< Osée 13 >
1 Si-tôt qu'Ephraïm eut parlé, on trembla; il avait élevé le [Royaume] en Israël, mais il s'est rendu coupable par Bahal, et il est mort.
Kale Efereimu ankati akayankhula, anthu ankanjenjemera; anali wolemekezeka mu Israeli. Koma analakwa popembedza Baala, motero anafa.
2 Et maintenant ils continuent à pécher, et ils se sont fait de leur argent une image de fonte, selon leur intelligence, des idoles qui ne sont qu'ouvrage d'ouvriers, [mais] desquelles [pourtant] ils disent aux hommes qui sacrifient: qu'on baise les veaux.
Tsopano akunka nachimwirachimwirabe; akudzipangira mafano pogwiritsa ntchito siliva wawo, zifanizo zopangidwa mwaluso, zonsezo zopangidwa ndi amisiri. Amanena za anthu awa kuti, “Amatenga munthu ndi kumupereka nsembe ndipo amapsompsona fano la mwana wangʼombe.”
3 C'est pourquoi ils seront comme la nuée du matin, et comme la rosée du matin, laquelle s'en va; comme la balle qui est emportée hors de l'aire par le tourbillon; et comme la fumée sortant de la cheminée.
Choncho adzakhala ngati nkhungu yammawa, ngati mame amene amakamuka msanga, ngati mungu wowuluka kuchokera pa malo opunthira tirigu, ngati utsi umene ukutulukira pa zenera.
4 Et moi je suis l'Eternel ton Dieu dès le pays d Egypte, et tu ne devrais reconnaître d'autre dieu que moi; aussi il n'y a point de Sauveur que moi.
Koma Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndinakutulutsani mu Igupto. Simuyenera kudziwa Mulungu wina, koma Ine ndekha, palibe Mpulumutsi wina kupatula Ine.
5 Je t'ai connu au désert, en une terre aride.
Ndinakusamalira mʼchipululu, mʼdziko lotentha kwambiri.
6 Ils ont été rassasiés selon [l'abondance de] leurs pâturages, ils ont été rassasiés, et leur cœur s'est élevé; et ils m'ont oublié.
Pamene ndinawadyetsa, iwo anakhuta; iwo atakhuta anayamba kunyada; ndipo anandiyiwala Ine.
7 Je leur ai donc été comme un grand lion; et je les ai épiés sur le chemin comme un léopard.
Motero ndidzawalumphira ngati mkango, ndidzawabisalira mu msewu ngati kambuku.
8 Je les rencontrerai comme une ourse à qui on a ôté ses petits, et je déchirerai la taie de leur cœur, et là je les dévorerai comme un vieux lion; la bête des champs les déchirera.
Ngati chimbalangondo cholandidwa ana ake, ndidzawambwandira ndi kuwathyolathyola. Ndidzawapwepweta ngati mkango; chirombo chakuthengo chidzawakhadzula.
9 On t'a perdu, ô Israël! mais en moi réside ton secours.
“Iwe Israeli, wawonongedwa, chifukwa ukutsutsana ndi Ine, ukutsutsana ndi mthandizi wako.
10 Serai-je ton Roi? Où est-il [ton roi?] et qu'il te délivre en toutes tes villes; où sont tes Gouverneurs, desquels tu as dit: Donne-moi un Roi, et des Seigneurs?
Kodi mfumu yako ili kuti, kuti ikupulumutse? Olamulira ako a mʼmizinda yonse ali kuti, amene iwe unanena za iwo kuti, ‘Patseni mfumu ndi akalonga?’
11 Je t'ai donné un Roi en ma colère, et je l'ôterai en ma fureur.
Choncho Ine ndinakupatsani mfumu mwachipseramtima, ndipo ndinayichotsa mwaukali.
12 L'iniquité d'Ephraïm est liée, et son péché est serré.
Kulakwa kwa Efereimu kwasungidwa, machimo ake alembedwa mʼbuku.
13 Les douleurs [comme] de celle qui enfante le surprendront; c'est un enfant qui n'est pas sage, car il ne se tient pas à temps à la brèche des enfants.
Zowawa zonga za mayi pa nthawi yobala mwana zamugwera, koma iye ndi mwana wopanda nzeru, pamene nthawi yake yobadwa yafika iyeyo safuna kutuluka mʼmimba mwa amayi ake.
14 Je les eusse rachetés de la puissance du sépulcre, et les eusse garantis de la mort; j'eusse été tes pestes, ô mort! et ta destruction, ô sépulcre! [mais] la repentance est cachée loin de mes yeux. (Sheol )
“Ndidzawapulumutsa ku mphamvu ya manda; ndidzawawombola ku imfa. Kodi iwe imfa, miliri yako ili kuti? Kodi iwe manda, kuwononga kwako kuli kuti? “Sindidzachitanso chifundo, (Sheol )
15 Quand il aura fructifié entre ses frères, le vent Oriental, le vent de l'Eternel montant du désert, viendra, et ses sources sécheront, et sa fontaine tarira, et on pillera le trésor de toutes les choses désirables.
ngakhale Efereimu akondwe pakati pa abale ake, mphepo ya kummawa yochokera kwa Yehova idzabwera, ikuwomba kuchokera ku chipululu. Kasupe wake adzaphwa ndipo chitsime chake chidzawuma. Chuma chake chonse chamtengowapatali chidzafunkhidwa ndipo chidzatengedwa.
16 Samarie sera désolée, car elle s'est rebellée contre son Dieu; ils tomberont par l'épée, leurs petits enfants seront écrasés, et on fendra le ventre de leurs femmes enceintes.
Anthu a ku Samariya adzalangidwa chifukwa cha zolakwa zawo, chifukwa anawukira Mulungu wawo. Adzaphedwa ndi lupanga; ana awo adzaphedwa mowamenyetsa pansi, akazi awo oyembekezera adzatumbulidwa pa mimba.”