalikulu lidzalira. Amene akuzunzika ku Asiriya iwo amene ali ku ukapolo ku Igupto adzabwera ndi kudzalambira Yehova pa phiri lopatulika mu Yerusalemu.