< Ézéchiel 46 >

1 Ainsi a dit le Seigneur l'Eternel: la porte du parvis intérieur, laquelle regarde l'Orient, sera fermée les six jours ouvriers, mais elle sera ouverte le jour du Sabbat, et pareillement elle sera ouverte le jour de la nouvelle lune.
“Ambuye Yehova akuti, Chipata chakummawa cha bwalo lamʼkati chizikhala chotseka pa masiku asanu ndi limodzi ogwira ntchito, koma chizitsekulidwa pa tsiku la sabata ndi pa tsiku la chikondwerero cha mwezi watsopano.
2 Et le Prince y entrera par le chemin de l'allée de la porte [du parvis] extérieur, et se tiendra près de l'un des poteaux de [l'autre] porte, et les Sacrificateurs prépareront son holocauste et ses sacrifices de prospérité; puis il se prosternera sur le seuil de cette [autre] porte, et ensuite il sortira; mais cette [autre] porte ne sera point fermée jusques au soir.
Mfumu izilowa podzera mʼkhonde la mʼkati la chipata pochokera kunja, nʼkudzayima pafupi ndi nsanamira yapakhomo. Ansembe apereke nsembe yake yopsereza ndi nsembe yake yachiyanjano. Mfumuyo ipembedze pa chiwundo cha pa chipatacho kenaka nʼkutuluka. Koma chipatacho asachitseke mpaka madzulo.
3 Tellement que le peuple du pays se prosternera devant l'Eternel à l'entrée de cette [autre] porte-ci, les jours de Sabbat et des nouvelles lunes.
Anthu a mʼdziko azipembedza pamaso pa Yehova pa khomo la chipata chimenechi pa masiku a sabata ndi pa tsiku la mwezi watsopano.
4 Or l'holocauste que le Prince offrira à l'Eternel le jour du Sabbat sera de six agneaux sans tare, et d'un bélier sans tare.
Nsembe yopsereza imene mfumu iyenera kupereka kwa Yehova ikhale motere: pa tsiku la Sabata izipereka ana ankhosa aamuna asanu ndi mmodzi wopanda chilema, ndiponso nkhosa yayima yopanda chilema.
5 Et le gâteau pour le bélier [sera] d'un épha, et le gâteau pour chacun des agneaux sera selon ce qu'il pourra donner; mais il y aura un hin d'huile pour chaque épha.
Pamodzi ndi nkhosa yayimuna, mfumu izipereka nsembe ya chakudya yokwanira efa imodzi. Pamodzi ndi ana ankhosa, mfumu izipereka monga ikufunira kutero. Iperekenso hini imodzi ya mafuta pa efa iliyonse ya tirigu.
6 Et au jour de la nouvelle Lune [son holocauste] sera d'un jeune veau, sans tare, et de six agneaux et d'un bélier, aussi sans tare.
Pa tsiku la mwezi watsopano mfumuyo ipereke mwana wangʼombe wamwamuna, ana ankhosa asanu ndi mmodzi ndiponso nkhosa yayimuna, zonsezi zopanda chilema.
7 Et il offrira pour le gâteau du veau, un épha, et pour le gâteau du bélier, un [autre] épha, et pour chacun des agneaux selon ce qu'il pourra donner; mais [il y aura] un hin d'huile pour chaque épha.
Ipereke efa imodzi ya tirigu pa ngʼombe yayimuna iliyonse ndiponso efa ina pa nkhosa yayimuna iliyonse. Pa ana ankhosa ipereke tirigu monga ikufunira kutero. Pamodzi ndi efa ya tirigu, ipereke hini imodzi ya mafuta.
8 Et comme le Prince sera entré [au Temple] par le chemin de l'allée de cette [même] porte [du parvis] extérieur, laquelle regarde l'Orient, aussi sortira-t-il par le même chemin.
Pamene mfumu ikulowa, izidzera mʼkhonde lamʼkati la chipata chakummawa, izitulukiranso pomwepo.
9 Mais quand le peuple du pays [y] entrera pour se présenter devant l'Eternel, aux fêtes solennelles, celui qui y entrera par le chemin de la porte du Septentrion pour y adorer l'Eternel, sortira par le chemin de la porte du Midi; et celui qui y entrera par le chemin de la porte du Midi, sortira par le chemin de la porte qui regarde vers le Septentrion; tellement que personne ne retournera par le chemin de la porte par laquelle il sera entré, mais il sortira par celle qui est vis-à-vis.
“Anthu a mʼdzikomo akabwera kudzapembedza Yehova pa masiku a chikondwerero, ngati munthu alowera pa chipata chakumpoto atulukire chipata chakummwera. Munthu wolowera chipata chakummwera, atulukire chipata chakumpoto. Munthu asatulukire pomwe walowera, koma atulukire pa chipata choyangʼanana nacho.
10 Alors le Prince entrera parmi eux, quand ils entreront; et quand ils sortiront, ils sortiront [ensemble].
Mfumu izidzakhala pakati pawo. Anthu akamadzalowa mfumu idzalowa nawo. Anthu akamadzatuluka mfumu idzatuluka nawo.
11 Or dans ces fêtes solennelles, et dans ces solennités, le gâteau d'un veau sera d'un épha, et [le gâteau] d'un bélier d'un [autre] épha, et le gâteau de chacun des agneaux sera selon que le Prince pourra donner, et il y aura un hin d'huile pour chaque épha.
“Pa masiku achikondwerero ndi pa masiku ena osankhidwa, zopereka za chakudya zikhale zokwanira efa imodzi pamodzi ndi ngʼombe yayimuna iliyonse, efa imodzinso ndi nkhosa yayimuna, koma pa mwana wankhosa apereke monga angathere. Iperekenso hini imodzi ya mafuta pa efa iliyonse.
12 Que si le Prince offre un sacrifice volontaire, quelque holocauste, soit quelques sacrifices de prospérités en offrande volontaire à l'Eternel, on lui ouvrira la porte qui regarde l'Orient, et il offrira son holocauste et ses sacrifices de prospérités comme il les offre le jour du Sabbat, puis il sortira, et après qu'il sera sorti, on fermera cette porte.
Pamene mfumu ikufuna kupereka chopereka chaufulu kwa Yehova, kaya ndi nsembe yopsereza kapena zopereka za chiyanjano, ayitsekulire chipata chakummawa. Iyo ipereke nsembe yopsereza kapena zopereka zake za chiyanjano monga imachitira pa tsiku la Sabata. Kenaka ituluke ndipo mfumuyo itatuluka, atseke chitsekocho.
13 Tu sacrifieras chaque jour en holocauste à l'Eternel un agneau d'un an sans tare, tu le sacrifieras tous les matins.
“Tsiku lililonse nthawi ya mmawa azipereka kwa Yehova mwana wankhosa wa chaka chimodzi.
14 Tu offriras aussi tous les matins avec lui un gâteau, fait de la sixième partie d'un épha, et de la troisième d'un hin d'huile pour en détremper la fine farine; c'est là le gâteau continuel qu'il faut offrir par ordonnances perpétuelles.
Pamodzi ndi nyamayo aziperekanso mmawa uliwonse chopereka cha chakudya chokwanira chimodzi mwa zigawo zisanu ndi chimodzi za efa. Aziperekanso chimodzi mwa zigawo zitatu za hini ya mafuta okandira ufa wosalala. Chopereka cha chakudya chimenechi chiziperekedwa kwa Yehova nthawi zonse mwa lamulo.
15 Ainsi on offrira tous les matins [en] holocauste continuel cet agneau et ce gâteau détrempé avec cette huile.
Motero azipereka mwana wankhosa ndi chopereka cha chakudya ndi mafuta mmawa uliwonse kuti zikhale nsembe zopsereza za tsiku ndi tsiku.
16 Ainsi a dit le Seigneur l'Eternel: quand le Prince aura fait un don [de quelque pièce] de son héritage à quelqu'un de ses fils, ce don appartiendra à ses fils; parce qu'ils ont droit de possession en l'héritage.
“‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ngati kalonga apereka mphatso chigawo cha cholowa chake kwa mmodzi mwa ana ake, mphatsoyo idzakhala ya ana akewo. Idzakhala yawo chifukwa ndi cholowa chawo.
17 Mais s'il fait un don [de quelque pièce] de son héritage à l'un de ses serviteurs, le don lui appartiendra bien, mais seulement jusques à l'an d'affranchissement, auquel il retournera au Prince; [car] quoi qu'il en soit, c'est son héritage qui appartient à ses fils, [c'est pourquoi] il leur demeurera.
Koma ngati ipereka mphatso yotere kuchokera pa cholowa chake kwa mmodzi mwa antchito ake, mphatsoyo idzakhala ya wantchitoyo mpaka chaka chaufulu. Pambuyo pake idzabwereranso kwa kalongayo chifukwa cholowa chake ndi cha ana ake.
18 Et le Prince n'usurpera rien de l'héritage du peuple, les fraudant de la possession qui leur appartient, [seulement] il laissera en héritage à ses fils la possession qui lui appartient, afin qu'aucun de mon peuple ne soit chassé de sa possession.
Kalonga asalande cholowa chilichonse cha anthu, kuwachotsa mʼdera lawo la dziko. Iye apereke kwa ana ake cholowa chawo chochokera pa chuma chakechake, kuti pasapezeke ndi mmodzi yemwe mwa anthu anga wolandidwa chuma chake.’”
19 Puis il me mena par l'entrée qui était vers le côté de la porte, aux chambres saintes qui appartenaient aux Sacrificateurs, lesquelles regardaient vers le Septentrion, et voilà, il y avait un certain lieu aux deux côtés du fond qui regardaient vers l'Occident.
Kenaka munthu uja anandidzeretsa pa khomo la pambali pa chipata nandilowetsa ku zipinda za ansembe zoyangʼana kumpoto. Ndipo ndinaona kumeneko malo chakumadzulo kwa zipindazo.
20 Et il me dit: c'est là le lieu auquel les Sacrificateurs bouilliront [le reste de la bête qu'on aura sacrifiée pour] le délit, et [le reste de la bête qu'on aura sacrifiée pour] le péché, et où ils cuiront les gâteaux; afin qu'ils ne les emportent point au parvis extérieur pour en sanctifier le peuple.
Munthuyo anandiwuza kuti, “Awa ndi malo amene ansembe adzaphikirapo nsembe yopepesera kupalamula ndi nsembe yopepesera machimo. Kumenekonso azidzawotcherako chopereka cha chakudya. Sadzatuluka nazo zoyerazi mʼbwalo lakunja kuopa kuti angapatsireko kuyera anthu ena.”
21 Puis il me fit sortir vers le parvis extérieur, et me fit traverser vers les quatre coins du parvis, et voici, il y avait un parvis à chaque coin du parvis.
Pambuyo pake anandilowetsa mʼbwalo lakunja napita nane ku ngodya zinayi za bwalolo. Ndipo ndinaona mʼkati mwa ngodya iliyonse bwalo lina.
22 Tellement qu'aux quatre coins de ce parvis il y avait d'autres parvis qui y étaient joints, et ils étaient longs de quarante [coudées], et larges de trente; [et] tous quatre avaient une même mesure, [et] avaient leurs [quatre] coins.
Motero pa ngodya zinayi za bwalo panalinso mabwalo ena angʼonoangʼono. Mabwalo amenewa anali ofanana. Mulitali mwake munali mamita makumi awiri ndipo mulifupi mwake munali mamita khumi ndi asanu.
23 Tous ces quatre parvis avaient une rangée de bâtiments élevés tout à l'entour, et ce qui était bâti au dessous de ces rangées de bâtiment élevé, tout [à] l'entour, c'étaient des lieux propres à cuire.
Kuzungulira mabwalo anayi angʼonoangʼono aja panali mpanda wamiyala, ndi malo asonkhapo moto omangidwa mʼmunsi mwa mpandawo mozungulira.
24 Et il me dit: ce sont ici les cuisines, où ceux qui font le service de la maison cuiront les sacrifices du peuple.
Munthuyo anandiwuza kuti, “Izi ndi zipinda zophikiramo. Mʼmenemu anthu otumikira ku Nyumba ya Mulungu adzaphikiramo nyama za nsembe za anthu.”

< Ézéchiel 46 >