< Isaïe 25 >

1 Eternel, tu [es] mon Dieu, je t'exalterai, je célébrerai ton nom, car tu as fait des choses merveilleuses; les conseils pris dès longtemps [se sont trouvés être] la fermeté même.
Yehova ndinu Mulungu wanga; ine ndidzakukwezani ndi kutamanda dzina lanu, pakuti mwachita zodabwitsa zimene munakonzekeratu kalekale mokhulupirika kwambiri.
2 Car tu as fait de la ville un monceau de pierres, et de la forte cité une ruine; le palais des étrangers qui était dans la ville, ne sera jamais rebâti.
Inu mwasandutsa mzinda uja kukhala mulu wamiyala. Ndipo mzinda wamalinga wasanduka bwinja, linga la anthu achilendo lero si mzindanso ndipo sidzamangidwanso.
3 Et à cause de cela le peuple fort te glorifiera, la ville des nations redoutables te révérera.
Nʼchifukwa chake anthu amphamvu adzakulemekezani; mizinda ya mitundu ya anthu ankhanza idzakuopani.
4 Parce que tu as été la force du chétif, la force du misérable en sa détresse, le refuge contre le débordement, l'ombrage contre le hâle; car le souffle des terribles est comme un débordement [qui abattrait] une muraille.
Inu mwakhala ngati populumukira pa anthu osauka, mwakhala ngati kobisalirako munthu wovutika pa nthawi ya masautso ake. Mwakhala ngati pobisalirapo pa nthawi ya mphepo yamkuntho ndi mthunzi pa nthawi ya dzuwa. Pakuti anthu ankhanza ali ngati mphepo yamkuntho yowomba pa khoma,
5 Tu rabaisseras la tempête éclatante des étrangers, comme le hâle [est rabaissé] dans un pays sec, le hâle, [dis-je, ] par l'ombre d'une nuée; le branchage des terribles sera abattu.
ndiponso ngati kutentha mʼdziko lowuma. Inu mumaletsa phokoso la anthu achilendo. Monga momwe mthunzi wa mtambo umachepetsa kutentha, inu munaletsa nyimbo za anthu ankhanza.
6 Et l'Eternel des armées fera à tous les peuples en cette montagne un banquet de choses grasses, un banquet de vins étant sur leur mère, [un banquet, dis-je, ] de choses grasses et mœlleuses, et de vins étant sur leur mère, bien purifiés.
Pa phiri ili Yehova Wamphamvuzonse adzakonzera anthu a mitundu yonse madyerero a zakudya zokoma ndi vinyo wabwino. Phwando la nyama yonona ndi vinyo wabwino kwambiri.
7 Et il enlèvera en cette montagne l'enveloppe redoublée qu'on voit sur tous les peuples, et la couverture qui est étendue sur toutes les nations.
Iye adzachotsa kulira kumene kwaphimba anthu ngati nsalu. Adzachotsa chinsalu chimene chakuta mitundu yonse ya anthu.
8 Il détruira la mort par sa victoire; et le Seigneur l'Eternel essuiera les larmes de dessus tout visage, et il ôtera l'opprobre de son peuple de dessus toute la terre; car l'Eternel a parlé.
Yehova adzathetsa imfa mpaka muyaya, Ambuye Yehova adzapukuta misozi mʼmaso mwa munthu aliyense; adzachotsa manyazi a anthu ake pa dziko lonse lapansi, Yehova wayankhula.
9 Et l'on dira en ce jour-là; voici, c'est ici notre Dieu; nous l'avons attendu, aussi nous sauvera-t-il; c'est ici l'Eternel; nous l'avons attendu; nous nous égayerons, et nous réjouirons de son salut.
Tsiku limenelo iwo adzati, “Ndithudi, uyu ndiye Mulungu wathu; ife tinamudalira ndipo anatipulumutsa. Uyu ndiye Yehova, ife tinamudalira; tiyeni tikondwe ndi kusangalala chifukwa watipulumutsa.”
10 Car la main de l'Eternel reposera sur cette montagne; mais Moab sera foulé sous lui, comme on foule la paille pour en faire du fumier.
Yehova adzateteza phiri limeneli ndi dzanja lake; ndipo Amowabu adzawapondereza pomwe alilipo, ngati mmene amapondera manyowa mʼdzenje.
11 Et il étendra ses mains au travers de lui, comme celui qui nage les étend pour nager, et il rabaissera sa fierté, se faisant ouverture avec ses mains.
Amowabuwo adzatambasula manja awo mʼmenemo, ngati mmene amachitira munthu wosambira. Koma Mulungu adzathetsa kunyada kwawo ngakhale luso la manja awo.
12 Et il abaissera la forteresse des plus hautes retraites de tes murailles, il les renversera, il les jettera à terre, et les réduira en poussière.
Iye adzagumula malinga awo ataliatali ndipo adzawagwetsa ndi kuwaponya pansi, pa fumbi penipeni.

< Isaïe 25 >