< Ézéchiel 45 >
1 Or quand vous partagerez au sort le pays en héritage, vous en lèverez une portion pour l'Eternel, [la lui présentant comme] en offrande élevée, [laquelle étant prise sur] la longueur du pays, sera sanctifiée d'entre toutes les autres portions du pays, et aura de longueur vingt-cinq mille [cannes], et de largeur, dix mille; ce sera une chose sainte dans tous ses confins à l'entour.
“‘Mukamadzagawa dziko kuti fuko lililonse lilandire cholowa chake, mudzapatuleko chigawo chimodzi kuti chikhale cha Yehova. Mulitali mwake mudzakhale makilomita khumi ndi awiri ndi theka ndipo mulifupi mwake makilomita khumi. Malo onsewo adzakhale opatulika.
2 De cette [portion] il y aura cinq cents [cannes] correspondantes à cinq cents autres cannes, mesurées en carré à l'entour, pour le lieu Saint, et cinquante coudées à l'entour pour ses faubourgs.
Mʼkati mwa chigawo chimenechi, malo a mamita 250 mbali iliyonse adzakhala malo a Nyumba ya Mulungu. Pozungulira pake ponse padzakhala malo a mamita 25.
3 Tu mesureras donc de cette mesure [l'espace du lieu Saint, savoir] de la longueur de vingt-cinq mille, et de la largeur de dix mille [cannes]; et le Sanctuaire, [et] le lieu Très-saint, sera dans cet [espace].
Mʼchigawo chopatulikacho muyeze malo a makilomita 12 ndi theka mulitali mwake, makilomita asanu mulifupi mwake. Pamenepo padzakhala malo opatulika kwambiri.
4 Cette [portion] sanctifiée [d'entre les autres] du pays appartiendra aux Sacrificateurs ministres du Sanctuaire, qui approchent de l'Eternel pour faire son service, et elle leur sera un lieu pour des maisons, et un Sanctuaire pour le Sanctuaire.
Malo opatulika amenewa adzakhalanso a ansembe amene amatumikira ku malo opatulika, amene amayandikira Yehova kuti amutumikire. Pamenepo padzakhala malo omangapo nyumba zawo ndi malo omangapo Nyumba ya Mulungu.
5 Puis il y aura vingt-cinq mille [autres cannes] en longueur, et dix mille en largeur, lesquelles appartiendront aux Lévites qui font le service de la maison, pour être leur possession, avec les vingt chambres.
Alevi otumikira ku Nyumba ya Mulungu adzakhala ndi malo a makilomita khumi ndi awiri ndi theka mulitali mwake ndi makilomita asanu mulifupi mwake. Kumeneko ndiko kudzakhale midzi yawo.
6 Puis vous donnerez pour la possession de la ville la largeur de cinq mille, et la longueur de vingt-cinq mille, suivant la proportion de la portion sanctifiée, qui aura été levée sur toute la masse; et cela sera pour toute la maison d'Israël.
“‘Moyandikana ndi malo opatulika, padzakhale malo a makilomita awiri ndi theka mulifupi mwake ndi makilomita khumi ndi awiri ndi theka mulitali mwake; kuti akhale malo a mzinda. Malo amenewa adzakhala a Aisraeli onse.
7 Puis [vous assignerez la portion] du Prince tant au delà de la portion sanctifiée qui aura été levée sur toute la masse, qu'au deçà de la possession de la ville, [savoir] tout le long de la portion sanctifiée qui aura été levée sur toute la masse, et tout le long de la possession de la ville, tirant depuis le canton de l'Occident, jusques à l'Occident, et depuis le canton qui regarde vers l'Orient, jusque vers l'Orient; tellement que [l'autre] longueur sera aux parties opposées à l'une des [autres] portions, [tirant] depuis les confins d'Occident vers les confins qui regardent vers l'Orient.
“‘Mfumu idzakhale ndi malo okhudzana ndi chigawo cha malo opatulika ndi cha mzinda. Malowo ayandikane ndi zigawozo chakummawa ndi chakumadzulo. Malowo atalike ngati chigawo chimodzi cha fuko la Israeli kuyambira ku malire akummawa mpaka ku malire akumadzulo.
8 Ce qui sera de toute cette terre-là appartiendra au [Prince] pour être possédé par lui au pays d'Israël; et les Princes que j'établirai ne fouleront plus mon peuple, mais ils distribueront le pays à la maison d'Israël, selon leurs Tribus.
Malowa adzakhala chigawo cha mfumu mu Israeli. Choncho mafumu anga sadzazunzanso anthu anga, koma adzidzalola Aisraeli kuti akhale ndi zigawo zawozawo.
9 Ainsi a dit le Seigneur l'Eternel: Princes d'Israël, qu'il vous suffise; ôtez la violence et le pillage, et faites jugement et justice; ôtez vos extorsions de dessus mon peuple, dit le Seigneur l'Eternel.
“‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Tsono pakwana, inu akalonga a Israeli. Lekani nkhanza zanu ndi kupondereza anthu anga. Muzitsata chilungamo ndi kuchita zokomera anthu. Musapirikitse anthu anga mʼdzikomo. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
10 Ayez la balance juste, et l'épha juste, et le bath juste.
Miyeso yanu yoyezera zinthu monga efa ndi bati zizikhala zokhulupirika.
11 L'épha et le bath seront de même mesure; tellement qu'on prendra un bath pour la dixième partie d'un homer, et l'épha sera la dixième partie d'un homer, la mesure de l'un et de l'autre se rapportera à l'homer.
Efa ndi bati ikhale miyeso yolingana kukula kwake. Muyeso wa homeri ukhale wokwanira mabati khumi, ukhalenso wokwanira maefa khumi. Ndiye kuti kukula kwa miyeso iwiriyo kuzidzatsata kukula kwa homeriyo.
12 Et le sicle sera de vingt oboles; [et] vingt sicles, vingt-cinq sicles, quinze sicles feront la mine.
Muyeso wa sekeli ukhale wokwanira magera makumi awiri. Muyeso wa mina ukhale wolemera masekeli 60.
13 C'est ici l'oblation que vous offrirez en offrande élevée; la sixième partie d'un épha d'un homer de blé; et vous donnerez la sixième partie d'un épha d'un homer d'orge.
“‘Zopereka zomwe mudzidzapereka ndi izi: chimodzi mwa zigawo 60 za tirigu, barelenso chimodzimodzi ndiponso gawo limodzi la magawo asanu ndi limodzi la efa, kulitapa pa barele wa homeri.
14 [Et parce que] le bath [est la mesure] pour l'huile, l'offrande ordonnée pour l'huile sera la dixième partie d'un bath pour core, [en tant que] dix baths feront un homer; car dix baths feront un homer.
Gawo loyenera la mafuta, loyezedwa ndi bati, ndiponso chigawo mwa zigawo 100 za mafuta. Miyeso yake ili motere: mabati khumi afanana ndi homeri imodzi kapena kori imodzi.
15 Pareillement l'offrande ordonnée des bêtes du menu bétail sera de deux cents l'une, même des meilleurs pâturages d'Israël; [toute laquelle oblation] sera employée en gâteaux, et en holocaustes, et en sacrifices de prospérité, afin de faire propitiation pour vous, dit le Seigneur l'Eternel.
Muperekenso nkhosa imodzi pa gulu lankhosa 200 za pa msipu wabwino wa mu Israeli. Izi zidzagwiritsidwa ntchito monga nsembe za chakudya, nsembe zopsereza, ndi nsembe zachiyanjano ndi nsembe zopepesera milandu ya anthu. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
16 Tout le peuple qui est du pays sera tenu à cette offrande élevée, pour celui qui sera Prince en Israël.
Anthu onse a mʼdzikomo azidzapereka zimenezi kwa mfumu ya Israeli.
17 Mais le Prince sera tenu de fournir les holocaustes, et les gâteaux, et les aspersions qu'il faudra offrir aux fêtes solennelles, aux nouvelles lunes et aux Sabbats, [et] dans toutes les solennités de la maison d'Israël. Il tiendra prêtes les bêtes qu'on sacrifiera pour le péché, et les gâteaux, et les bêtes qu'on sacrifiera pour l'holocauste, et les bêtes qu'on sacrifiera pour les sacrifices de prospérité, afin de faire propitiation pour la maison d'Israël.
Udzakhala udindo wa mfumu kupereka zofunikira ku nsembe zopsereza, nsembe za chakudya, ndi nsembe za zakumwa pa nthawi ya zikondwerero, chikondwerero cha mwezi watsopano ndi cha masabata, nthawi yonse ya zikondwerero zoyikika za Aisraeli. Mfumuyo idzapereka nsembe zopepesera machimo, nsembe za chakudya, nsembe zopsereza, ndi nsembe zachiyanjano kuti zikhale nsembe zopepesera machimo a Aisraeli.
18 Ainsi a dit le Seigneur l'Eternel: au premier mois, au premier [jour] du mois, tu prendras un jeune veau sans tare, et tu purifieras le Sanctuaire par ce sacrifice offert pour le péché.
“‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pa tsiku loyamba la mwezi woyamba muzitenga mwana wangʼombe wamwamuna wopanda chilema ndi kuchita mwambo woyeretsa malo opatulika.
19 Tellement que le Sacrificateur prendra du sang de ce [sacrifice offert pour le] péché, et en mettra sur les poteaux de la maison, et sur les quatre coins des saillies de l'autel, et sur les poteaux des portes des parvis intérieurs.
Wansembe atengeko magazi a nsembe yopepesera machimoyo ndipo awapake pa mphuthu za Nyumba ya Mulungu, pa ngodya zinayi za pamwamba pa guwa lansembe ndi pa mphuthu za pa chipata cha bwalo la mʼkati.
20 Tu en feras ainsi au septième jour du même mois, à cause des hommes qui pèchent par ignorance, et à cause des hommes simples; et vous ferez ainsi propitiation pour la maison.
Muzichita chimodzimodzi pa tsiku la chisanu ndi chiwiri la mwezi, kuchitira aliyense amene wachimwa mosafuna kapena mosadziwa. Motero Nyumba ya Mulungu idzakhala yoyera.
21 Au premier mois au quatorzième jour du mois, vous aurez la Pâque, fête solennelle qui durera sept jours, pendant lesquels on mangera des pains sans levain.
“‘Pa tsiku la 14 la mwezi woyamba muzichita chikondwerero cha Paska, chikondwerero chake cha masiku asanu ndi awiri. Pa masiku amenewo muzidzadya buledi wopanda yisiti.
22 Et en ce jour-là le Prince offrira un veau pour le péché, tant pour lui que pour tout le peuple du pays.
Pa tsiku loyamba la chikondwererocho, mfumu ipereke nsembe ya ngʼombe yayimuna monga nsembe yopepesera machimo ake ndi machimo a anthu onse a mʼdziko.
23 Pareillement durant les sept jours de cette fête solennelle, il offrira chaque jour sept veaux et sept béliers, sans tare, pour l'holocauste qu'on offrira à l'Eternel, et un bouc d'entre les chèvres [pour le sacrifice] pour le péché, chacun de ces sept jours-là.
Pa masiku asanu ndi awiri a chikondwererocho, mfumu ipereke kwa Yehova nsembe zopsereza izi: ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri, zonsezi zopanda chilema. Pa masikuwa mfumu iziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ngati nsembe yopepesera machimo.
24 Pareillement il offrira un épha pour le gâteau de chaque veau, et un épha [pour le gâteau] de chaque bélier, et un hin d'huile pour chaque épha.
Pamodzi ndi ngʼombe iliyonse yayimuna ndi nkhosa iliyonse yayimuna, mfumu ipereke chopereka cha chakudya chokwanira efa imodzi ndiponso mafuta okwanira hini imodzi pa efa iliyonse.
25 Au septième mois, le quinzième jour du mois, en la fête solennelle, il offrira durant sept jours les mêmes choses, [savoir] le même sacrifice pour le péché, le même holocauste, les mêmes gâteaux, et les mêmes mesures d'huile.
“‘Pa nthawi ya chikondwerero cha masiku asanu ndi awiri, chimene chimayamba pa tsiku la 15 la mwezi wachisanu ndi chiwiri, mfumuyo iziperekanso nsembe za mtundu womwewo: nsembe zopepesera machimo, nsembe zopsereza, nsembe za chakudya ndi za mafuta.’”