< Isaïe 14 >
1 Car l'Eternel aura pitié de Jacob, et élira encore Israël, et il les rétablira dans leur terre, et les étrangers se joindront à eux, et s'attacheront à la maison de Jacob.
Yehova adzachitira chifundo Yakobo; adzasankhanso Israeli ndi kuwalola kuti akhalenso mʼdziko lawo. Alendo adzabwera kudzakhala nawo ndi kudziphatika okha kukhala ngati a mʼnyumba ya Yakobo.
2 Et les peuples les prendront, et les mèneront en leur lieu, et la maison d'Israël les possédera en droit d'héritage sur la terre de l'Eternel, comme des serviteurs et des servantes; ils tiendront captifs ceux qui les avaient tenus captifs, et ils domineront sur leurs exacteurs.
Anthu a mitundu ina adzaperekeza a Israeli ku dziko lawo. Tsono Aisraeli adzasandutsa anthu a mitundu ina aja kukhala antchito awo aamuna ndi aakazi mʼdziko la Yehova. Ndiye kuti Aisraeli adzasandutsa akapolo anthu amene kale anali ambuye awo. Iwo adzasandutsa akapolo anthu amene kale ankawalamulira ndi kuwazunza.
3 Et il arrivera qu'au jour que l'Eternel fera cesser ton travail, ton tourment, et la dure servitude sous laquelle on t'aura asservi.
Yehova akadzakupumitsani ku zowawa ndi mavuto, ndiponso kuntchito yakalavulagaga imene ankakugwiritsani,
4 Tu te moqueras ainsi du Roi de Babylone, et tu diras; comment se repose l'exacteur? [comment] se repose celle qui était si avide de richesses?
mudzayankhula monyogodola mfumu ya Babuloni kuti, Wopsinja uja watha! Ukali wake uja watha!
5 L'Eternel a rompu le bâton des méchants, et la verge des dominateurs.
Yehova wathyola chikwapu cha anthu oyipa, Iye waphwanya ndodo ya olamulira.
6 Celui qui frappait avec fureur les peuples de coups que l'on ne pouvait point détourner, qui dominait sur les nations avec colère, est poursuivi sans qu'il s'en puisse garantir.
Mfumu ya ku Babuloni inkakantha mitundu ya anthu mwaukali powamenya kosalekeza, Iyo inkagonjetsa anthu a mitundu ina mwaukali ndikuwazunza kosalekeza.
7 Toute la terre a été mise en repos et en tranquillité; on a éclaté en chant de triomphe, à gorge déployée.
Koma tsopano mayiko onse ali pa mpumulo ndi pa mtendere; ndipo akuyimba mokondwa.
8 Même les sapins et les cèdres du Liban se sont réjouis de toi, [en disant]; Depuis que tu es endormi, personne n'est monté pour nous tailler.
Ngakhale mitengo ya payini ndi mikungudza ya ku Lebanoni ikuyimba za iwe mokondwa ndipo ikuti, “Chigwetsedwere chako pansi, palibe wina anabwera kudzatigwetsa.”
9 Le sépulcre profond s'est ému à cause de toi, pour aller au-devant de toi à ta venue, il a réveillé à cause de toi les trépassés, et a fait lever de leurs sièges tous les principaux de la terre, tous les Rois des nations. (Sheol )
Ku manda kwatekeseka kuti akulandire ukamabwera; mizimu ya anthu akufa, aja amene anali atsogoleri a dziko lapansi, yadzutsidwa. Onse amene anali mafumu a mitundu ya anthu ayimiritsidwa pa mipando yawo. (Sheol )
10 Eux tous prendront la parole, et te diront; tu as été aussi affaibli que nous; tu as été rendu semblable à nous;
Onse adzayankha; adzanena kwa iwe kuti, “Iwenso watheratu mphamvu ngati ife; Iwe wafanana ndi ife.”
11 On a fait descendre ta hauteur au sépulcre, avec le bruit de tes musettes; tu es couché sur une couche de vers, et la vermine est ce qui te couvre. (Sheol )
Ulemerero wako wonse walowa mʼmanda, pamodzi ndi nyimbo za azeze ako; mphutsi zayalana pogona pako ndipo chofunda chako ndi nyongolotsi. (Sheol )
12 Comment es-tu tombée des cieux, Etoile du matin, fille de l'aube du jour? toi qui foulais les nations, tu es abattue jusques en terre.
Wagwa pansi bwanji kuchoka kumwamba, iwe nthanda, mwana wa mʼbandakucha! Wagwetsedwa pansi pa dziko lapansi, Iwe amene unagonjetsapo mitundu ya anthu!
13 Tu disais en ton cœur; Je monterai aux cieux, je placerai mon trône au-dessus des étoiles du [Dieu] Fort; je serai assis en la montagne d'assignation, aux côtés d'Aquilon;
Mu mtima mwako unkanena kuti, “Ndidzakwera mpaka kumwamba; ndidzakhazika mpando wanga waufumu pamwamba pa nyenyezi za Mulungu; ndidzakhala pa mpando waufumu pa phiri losonkhanirako, pamwamba penipeni pa phiri la kumpoto.
14 Je monterai au-dessus des hauts lieux des nuées; je serai semblable au Souverain.
Ndidzakwera pamwamba pa mitambo; ndidzafanana ndi Wammwambamwamba.”
15 Et cependant on t'a fait descendre au sépulcre, au fond de la fosse. (Sheol )
Koma watsitsidwa mʼmanda pansi penipeni pa dzenje. (Sheol )
16 Ceux qui te verront te regarderont et te considéreront, [en disant]; N'est-ce pas ici ce personnage qui faisait trembler la terre, qui ébranlait les Royaumes.
Anthu akufa adzakupenyetsetsa nadzamalingalira za iwe nʼkumati, “Kodi uyu ndi munthu uja anagwedeza dziko lapansi ndi kunjenjemeretsa maufumu,
17 Qui a réduit le monde habitable comme en un désert, et qui a détruit ses villes, et n'a point relâché ses prisonniers [pour les renvoyer] en leur maison?
munthu amene anasandutsa dziko lonse chipululu, amene anagwetsa mizinda yake ndipo sankalola kuti anthu ogwidwa abwerere kwawo?”
18 Tous les Rois des nations sont morts avec gloire, chacun dans sa maison;
Mafumu onse a mitundu ya anthu akugona mwaulemu aliyense mʼmanda akeake.
19 Mais tu as été jeté loin de ton sépulcre, comme un rejeton pourri, [comme] un habillement de gens tués, transpercés avec l'épée, qui sont descendus parmi les pierres d'une fosse, comme une charogne foulée aux pieds.
Koma iwe watayidwa kunja kwa manda ako, ngati nthambi yowola ndi yonyansa. Mtembo wako waphimbidwa ndi anthu ophedwa; amene anabayidwa ndi lupanga, anatsikira mʼdzenje lamiyala ngati mtembo woponderezedwa.
20 Tu ne seras point rangé comme eux dans le sépulcre; car tu as ravagé ta terre; tu as tué ton peuple; la race des malins ne sera point renommée à toujours.
Sudzayikidwa nawo mʼmanda mwaulemu, chifukwa unawononga dziko lako ndi kupha anthu ako. Zidzukulu za anthu oyipa sizidzakumbukika nʼpangʼono pomwe.
21 Préparez la tuerie pour ses enfants, à cause de l'iniquité de leurs pères; afin qu'ils ne se relèvent point, et qu'ils n'héritent point la terre, et ne remplissent point de villes le dessus de la terre habitable.
Konzani malo woti muphere ana ake aamuna chifukwa cha machimo a makolo awo; kuti angadzuke ndi kulanda dziko lapansi ndi kulidzaza dziko lonselo ndi mizinda yawo.
22 Je m'élèverai contre eux, dit l'Eternel des armées, et je retrancherai à Babylone le nom, et le reste [qu'elle a], le fils et le petit-fils, dit l'Eternel.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ine ndidzathira nkhondo mzinda wa Babuloni. Ndidzachotseratu mu Babuloni dzina lake ndi onse otsaliramo. Ndiye kuti sipadzakhala ana kapena zidzukulu,” akutero Yehova.
23 Et je la réduirai en habitation de butors, et en marais d'eaux, et je la balayerai d'un balai de destruction, dit l'Eternel des armées.
“Ndidzawusandutsa mzindawo malo okhalamo anungu ndiponso dambo lamatope; ndidzawusesa ndi tsache lowononga,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
24 L'Eternel des armées a juré, en disant; S'il n'est fait ainsi que je l'ai pensé, même comme je l'ai arrêté dans mon conseil, il tiendra;
Yehova Wamphamvuzonse walumbira kuti, “Ndithudi, monga ndaganizira ndidzachitadi choncho, ndipo monga momwe ndatsimikizira zidzakhala momwemo ndithu.
25 C'est que je froisserai le Roi d'Assyrie dans ma terre, je le foulerai sur mes montagnes; et son joug sera ôté de dessus eux, et son fardeau sera ôté de dessus leurs épaules.
Ndidzawawononga Asiriya mʼdziko langa; ndidzawapondereza ndi mapazi pa mapiri anga; ndidzachotsa goli lawo pa anthu anga, ndipo ndidzachotsa katundu wawo pa mapewa awo.”
26 C'est là le conseil qui a été arrêté contre toute la terre, et c'est là la main étendue sur toutes les nations.
Izi ndizo ndakonza kuti zichitike pa dziko lonse lapansi, ndatambasula dzanja pa anthu a mitundu yonse.
27 Car l'Eternel des armées l'a arrêté en son conseil; et qui l'empêcherait? et sa main est étendue; et qui la détournerait?
Pakuti Yehova Wamphamvuzonse watsimikiza, ndipo ndani angamuletse? Dzanja lake latambasulidwa ndipo ndani angalibweze?
28 L'année en laquelle mourut le Roi Achaz, cette charge-ci fut [mise en avant].
Uthenga uwu unabwera chaka chimene mfumu Ahazi anamwalira:
29 Toi, toute la contrée des Philistins, ne te réjouis point de ce que la verge de celui qui te frappait a été brisée; car de la racine du serpent sortira un basilic, et son fruit sera un serpent brûlant qui vole.
Musakondwere inu Afilisti nonse kuti Asiriya amene anali ngati ndodo yokukanthani anathedwa; chifukwa kuchokera ku njoka yomweyi (mfumu ya Aasiriya) mudzatuluka mphiri, ndipo chipatso chake chidzakhala njoka yaliwiro ndiponso yaululu.
30 Les plus misérables seront repus, et les pauvres reposeront en assurance, mais je ferai mourir de faim ta racine, et on tuera ce qui sera resté en toi.
Osaukitsitsa adzapeza chakudya ndipo amphawi adzakhala mwamtendere. Koma anthu ako ndidzawawononga ndi njala, ndipo njalayo idzapha ngakhale opulumuka ako.
31 Toi porte, hurle; toi ville, crie; toi tout le pays des Philistins, sois [comme] une chose qui s'écoule; car une fumée viendra de l'Aquilon, et il ne restera pas un seul homme dans ses habitations.
Lirani kwambiri, anthu a pa chipata! Fuwulani kwambiri, anthu a mu mzinda! Njenjemerani ndi mantha, inu Afilisti nonse! Mtambo wa utsi ukuchokera kumpoto, ndipo palibe wamantha pakati pa ankhondo ake.
32 Et que répondra-t-on aux Ambassadeurs de [cette] nation? [On répondra] que l'Eternel a fondé Sion; et que les affligés de son peuple se retireront vers elle.
Kodi tidzawayankha chiyani amithenga a ku Filisitiya? “Yehova wakhazikitsa Ziyoni, ndipo mu mzinda wakewu, anthu ozunzika apeza populumukira.”