< Osée 9 >

1 Israël ne te réjouis point jusqu'à t'égayer comme les [autres] peuples, de ce que tu as commis adultère, [te retirant] loin de ton Dieu. Tu as aimé le salaire [de la fornication] dans toutes les aires de froment.
Iwe Israeli, usakondwere; monga imachitira mitundu ina. Pakuti wakhala wosakhulupirika kwa Mulungu wako; umakonda malipiro a chiwerewere pa malo aliwonse opunthira tirigu.
2 L'aire et la cuve ne les repaîtra point, et le vin doux leur mentira.
Malo opunthira tirigu ndi malo opsinyira mphesa sadzadyetsa anthu; adzasowa vinyo watsopano.
3 Ils ne demeureront point en la terre de l'Eternel, mais Ephraïm retournera en Egypte, et ils mangeront en Assyrie la viande souillée.
Sadzakhalanso mʼdziko la Yehova. Efereimu adzabwerera ku Igupto ndipo mudzadya chakudya chodetsedwa ku Asiriya.
4 Ils ne feront point aspersion de vin à l'Eternel, et leurs sacrifices ne lui plairont point; [mais ils] leur seront comme le pain de deuil; tous ceux qui en mangeront seront souillés; parce que leur pain est pour leurs trépassés, il n'entrera point dans la maison de l'Eternel.
Iwo sadzaperekanso chopereka cha chakumwa kwa Yehova, kapena nsembe zawo kuti akondweretse Yehovayo. Nsembe zotere zidzakhala kwa iwo ngati chakudya cha anamfedwa; onse akudya chakudya chimenechi adzakhala odetsedwa. Chakudya ichi chidzakhala chodya okha, sichidzalowa mʼnyumba ya Yehova.
5 Que ferez-vous aux jours des fêtes solennelles, et aux jours des fêtes de l'Eternel?
Kodi mudzachita chiyani pa tsiku la maphwando anu oyikika; pa masiku a zikondwerero za Yehova?
6 Car voici, ils s'en sont allés à cause du dégât; l'Egypte les serrera, Memphis les ensevelira; on ne désirera que leur argent; le chardon sera leur héritier, et l'épine sera dans leurs tabernacles.
Ngakhale iwo atathawa chiwonongeko, Igupto adzawasonkhanitsa, ndipo Mefisi adzawayika mʼmanda. Khwisa adzamera pa ziwiya zawo zasiliva, ndipo minga idzamera mʼmatenti awo.
7 Les jours de la visitation sont venus, les jours de la rétribution sont venus, et Israël le saura. Les Prophètes sont fous, les hommes de révélation sont insensés à cause de la grandeur de ton iniquité, et de [ta] grande aversion.
Masiku achilango akubwera, masiku obwezera ali pafupi. Israeli adziwe zimenezi. Chifukwa machimo anu ndi ochuluka kwambiri ndipo udani wanu pa Mulungu ndi waukulu kwambiri. Mneneri amamuyesa chitsiru, munthu wanzeru za kwa Mulungu ngati wamisala.
8 La sentinelle d'Ephraïm est avec mon Dieu; [mais] le Prophète est un filet d'oiseleur dans tous les chemins d'Ephraïm, il [est] l'aversion contre la maison de son Dieu.
Mneneri pamodzi ndi Mulungu wanga ndiwo alonda a Efereimu, koma mneneri amutchera misampha mʼnjira zake zonse, ndipo udani ukumudikira mʼnyumba ya Mulungu wake.
9 Ils se sont extrêmement corrompus, comme aux jours de Guibha; il se souviendra de leur iniquité, il punira leurs péchés.
Iwo azama mu zachinyengo monga masiku a Gibeya. Mulungu adzakumbukira zolakwa zawo ndipo adzawalanga chifukwa cha machimo awo.
10 J'avais, [dira-t-il], trouvé Israël comme des grappes dans un désert; j'avais vu vos pères comme un premier fruit en un figuier dans son commencement; [mais] ils sont entrés vers Bahal-péhor, et se sont séparés pour aller après une chose honteuse, et se sont rendus abominables comme ce qu'ils ont aimé.
“Pamene ndinamupeza Israeli zinali ngati kupeza mphesa mʼchipululu. Nditaona makolo anu, zinali ngati ndikuona nkhuyu zoyambirira kupsa. Koma atafika ku Baala Peori, anadzipereka ku fano lija lochititsa manyazi ndipo anakhala onyansa ngati chinthu chimene anachikondacho.
11 La gloire d'Ephraïm s'envolera aussi vite qu'un oiseau, dès la naissance, dès le ventre, et dès la conception.
Ulemerero wa Efereimu udzawuluka ngati mbalame. Sipadzakhalanso kubereka ana, kuyembekezera kapena kutenga pathupi.
12 Que s'ils élèvent leurs enfants, je les en priverai, [tellement que pas un d'entre eux] ne deviendra homme; car aussi, malheur à eux, quand je me serai retiré d'eux.
Ngakhale atalera ana ndidzachititsa kuti mwana aliyense amwalire. Tsoka kwa anthuwo pamene Ine ndidzawafulatira!
13 Ephraïm était comme j'ai vu Tyr, plantée en un lieu agréable, mais néanmoins Ephraïm mènera ses fils au meurtrier.
Ndaona Efereimu ngati Turo, atadzalidwa pa nthaka ya chonde. Koma Efereimu adzatsogolera ana ake kuti akaphedwe.”
14 Ô Eternel! donne-leur; [mais] que leur donnerais-tu? donne-leur un sein sujet à avorter, et des mamelles taries.
Inu Yehova, muwapatse. Kodi mudzawapatsa chiyani? Apatseni mimba yomangopita padera ndi mawere owuma.
15 Toute leur méchanceté est à Guilgal; c'est pourquoi je les ai là haïs; je les chasserai de ma maison à cause de la malice de leurs actions; je ne continuerai plus à les aimer; tous les principaux d'entre eux sont revêches.
“Chifukwa cha zoyipa zawo zonse ku Giligala, Ine ndinawada kumeneko. Chifukwa cha machitidwe awo auchimo, ndidzawapirikitsa mʼnyumba yanga. Sindidzawakondanso; atsogoleri awo onse ndi owukira.
16 Ephraïm a été frappé; et leur racine est asséchée, ils ne feront plus de fruit; et s'ils engendrent [des enfants], je mettrai à mort les [fruits] désirables de leur ventre.
Efereimu wathedwa, mizu yake yauma sakubalanso zipatso. Ngakhale atabereka ana, Ine ndidzapha ana awo okondedwawo.”
17 Mon Dieu les rejettera, parce qu'ils ne l'ont point écouté, et ils seront vagabonds parmi les nations.
Mulungu wanga adzawakana chifukwa sanamumvere Iye; adzakhala oyendayenda pakati pa anthu a mitundu ina.

< Osée 9 >