< Esdras 10 >

1 Et comme Esdras priait, et faisait cette confession, pleurant, et étant prosterné en terre devant la maison de Dieu, une fort grande multitude d'hommes, et de femmes, et d'enfants de ceux d'Israël, s'assembla vers lui; et le peuple pleura abondamment.
Pamene Ezara ankapemphera ndi kuvomereza tchimo lawo, akulira ndipo atadzigwetsa pansi ku Nyumba ya Mulungu, anthu ambiri anabwera kwa iye kudzasonkhana naye. Panali amuna, akazi ndi ana, kuchokera mʼdziko lonse la Israeli ndipo ankalira kwambiri.
2 Alors Sécania fils de Jéhiël, d'entre les enfants de Hélam, prit la parole, et dit à Esdras: Nous avons péché contre notre Dieu, en ce que nous avons pris des femmes étrangères d'entre les peuples de ce pays; mais maintenant il y a espérance pour Israël en ceci.
Ndipo Sekaniya, mwana wa Yehieli, wa fuko la Elamu, anawuza Ezara kuti, “Ife takhala osakhulupirika kwa Mulungu wathu ndipo takhala tikukwatira akazi achilendo a mayiko akunowa. Koma ngakhale zili chomwechi, chikhulupiriro chilipobe pakati pa Aisraeli.
3 C'est pourquoi traitons maintenant [cette] alliance avec notre Dieu, que nous ferons sortir toutes les femmes, et tout ce qui est né d'elles, selon le conseil du Seigneur, et de ceux qui tremblent au commandement de notre Dieu; et qu'il en soit fait selon la Loi.
Tsopano tiyeni tichite naye pangano Mulungu wathu, kuti tichotse akazi onsewa ndi ana awo, potsata malangizo a inu mbuye wanga ndi wa anthu amene amaopa malamulo a Mulungu wathu. Lolani kuti zichitike motsatira malamulo.
4 Lève-toi, car cette affaire te regarde, et nous serons avec toi; prends donc courage, et agis.
Tsono dzukani, imeneyi ndi ntchito yanu. Ife tikuthandizani. Limbani mtima ndipo gwirani ntchitoyi.”
5 Alors Esdras se leva, et fit jurer les principaux des Sacrificateurs, des Lévites, et de tout Israël, qu'ils feraient selon cette parole; et ils jurèrent.
Choncho Ezara anayimirira ndipo analumbiritsa akulu a ansembe, Alevi ndi Aisraeli onse, kuti adzachitedi monga Sekaniya ananenera. Tsono onse analumbira.
6 Puis Esdras se leva de devant la maison de Dieu, et s'en alla dans la chambre de Johanan fils d'Eliasib, et y entra; et il ne mangea point de pain, ni ne but point d'eau, parce qu'il menait deuil à cause du péché de ceux de la captivité.
Ezara anachoka ku Nyumba ya Mulungu napita ku chipinda cha Yehohanani, mwana wa Eliyasibu. Anatandala kumeneko usiku wonse ndipo sanadye chakudya kapena kumwa madzi popeza ankalira chifukwa cha kusankhulupirika kwa anthu obwera ku ukapolo.
7 Alors on publia dans le pays de Juda et dans Jérusalem, à tous ceux qui étaient retournés de la captivité, qu'ils eussent à s'assembler à Jérusalem.
Tsono anthu analengeza mʼdziko lonse la Yuda ndi mʼmizinda yonse ya Yerusalemu kwa onse ochokera ku ukapolo aja kuti asonkhane ku Yerusalemu.
8 Et que quiconque ne s'y rendrait pas dans trois jours, selon l'avis des principaux et des Anciens, tout son bien serait mis à l'interdit, et que pour lui, il serait séparé de l'assemblée de ceux de la captivité.
Ananena kuti wina aliyense amene saonekera pakutha pa masiku atatu, adzalandidwa katundu wake, potsata malangizo a nduna ndi akuluakulu, ndipo adzachotsedwa mʼgulu la anthu obwerako ku ukapolo.
9 Ainsi tous ceux de Juda et de Benjamin s'assemblèrent à Jérusalem dans les trois jours, ce qui fut au neuvième mois le vingtième jour du mois; et tout le peuple se tint devant la place de la maison de Dieu, tremblant pour ce sujet, et à cause des pluies.
Choncho anthu onse a mʼdziko la Yuda ndi a mʼdziko la Benjamini anasonkhana ku Yerusalemu asanathe masiku atatu. Limeneli linali tsiku la 20 la mwezi wa 9. Anthu onse anakhala pansi pa bwalo la Nyumba ya Mulungu akunjenjemera chifukwa cha mvula yambiri imene inagwa.
10 Puis Esdras le Sacrificateur se leva, et leur dit: Vous avez péché en ce que vous avez pris chez vous des femmes étrangères, de sorte que vous avez augmenté le crime d'Israël.
Ndipo wansembe Ezara anayimirira nawuza anthuwo kuti, “Inu mwachimwa pomakwatira akazi achikunja ndi kumawonjezera pa tchimo la Aisraeli.
11 Mais maintenant faites confession [de votre faute] à l'Eternel le Dieu de vos pères, et faites sa volonté, et séparez-vous des peuples du pays, et des femmes étrangères.
Tsopano lapani kwa Yehova, Mulungu wa makolo anu ndi kuchita zimene akufuna. Dzipatuleni kwa anthu a mayiko enawa ndi kwa akazi achikunjawa.”
12 Et toute l'assemblée répondit, et dit à haute voix: C'est notre devoir de faire ce que tu as dit;
Gulu lonse la anthu linayankha ndi mawu ofuwula kuti, “Nʼzoona! Tichita monga mwaneneramu.
13 Mais le peuple est grand, et ce temps est fort pluvieux, c'est pourquoi il n'[y a] pas moyen de demeurer dehors, et cette affaire n'est pas d'un jour, ni de deux; car nous sommes beaucoup de gens qui avons péché en cela.
Koma pano pali anthu ambiri ndiponso mvula ikugwa kwambiri, choncho sitingakayime panja. Ndiponso ntchitoyi si ya tsiku limodzi kapena awiri, chifukwa tachimwa kwambiri pa zimene tachitazi.
14 Que tous les principaux d'entre nous comparaissent donc devant toute l'assemblée, et que tous ceux qui sont dans nos villes, et qui ont pris chez eux des femmes étrangères, viennent en certain temps, et que les Anciens de chaque ville et ses juges soient avec eux; jusqu'à ce que nous détournions de nous l'ardeur de la colère de notre Dieu, [et] que ceci soit achevé.
Tsono mulole kuti atsogoleri athu ayimirire mʼmalo mwa anthu onse. Aliyense wa mʼmizinda yathu amene anakwatira mkazi wachikunja abwere pa nthawi imene inu munene, ndipo abwere pamodzi ndi akuluakulu ndi oweruza a mzindawo. Choncho mkwiyo wa Mulungu wathu udzatichoka.”
15 Et Jonathan fils d'Hazaël, et Jahzéja fils de Tikva furent établis pour cette affaire; et Mésullam et Sabéthaï, Lévites, les aidèrent.
Koma Yonatani yekha mwana wa Asaheli ndi Yahazieli mwana wa Tikiva ndiwo anatsutsapo pa zimenezi. Tsono Mesulamu ndi Mlevi Sebetai anawayikira kumbuyo.
16 Et ceux qui étaient retournés de la captivité en firent de même, tellement qu'on choisit Esdras le Sacrificateur, [et] ceux qui étaient les Chefs des pères selon les maisons de leurs pères, tous [nommés] par leurs noms, qui commencèrent leurs séances le premier jour du dixième mois, pour s'informer du fait.
Choncho anthu obwerako ku ukapolo aja anachita zimene zimafunika. Ndipo wansembe Ezara anasankha amuna amene anali atsogoleri a mabanja potsata mafuko awo ndipo onsewo analembedwa mayina awo. Tsiku loyamba la mwezi wa khumi anayambapo kuyifufuza nkhani imeneyi.
17 Et le premier jour du premier mois ils eurent fini avec tous ceux qui avaient pris chez eux des femmes étrangères.
Ndipo pofika tsiku loyamba la mwezi woyamba anali atathana nawo anthu amene anakwatira akazi achilendo aja.
18 Or quant aux fils des Sacrificateurs qui avaient pris chez eux des femmes étrangères, il se trouva d'entre les enfants de Jésuah, fils de Jotsadak et de ses frères, Mahaséja, Elihézer, Jarib, et Guédalia;
Nawu mʼndandanda wa ansembe amene anakwatira akazi achikunja: Pa banja la Yesuwa ndi abale ake, ana a Yozadaki, panali awa: Maaseiya, Eliezara, Yaribu ndi Gedaliya.
19 Qui donnèrent les mains à renvoyer leurs femmes; et avouant qu'ils étaient coupables, [ils offrirent] pour leur délit un bélier du troupeau.
Iwo anatsimikiza zochotsa akazi awo ndipo chifukwa cha kulakwa kwawo aliyense anapereka nkhosa yayimuna ngati nsembe yopepesera machimo.
20 Des enfants d'Immer, Hanani, et Zébadia;
Pa banja la Imeri panali awa: Hanani ndi Zebadiya.
21 Et des enfants de Harim, Mahaséja, Elie, Sémahia, Jéhiël, et Huzija;
Pa banja la Harimu panali awa: Maseya, Eliya, Semaya, Yehieli ndi Uziya.
22 Et des enfants de Pashur, Eliohenaï, Mahaséja, Ismaël, Nathanaël, Jozabad, et Elhasa;
Pa banja la Pasuri panali awa: Eliyoenai, Maseya, Ismaeli, Netaneli, Yozabadi ndi Eleasa.
23 Et des Lévites, Jozabad, Simhi, Kélaja, (qui est le même que Kélita) Péthahia, Juda, et Elihézer;
Pakati pa Alevi panali: Yozabadi, Simei, Kelaya (ndiye kuti, Kelita). Petaya, Yuda ndi Eliezara.
24 Et des chantres, Eliasib; et des portiers, Sallum, Telem, et Uri.
Pakati pa oyimba nyimbo panali Eliyasibu. Ochokera kwa alonda a zipata: Salumu, Telemu ndi Uri.
25 Et de ceux d'Israël; des enfants de Parhos, Ramia, Jizija, Malkija, Mijamin, Elhazar, Malkija et Bénaja;
Ochokera pakati pa Aisraeli ena: a fuko la Parosi anali Ramiya, Iziya, Malikiya, Miyamini, Eliezara, ndi Benaya.
26 Et des enfants de Hélam, Mattania, Zacharie, Jéhiël, Habdi, Jérémoth, et Elie;
A fuko la Elamu anali Mataniya, Zekariya, Yehieli, Abidi, Yeremoti ndi Eliya.
27 Et des enfants de Zattu, Eliohénaï, Eliasib, Mattania, Jérémoth, Zabad, et Haziza;
A fuko la Zatu anali Eliyoenai, Eliyasibu, Mataniya, Yeremoti, Zabadi ndi Aziza.
28 Et des enfants de Bébaï, Johanan, Hanania, Zabbaï, et Hathlaï;
A fuko la Bebai anali Yehohanani, Hananiya, Zabayi ndi Atilayi.
29 Et des enfants de Bani, Mésullam, Malluc, Hadaja, Jasub, Séal, et Ramoth;
A fuko la Bani anali Mesulamu, Maluki, Adaya, Yasubu, Seali ndi Yeremoti.
30 Et des enfants de Pahath-Moab, Hadna, Kélal, Bénaja, Mahaséja, Mattania, Bethsaléël, Binnuï, et Manassé;
A fuko la Pahati-Mowabu anali Adina, Kelali, Benaya, Maseya, Mataniya, Bezaleli, Binuyi ndi Manase.
31 Et des enfants de Harim, Elihézer, Jisija, Malkija, Sémahia, Siméon;
A fuko la Harimu anali Eliezara, Isiya, Malikiya, Semaya, Simeoni,
32 Benjamin, Malluc [et] Semaria;
Benjamini, Maluki ndi Semariya.
33 [Et] des enfants de Masum, Mattenaï, Mattata, Zabad, Eliphélet, Jérémaï, Manassé, et Simhi;
A fuko la Hasumu anali Mataneyi, Matata, Zabadi, Elifeleti, Yeremayi, Manase ndi Simei.
34 [Et] des enfants de Bani, Mahadaï, Hamram, Uël,
A fuko la Bani anali Madai, Amramu, Uweli,
35 Bénaja, Bédéja, Kéluhu,
Benaya, Bediya, Keluhi,
36 Vania, Mérémoth, Eliasib,
Vaniya, Meremoti, Eliyasibu,
37 Mattania, Matténaï, Jahasaï,
Mataniya, Matenayi ndi Yasu.
38 Bani, Binnuï, Simhi,
A fuko la Binuyi anali Simei,
39 Sélémia, Nathan, Hadaja,
Selemiya, Natani, Adaya,
40 Mabnadbaï, Sasaï, Saraï,
Makinadebayi, Sasai, Sarai,
41 Hazaréel, Sélémia, Sémaria,
Azaleli, Selemiya, Semariya,
42 Sallum, Amaria, et Joseph;
Salumu, Amariya ndi Yosefe.
43 [Et] des enfants de Nébo, Jéhiël, Mattitia, Zabad, Zébina, Jaddan, Joël, et Bénaja.
A fuko la Nebo anali Yeiyeli, Matitiya, Zabadi, Zebina, Yadai, Yoweli ndi Benaya.
44 Tous ceux-là avaient pris des femmes étrangères; et il y avait quelques-uns d'entr'eux qui avaient eu des enfants de ces femmes-là.
Onsewa anakwatira akazi achilendo. Tsono anawasudzula akaziwo ndi kuwatumiza kwawo pamodzi ndi ana awo.

< Esdras 10 >