< Osée 4 >

1 Enfants d'Israël, écoutez la parole de l'Eternel; car l'Eternel a un procès avec les habitants du pays; parce qu'il n'y a point de vérité, ni de miséricorde, ni de connaissance de Dieu au pays.
Inu Aisraeli, imvani mawu a Yehova, chifukwa Yehova ali ndi mlandu ndi inu amene mumakhala mʼdzikoli: “Mʼdziko mwanu mulibe kukhulupirika, mulibe chikondi mulibe kulabadira za Mulungu.
2 Il n'y a qu'exécration, que mensonge, que meurtre, que larcin et qu'adultère; ils se sont entièrement débordés, et un meurtre touche l'autre.
Muli kutemberera kokha, kunama ndi kupha. Kuba ndi kuchita chigololo; machimo achita kunyanya ndipo akungokhalira kuphana.
3 C'est pourquoi le pays sera en deuil, et tout homme qui y habite sera dans la langueur, avec les bêtes des champs, et les oiseaux des cieux; même les poissons de la mer périront.
Chifukwa chake dziko likulira ndipo onse amene amakhalamo akuvutika; zirombo zakuthengo ndi mbalame zamumlengalenga ndiponso nsomba zamʼnyanja zikufa.
4 Quoi qu'il en soit, qu'on ne plaide avec personne, et qu'on ne reprenne personne; car, quant à ton peuple, ce sont autant de gens qui disputent avec le Sacrificateur.
“Koma wina asapeze mnzake chifukwa, wina aliyense asayimbe mlandu mnzake, pakuti anthu ako ali ngati anthu amene amayimba mlandu wansembe.
5 Tu tomberas donc en plein jour, et le prophète aussi tombera avec toi de nuit, et j'exterminerai ta mère.
Mumapunthwa usana ndi usiku ndipo aneneri amapunthwa nanu pamodzi. Choncho ndidzawononga amayi anu.
6 Mon peuple est détruit à cause qu'il est sans science. Parce que tu as rejeté la science, je te rejetterai, afin que tu ne m'exerces plus la sacrificature. Puisque tu as oublié la Loi de ton Dieu, moi aussi j'oublierai tes enfants.
Anthu anga akuwonongeka chifukwa chosadziwa. “Pakuti mwakana kudziwa, Inenso ndidzakukanani monga ansembe anga; chifukwa mwayiwala lamulo la Mulungu wanu, Inenso ndidzayiwala ana anu.
7 A mesure qu'ils se sont accrus ils ont péché contre moi: je changerai leur gloire en ignominie.
Ansembe ankati akachuluka iwo ankandichimwiranso kwambiri; iwo anasinthanitsa ulemerero wawo ndi chinthu china chonyansa.
8 Ils mangent les péchés de mon peuple, et ne demandent rien que son iniquité.
Amalemererapo pa machimo a anthu anga ndipo amafunitsitsa kuti anthuwo azipitiriza kuchimwa.
9 C'est pourquoi le Sacrificateur sera [traité] comme le peuple, et je le visiterai selon son train, et je lui rendrai selon ses actions.
Ndipo zidzakhala motere: zochitikira anthu ena, zidzachitikiranso ansembe. Ndidzawalanga onsewo chifukwa cha njira zawo, ndidzawabwezera chifukwa cha machitidwe awo.
10 Et ils mangeront, mais ils ne seront point rassasiés; ils se prostitueront, mais ils ne multiplieront point; parce qu'ils ont abandonné l'Eternel, pour ne s'y tenir point.
“Iwo azidzadya koma sadzakhuta; azidzachita zachiwerewere koma sadzachulukana, chifukwa anasiya Yehova kuti adzipereke
11 La luxure, et le vin, et le moût, ôtent l'entendement.
ku zachiwerewere, ku vinyo wakale ndi watsopano, zimene zimachotsa nzeru zomvetsa zinthu
12 Mon peuple demande avis à son bois, et son bâton lui répond: car l'esprit de fornication [les] a fait errer, et ils ont commis adultère se détournant de leur Dieu.
za anthu anga. Anthu anga amapempha nzeru ku fano lamtengo ndipo ndodo yawo yamtengo imawayankha. Mzimu wachiwerewere umawasocheretsa; iwo sakukhulupirika kwa Mulungu wawo.
13 Ils sacrifient sur le sommet des montagnes, et font des parfums sur les coteaux, sous les chênes, sous les peupliers, et sous les ormes, parce que leur ombre est bonne; c'est pourquoi vos filles se prostitueront, et les femmes de vos fils commettront adultère.
Amapereka nsembe pamwamba pa mapiri ndi kufukiza lubani pa zitunda, pa tsinde pa mtengo wa thundu, mnjale ndi mkundi, pamene pali mthunzi wabwino. Nʼchifukwa chake ana anu aakazi akuchita zachiwerewere ndipo akazi a ana anu akuchita zigololo.
14 Je ne ferai point punition de vos filles quand elles se seront abandonnées, ni des femmes de vos fils, quand elles auront commis adultère; à cause qu'ils se séparent avec les prostituées, et qu'ils sacrifient avec les femmes débauchées; ainsi le peuple qui est sans intelligence, sera ruiné.
“Ine sindidzalanga ana anu aakazi pamene iwo adzachita zachiwerewere, kapena akazi a ana anu pamene adzachita zigololo. Paja inu nomwe amunanu mumayenda ndi akazi achiwerewere, ndipo mumapereka nsembe pamodzi ndi akazi achiwerewere a ku malo opembedzerako. Anthu amene alibe nzeru adzawonongeka ndithu!
15 Si tu commets adultère, ô Israël! [au moins] que Juda ne se rende point coupable; n'entrez donc point dans Guilgal, et ne montez point à Beth-aven, et ne jurez point; l'Eternel est vivant.
“Ngakhale umachita chigololo, iwe Israeli, Yuda asapezeke ndi mlandu wotere. “Usapite ku Giligala. Usapite ku Beti-Aveni. Ndipo usalumbire kuti, ‘Pali Yehova wamoyo!’
16 Parce qu'Israël a été revêche comme une génisse revêche, l'Eternel les paîtra maintenant comme des agneaux dans des lieux spacieux.
Aisraeli ndi nkhutukumve, ngosamva ngati ana angʼombe. Kodi Yehova angathe kuwaweta bwanji ngati ana ankhosa pa msipu wabwino?
17 Ephraïm s'est associé aux idoles; abandonne-le.
Efereimu waphathana ndi mafano; mulekeni!
18 Leur breuvage est devenu aigre; ils n'ont fait que se prostituer; ils n'aiment qu'à [dire], apportez; ce n'est qu'ignominie que ses protecteurs.
Ngakhale pamene zakumwa zawo zatha, amapitiriza kuchita zachiwerewere; atsogoleri awo amakonda kwambiri njira zawo zochititsa manyazi.
19 Le vent l'a enserré dans ses ailes, et ils auront honte de leurs sacrifices.
Adzachotsedwa ndi kamvuluvulu ndipo adzachita manyazi chifukwa cha nsembe zawo.

< Osée 4 >