< Ézéchiel 35 >
1 La parole de l'Eternel me fut encore [adressée], en disant:
Yehova anandiyankhula kuti:
2 Fils d'homme, tourne ta face contre la montagne de Séhir, et prophétise contre elle.
“Iwe mwana wa munthu, yangʼana phiri la Seiri; yankhula moliyimba mlandu ndipo
3 Et lui dis: ainsi a dit le Seigneur l'Eternel: voici, j'en veux à toi, montagne de Séhir, et j'étendrai ma main contre toi, et te réduirai en désolation et en désert.
awawuze anthu a kumeneko kuti zimene ndikuyankhula Ine Ambuye Yehova ndi izi: Inu anthu a ku mapiri a Seiri ndikudana nanu. Ndidzatambasula dzanja langa kulimbana nanu, ndipo ndidzasandutsa dziko lanu kukhala chipululu.
4 Je réduirai tes villes en désert, et tu [ne] seras [que] désolation, et tu connaîtras que je suis l'Eternel.
Mizinda yanu ndidzayisandutsa mabwinja, ndipo dziko lanu lidzasanduka chipululu. Zikadzachitika izi mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
5 Parce que tu as eu une inimitié immortelle, et que tu as fait couler le sang des enfants d'Israël à coups d'épée, au temps de leur calamité, et au temps de leur iniquité, [qui en a été] la fin.
“Munali adani a Israeli nthawi zonse, ndipo munkalola kuti Aisraeli aphedwe pa nkhondo pa nthawi ya mavuto awo, pa nthawi imene chilango chawo chinafika pachimake.
6 C'est pourquoi je suis vivant, dit le Seigneur l'Eternel, que je te mettrai toute en sang, et le sang te poursuivra; parce que tu n'as point haï le sang, le sang aussi te poursuivra.
Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pali Ine wamoyo, ndithu ndidzakukanthani. Imfa idzakulondolani. Popeza sunadane nako kukhetsa magazi, imfa idzakulondola.
7 Et je réduirai la montagne de Séhir en désolation et en désert, et j'en éloignerai tous ceux qui la fréquentaient.
Phiri la Seiri ndidzalisandutsa chipululu ndipo ndidzapha onse amene amapita nabwerera kumeneko.
8 Et je remplirai ses montagnes de ses gens mis à mort; tes hommes tués par l'épée tomberont en tes coteaux, et en tes vallées, et en tous tes courants d'eaux.
Ndidzaza mapiri ake ndi mitembo. Ophedwa pa nkhondo adzagwera pa zitunda zanu, zigwa zanu ndi mʼmitsinje yanu yonse.
9 Je te réduirai en désolations éternelles, et tes villes ne seront plus habitées; et vous saurez que je suis l'Eternel.
Ndidzasandutsa dziko lanu kukhala chipululu mpaka muyaya, ndipo mʼmizinda yanu simudzakhalanso anthu. Zikadzachitika izi mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
10 Parce que tu as dit: les deux nations, et les deux pays seront à moi, et nous les posséderons, quoique l'Eternel ait été là.
“Inu munanena kuti, ‘Mitundu iwiri iyi ya anthu, Yuda ndi Israeli, pamodzi ndi mayiko awo omwe idzakhala yathu.’ Munanena chomwechi ngakhale kuti Ine Yehova ndinali momwemo.
11 A cause de cela, je suis vivant, dit le Seigneur l'Eternel, que j'agirai selon ton courroux, et selon ton envie que tu as exécutée, à cause de tes haines contre eux; et je serai connu entre eux quand je t'aurai jugé.
Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pali Ine wamoyo, ndithu ndidzachita nanu monga munachita ndi anthu a ku Yuda ndi Israeli poonetsa mkwiyo wanu, nsanje yanu ndi chidani chanu pa iwo. Ndikadzakulangani mudzandidziwadi pakati panupo.
12 Et tu sauras que moi l'Eternel j'ai ouï toutes les paroles insultantes que tu as prononcées contre les montagnes d'Israël, en disant: elles ont été désolées, elles nous ont été données pour les consumer.
Ndipo mudzadziwa kuti Ine Yehova ndinamva mawu anu onse onyoza amene munanena molimbana ndi mapiri a Israeli. Inu munati, ‘Mapiri a Israeli asanduka bwinja, ndipo aperekedwa kwa ife kuti tiwawononge.’
13 Et vous m'avez bravé par vos discours, et vous avez multiplié vos paroles contre moi; je l'ai ouï.
Mawu anu amene munayankhula monyada kundinyoza Ine ndinawamva.
14 Ainsi a dit le Seigneur l'Eternel: quand toute la terre se réjouira, je te réduirai en désolation.
Ine Ambuye Yehova ndikuti: Dziko lonse lapansi lidzasangalala pamene ndidzakusandutsani bwinja.
15 Comme tu t'es réjouie sur l'héritage de la maison d'Israël, parce qu'il a été désolé, j'en ferai de même envers toi; tu ne seras que désolation, ô montagne de Séhir! même tout Edom entièrement; et ils sauront que je suis l'Eternel.
Monga momwe inu munasangalala pamene anthu anga Aisraeli anagwa, Inenso ndidzakuchitani chimodzimodzi. Udzasanduka bwinja, iwe Phiri la Seiri, iwe ndi dziko lonse la Edomu. Zikadzatero anthu onse adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”