< Isaïe 22 >

1 La charge de la vallée de vision. Qu'as-tu maintenant, que tu sois toute montée sur les toits,
Uthenga wonena za Chigwa cha Masomphenya: Kodi chachitika nʼchiyani, kuti nonsenu mukwere pa madenga?
2 Toi pleine de tumulte, ville bruyante, ville qui ne demandais qu'à t'égayer? tes blessés à mort n'ont pas été blessés à mort par l'épée, et ils ne sont pas morts par la guerre.
Iwe mzinda wodzaza ndi chisangalalo chodzaza tsaya, iwe mzinda waphokoso ndi wosokonekera? Anthu ako ophedwa aja sanaphedwe ndi lupanga, kapena kufera pa nkhondo.
3 Tous tes conducteurs sont allés errant çà et là ensemble, ils ont été liés par les archers; tous ceux des tiens qui ont été trouvés ont été liés ensemble, s'en étant fuis loin.
Atsogoleri ako onse ngakhale anathawa limodzi; koma anagwidwa osadziteteza nʼkomwe. Inu munapezeka ndipo nonse pamodzi munatengedwa ukapolo, ngakhale munathawa pamene mdani akanali patali.
4 C'est pourquoi j'ai dit; retirez-vous de moi, je pleurerai amèrement. Ne vous empressez point de me consoler touchant le dégât de la fille de mon peuple.
Nʼchifukwa chake Ine ndinati, “Chokani pamaso panga; ndilekeni ndilire ndi mtima wowawa. Musayesere kunditonthoza chifukwa cha kuwonongeka kwa anthu anga.”
5 Car c'est le jour de trouble, d'oppression, et de perplexité, de par le Seigneur, l'Eternel des armées, dans la vallée de vision; il s'en va démolir la muraille, et le cri en ira jusqu'à la montagne.
Lero Ambuye Yehova Wamphamvuzonse walola kuti tione mavuto ndi kugonjetsedwa ndiponso chisokonezo mʼChigwa cha Masomphenya. Malinga agumuka, komanso anthu akanalira mofuwula ku mapiri.
6 Même Hélam a pris son carquois, [il y a] des hommes montés sur des chariots, et Kir a découvert le bouclier.
Ankhondo a ku Elamu anadza pa magaleta ndi akavalo ali ndi mivi mʼmanja. Ankhondo a ku Kiri anakonzeka ndi zishango.
7 Et il est arrivé que l'élite de tes vallées a été remplie de chariots, et les gens de cheval se sont tous rangés en bataille contre la porte.
Zigwa zanu zachonde ndi zodzaza ndi magaleta, ndipo asilikali okwera pa akavalo ayikidwa pa zipata za mzinda;
8 Et on a découvert ce qui couvrait Juda, et tu as regardé en ce jour-là vers les armes de la maison du parc.
zonse zoteteza Yuda zachotsedwa. Ndipo tsiku limenelo munayangʼanayangʼana zida zankhondo zomwe zinali mʼnyumba yaufumu ya nkhalango;
9 Et vous avez vu que les brèches de la cité de David étaient grandes; et vous avez assemblé les eaux du bas étang.
inu munaona kuti makoma ambiri a mzinda wa Davide anali ndi malo ambiri ogumuka; munasunga madzi mu chidziwe chakumunsi.
10 Et vous avez fait le dénombrement des maisons de Jérusalem, et démoli les maisons pour fortifier la muraille.
Munawerenga nyumba zonse za mu Yerusalemu ndipo munagwetsa nyumba zina kuti mulimbitse linga logumuka lija.
11 Vous avez aussi fait un réservoir d'eaux entre les deux murailles, pour les eaux du vieux étang; mais vous n'avez point regardé à celui qui l'a faite et formée dès longtemps.
Pakati pa makoma awiri munamanga chitsime chosungiramo madzi ochokera ku dziwe lakale, koma inu simunadalire Mulungu amene anapanga zimenezi, kapena kusamalako za Iye amene anazilenga kale lomwe.
12 Et le Seigneur, l'Eternel des armées, [vous] a appelés ce jour-là aux pleurs et au deuil, à vous arracher les cheveux, et à ceindre le sac;
Pa tsiku limenelo, Ambuye Yehova Wamphamvuzonse anakuyitanani kuti mulire ndi kukhetsa misozi; kumeta mutu wanu mpala ndi kuvala ziguduli.
13 Et voici il y a de la joie et de l'allégresse; on tue des bœufs, on égorge des moutons, on en mange la chair, et on boit du vin; [puis on dit]; Mangeons et buvons; car demain nous mourrons.
Koma mʼmalo mwake inu munakondwa ndi kusangalala; munapha ngʼombe ndi nkhosa; munadya nyama ndi kumwa vinyo. Inu mumati, “Tiyeni tidye ndi kumwa pakuti mawa tifa!”
14 Or l'Eternel des armées m'a déclaré, disant; si jamais cette iniquité vous est pardonnée, que vous n'en mouriez, a dit le Seigneur, l'Eternel des armées.
Yehova Wamphamvuzonse wandiwululira mondinongʼoneza kuti, “Tchimo limeneli sindidzakhululuka mpaka tsiku la kufa kwanu,” akutero Ambuye, Yehova Wamphamvuzonse.
15 Ainsi a dit le Seigneur, l'Eternel des armées; va, entre chez ce trésorier, chez Sebna maître d'hôtel [et lui dis];
Chimene Ambuye, Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Pita, ukanene kwa Sabina kapitawo, amene amayangʼanira nyumba yaufumu:
16 Qu'as-tu à faire ici? et qui [est] ici qui t'appartienne, que tu te sois taillé ici un sépulcre? Il taille un lieu éminent pour son sépulcre, et se creuse une demeure dans un rocher.
Kodi ukuchita chiyani kuno, nanga ndani anakupatsa chilolezo kuti udzikumbire manda kuno, kudzikumbira manda pa phiri ndi kudzisemera malo opumulira mʼthanthwe?
17 Voici, ô homme! l'Eternel te chassera loin, et te couvrira entièrement.
“Samalira, Yehova watsala pangʼono kukugwira zolimba ndi kukuponya mwamphamvu, iwe munthu wamphamvu.
18 Il te fera rouler fort vite comme une boule en un pays large et spacieux; tu mourras là, et là seront les chariots de ta gloire, [de toi qui es] la honte de la maison de ton Seigneur.
Iye adzakukulunga kwambiri ngati mpira ndipo adzakuponyera mʼdziko lalikulu. Kumeneko ndiko ukafere ndipo kumeneko ndiko kudzatsalire magaleta ako. Ndipo udzasanduka wochititsa manyazi nyumba ya mbuye wako.
19 Et je te jetterai hors de ton rang, et on te déposera de ton emploi.
Ine ndidzakuchotsa pa ukapitawo wako ndipo ndidzakutsitsa pa udindo wako.
20 Et il arrivera en ce jour-là que j'appellerai mon serviteur Eliakim, fils de Hilkija.
“Tsiku limenelo ndidzayitanitsa mtumiki wanga, Eliyakimu mwana wa Hilikiya.
21 Et je le vêtirai de ta casaque, je le ceindrai de ton baudrier, je mettrai ton autorité entre ses mains, et il sera pour père à ceux qui habitent dans Jérusalem, et à la maison de Juda.
Ndidzamuveka mkanjo wako ndi kumangira lamba wako mʼchiwuno mwake ndi kumupatsa ulamuliro wako. Iye adzakhala kholo la amene amakhala mu Yerusalemu ndiponso a fuko la Yuda.
22 Et je mettrai la clef de la maison de David sur son épaule; et il ouvrira, et il n'y aura personne qui ferme; et il fermera, et il n'y aura personne qui ouvre.
Ndidzamupatsa ulamuliro wa banja la Davide. Adzatsekula ndipo palibe adzatseke, adzatseka popanda wina kutsekula.
23 Et je le ficherai comme un croc en un lieu ferme; et il sera pour trône de gloire à la maison de son père.
Ufumu wake udzakhala wokhazikika ngati chikhomo chokhomedwa pa malo olimba. Anthu adzalemekeza nyumba ya abale ake chifukwa cha iye.
24 Et on y pendra toute la gloire de la maison de son père, de ses parents, et de celles qui lui appartiennent; tous les ustensiles des plus petites choses, depuis les ustensiles des tasses jusques à tous les ustensiles des musettes.
Ana ndi abale a nyumba ya abambo ake adzakhala ngati katundu pa iye ngati ziwiya zopanda ntchito zimene zapachikidwa pa chikhomo.
25 En ce jour-là, dit l'Eternel des armées, le croc qui avait été fiché en un lieu ferme, sera ôté; et étant retranché il tombera, et ce dont il était chargé sera retranché; car l'Eternel a parlé.
“Yehova Wamphamvuzonse akunena kuti, ‘Tsiku limeneli chikhomo chokhomedwa kwambiri chija sichidzalimbanso; chidzazuka ndipo chidzagwa ndipo zonse zopachikidwa zidzawonongedwa.’” Yehova wayankhula chomwechi.

< Isaïe 22 >