< Osée 5 >
1 Ecoutez ceci Sacrificateurs, et vous maison d'Israël, soyez attentifs, et [vous] maison du Roi, prêtez l'oreille; car c'est à vous de faire justice; mais vous êtes devenus [comme] un piège en Mitspa, et comme un rets étendu sur Tabor.
“Ansembe inu, imvani izi! Inu Aisraeli, tcherani khutu! Inu nyumba yaufumu, mvetserani! Chiweruzo ichi ndi chotsutsa inu: Inu munali ngati msampha ku Mizipa, munali ngati ukonde woyalidwa pa phiri la Tabori.
2 Et ils ont subtilement inventé les moyens d'égorger les révoltés, mais je les châtierai tous.
Owukira azama mʼmoyo wakupha, Ine ndidzawalanga onsewo.
3 Je sais qui est Ephraïm, et Israël ne m'est point inconnu: car maintenant, toi, Ephraïm, tu as commis adultère, Israël est souillé.
Ndimadziwa zonse za Efereimu; Aisraeli ndi osabisika kwa Ine. Efereimu wayamba tsopano kuchita zachiwerewere; Israeli wadziyipitsa.
4 Leurs déportements ne permettront point qu'ils retournent à leur Dieu, parce que l'esprit de fornication est au milieu d'eux, et ils ne connaissent point l'Eternel.
“Ntchito zawo siziwalola kubwerera kwa Mulungu wawo. Mʼmitima mwawo muli mzimu wachiwerewere; Iwo sadziwa Yehova.
5 Aussi la fierté d'Israël témoignera contre lui, et Israël et Ephraïm tomberont dans leur iniquité; Juda aussi tombera avec eux.
Kudzikuza kwa Israeli kwakhala umboni womutsutsa; Aisraeli, ngakhale Aefereimu, anagwa mʼmachimo awo; Yudanso anagwa nawo pamodzi.
6 Ils iront avec leurs brebis et leurs bœufs chercher l'Eternel, mais ils ne le trouveront point, il s'est retiré d'avec eux.
Pamene adzapita ndi nkhosa zawo ndi ngʼombe zawo kukapereka nsembe kwa Yehova, iwo sadzamupeza; Iye wawachokera.
7 Ils se sont portés infidèlement contre l'Eternel; car ils ont engendré des enfants étrangers; maintenant un mois les dévorera avec leurs biens.
Iwo ndi osakhulupirika kwa Yehova; amabereka ana amʼchigololo ndipo chikondwerero chawo cha mwezi watsopano chidzawawononga pamodzi ndi minda yawo.
8 Sonnez du cor à Guibha, et de la trompette à Rama; sonnez avec retentissement à Bethaven; on est derrière toi, Benjamin.
“Womba lipenga mu Gibeya, liza mbetete mu Rama. Fuwulani mfuwu wankhondo mu Beti-Aveni; iwe Benjamini tsogolera.
9 Ephraïm sera en désolation au jour de la correction; je le fais savoir parmi les Tribus d'Israël [comme] une chose certaine.
Efereimu adzasanduka bwinja pa tsiku la chilango. Ine ndikulengeza zomwe zidzachitikadi pakati pa mafuko a Israeli.
10 Les Gouverneurs de Juda sont autant de remueurs de bornes, je répandrai sur eux ma fureur comme de l'eau.
Atsogoleri a Yuda ali ngati anthu amene amasuntha miyala ya mʼmalire. Ndidzawakhutulira ukali wanga ngati madzi a chigumula.
11 Ephraïm est opprimé, il est brisé justement, parce que de son bon gré il est allé après le commandement.
Efereimu waponderezedwa, akulangidwa chifukwa chotsatira mafano.
12 Je serai donc à Ephraïm comme la teigne, et à la maison de Juda, comme la vermoulure.
Ine ndili ngati njenjete kwa Efereimu, ngati chinthu chowola kwa anthu a ku Yuda.
13 Et Ephraïm a vu sa langueur, et Juda sa plaie; Ephraïm s'en est allé vers le Roi d'Assyrie, et on a envoyé vers le Roi Jareb, mais il ne vous pourra pas guérir, et il ne pansera point la plaie pour vous en délivrer.
“Efereimu ataona nthenda yake, ndi Yuda ataona zilonda zake, pamenepo Efereimu anatembenukira kwa Asiriya, ndipo anawatumizira mfumu yayikulu kudzawathandiza. Koma mfumuyo singathe kukuchizani, singathe kuchiritsa mabala anu.
14 Car je serai comme un lion à Ephraïm, et comme un lionceau à la maison de Juda; c'est moi, c'est moi qui déchirerai, puis je m'en irai; j'emporterai [la proie], et il n'y aura personne qui me l'ôte.
Pakuti Ine ndidzakhala ngati mkango kwa Efereimu. Ngati mkango wamphamvu kwa Yuda. Ndidzawakhadzula nʼkuchokapo; ndidzawatenga ndipo palibe amene adzawalanditse.
15 Je m'en irai, et retournerai en mon lieu, jusqu'à ce qu'ils se reconnaissent coupables, et qu'ils cherchent ma face; ils me chercheront de grand matin dans leur angoisse.
Ndipo ndidzabwerera ku malo anga mpaka anthu anga atavomereza kulakwa kwawo. Ndipo iwo adzafunafuna nkhope yanga; mʼmasautso awo adzandifunitsitsa Ine.”