< Ézéchiel 4 >

1 Et toi, fils d'homme, prends-toi un tableau carré, et le mets devant toi, et traces-y la ville de Jérusalem.
Mulungu anati, “Iwe mwana wa munthu, tsopano tenga njerwa, uliyike pamaso pako ndipo ujambulepo chithunzi cha mzinda wa Yerusalemu.
2 Puis tu mettras le siège contre elle, tu bâtiras contre elle des forts, tu élèveras contre elle des terrasses, tu poseras des camps contre elle, et tu mettras autour d'elle des machines pour la battre.
Ndipo uwuzinge mzindawo motere: uwumangire nsanja zowuzinga, uwumbire mitumbira ya nkhondo, uwumangire misasa ya nkhondo ndipo uyike zida zogumulira kuzungulira mzindawo.
3 Tu prendras aussi une plaque de fer, et tu la mettras pour un mur de fer entre toi et la ville, et tu dresseras ta face contre elle, et elle sera assiégée, et tu l'assiégeras; ce sera un signe à la maison d'Israël.
Kenaka utenge chiwaya chachitsulo uchiyike ngati khoma lachitsulo pakati pa iwe ndi mzindawo. Uyangʼanitsitse mzindawo ndipo udzakhala wozingidwa ndi nsanja za nkhondo. Choncho umangire nsanja zankhondo. Chimenechi chidzakhala chizindikiro kwa Aisraeli.
4 Après tu dormiras sur ton côté gauche, et tu mettras sur lui l'iniquité de la maison d'Israël; selon le nombre des jours que tu dormiras sur ce [côté], tu porteras leur iniquité.
“Tsono iwe ugonere kumanzere kwako ndipo ndidzayika pa iwe tchimo la Aisraeli. Iwe udzasenza tchimolo masiku onse amene udzagonere mbali imeneyo.
5 Et je t'ai assigné les ans de leur iniquité selon le nombre des jours, [savoir] trois cent quatre-vingt-dix jours; ainsi tu porteras l'iniquité de la maison d'Israël.
Ine ndakuyikira masiku okwana 390 malingana ndi zaka za machimo awo. Umu ndi mmene udzasenzere machimo a Aisraeli.
6 Et quand tu auras accompli ces jours-là, tu dormiras la seconde fois sur ton côté droit, et tu porteras l'iniquité de la maison de Juda pendant quarante jours, un jour pour un an; [car] je t'ai assigné un jour pour un an.
“Utatha zimenezo udzagonerenso mbali ya kudzanja lamanja, ndipo udzasenza machimo a anthu a ku Yuda masiku makumi anayi, tsiku lililonse kuyimira chaka chimodzi.
7 Et tu dresseras ta face vers le siège ordonné contre Jérusalem, et ton bras sera retroussé; et tu prophétiseras contre elle.
Tsono udzayangʼanitsitse nsanja za nkhondo zozinga. Dzanja la mkanjo wako utalikwinya ndi dzanja lako utakweza, udzalosere modzudzula Yerusalemu.
8 Or voici j'ai mis sur toi des cordes, et tu ne te tourneras point de l'un de tes côtés à l'autre, jusqu'à ce que tu aies accompli les jours de ton siège.
Ine ndidzakumanga ndi zingwe kotero kuti sudzatha kutembenukira uku ndi uku mpaka utatsiriza masiku akuzingidwa ako.
9 Tu prendras aussi du froment, de l'orge, des fèves, des lentilles, du millet, et de l'épeautre, et tu les mettras dans un vaisseau, et t'en feras du pain selon le nombre des jours que tu dormiras sur ton côté; tu en mangeras pendant trois cent quatre-vingt-dix jours.
“Tsono tenga tirigu ndi barele, nyemba ndi mphodza, mapira ndi mchewere; ndipo uyike zonsezi mʼmbale imodzi ndipo upange buledi wako. Uzidya pa masiku 390 amene udzakhala ukugonera mbali imodzi.
10 Et la viande que tu mangeras sera du poids de vingt sicles par jour; et tu la mangeras depuis un temps jusqu'à l'autre temps.
Uyeze theka la kilogalamu la chakudyacho kuti uzidya tsiku lililonse kamodzi kokha.
11 Et tu boiras de l'eau par mesure, [savoir] la sixième partie d'un Hin; tu la boiras depuis un temps jusqu'à l'autre temps.
Uyezenso zikho ziwiri zamadzi ndipo uzimwa tsiku ndi tsiku.
12 Tu mangeras aussi des gâteaux d'orge, et tu les cuiras avec de la fiente sortie de l'homme, eux le voyant.
Uzidya chakudya chako ngati momwe amadyera keke ya barele. Uzidzaphika chakudyacho anthu akuona pogwiritsa ntchito ndowe ya munthu ngati nkhuni.”
13 Puis l'Eternel dit: les enfants d'Israël mangeront ainsi leur pain souillé parmi les nations vers lesquelles je les chasserai.
Yehova anati, “Chimodzimodzi anthu a Israeli adzadya chakudya chodetsedwa ku mayiko achilendo kumene Ine ndidzawapirikitsira.”
14 Et je dis: ah! ah! Seigneur Eternel, voici, mon âme n'a point été souillée, et je n'ai mangé d'aucune bête morte d'elle-même, ou déchirée [par les bêtes sauvages], depuis ma jeunesse jusqu'à présent; et aucune chair impure n'est entrée dans ma bouche.
Koma ine ndinati, “Zisatero, Ambuye Yehova! Ine sindinadziyipitsepo pa zachipembedzo. Kuyambira ubwana wanga mpaka tsopano, sindinadyepo kanthu kalikonse kopezeka katafa kapena kophedwa ndi zirombo za kutchire. Palibe nyama yodetsedwa pa zachipembedzo imene inalowa pakamwa panga.”
15 Et il me répondit: voici, je t'ai donné la fiente des bœufs, au lieu de la fiente de l'homme, et tu feras cuire ton pain avec cette fiente.
Iye anati, “Chabwino, ndidzakulola kuti uphike buledi wako ndi ndowe za ngʼombe mʼmalo mwa ndowe za munthu.”
16 Puis il me dit: fils d'homme, voici, je m'en vais rompre le bâton du pain dans Jérusalem; et ils mangeront leur pain à poids, et avec chagrin; et ils boiront l'eau par mesure, et avec étonnement;
Pambuyo pake anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, anthu a ku Yerusalemu ndidzawachepetsera chakudya. Anthuwo adzadya chakudya chochita kuyeza ndipo azidzadya mwa nkhawa. Azidzamwanso madzi ochita kuyeza ndiponso mwa mantha.
17 Parce que le pain et l'eau leur manqueront, et ils seront étonnés se regardant l'un l'autre, et ils fondront à cause de leur iniquité.
Ndidzachita zimenezi kuti adzasowe chakudya ndi madzi. Choncho adzachita nkhawa akumapenyana ndipo adzatheratu ndi kuwonda chifukwa cha machimo awo.”

< Ézéchiel 4 >