< Ézéchiel 25 >
1 Puis la parole de l'Eternel me fut [adressée], en disant:
Yehova anandiyankhula kuti:
2 Fils d'homme, tourne ta face vers les enfants de Hammon, et prophétise contre eux.
“Iwe mwana wa munthu, tembenukira anthu a ku Amoni ndipo unenere mowadzudzula.
3 Et dis aux enfants de Hammon: écoutez la parole du Seigneur l'Eternel. Parce que vous avez dit: ha! ha! contre mon Sanctuaire, à cause qu'il était profané; et contre la terre d'Israël, parce qu'elle était désolée; et contre la maison de Juda, parce qu'ils allaient en captivité;
Awawuze kuti, ‘Inu anthu a ku Amoni, imvani zimene Ambuye Yehova akunena. Iye akuti: Inu munanena mawu onyoza pamene Nyumba yanga yopatulika inkayipitsidwa. Munanyozanso dziko la Israeli pamene linaguga ndiponso anthu a ku Yuda pamene anatengedwa ukapolo.
4 A cause de cela voici, je m'en vais te donner en héritage aux enfants d'Orient, et ils bâtiront des palais dans tes villes, et ils demeureront chez toi; ils mangeront tes fruits et boiront ton lait.
Nʼchifukwa chake Ine ndidzakuperekani mʼmanja mwa anthu akummawa ngati cholowa chawo. Iwo adzamanga misasa yawo ndi kukhoma matenti awo pakati panu. Adzadya zipatso zanu ndi kumwa mkaka wanu.
5 Et je livrerai Rabba pour être le repaire des chameaux, et [le pays] des enfants de Hammon pour être le gîte des brebis; et vous saurez que je suis l'Eternel.
Ndidzasandutsa Raba kuti akhale busa la ngamira ndi mizinda ya Aamoni kuti ikhale makola a nkhosa. Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
6 Car ainsi a dit le Seigneur l'Eternel: parce que tu as frappé des mains, et que tu as battu des pieds, et que tu t'es réjouie de bon cœur dans tout le mépris que tu as eu pour la terre d'Israël.
Zimene ndikunena Ine Ambuye Yehova ndi izi: Inu munawomba mʼmanja ndi kumalumphalumpha. Munkakondwa mu mtima mwanu pamene munkanyoza dziko la Israeli.
7 A cause de cela voici, j'ai étendu ma main sur toi, et je te livrerai pour être pillée par les nations, et je te retrancherai d'entre les peuples, je te ferai périr d'entre les pays; je te détruirai; et tu sauras que je suis l'Eternel.
Nʼchifukwa chake ndidzatambasula dzanja langa kuti ndikulangeni, ndipo ndidzakuperekani kuti mukhale chofunkha cha anthu a mitundu ina. Ndidzakuchotsani pakati pa anthu a mitundu ina ndi kukufafanizani mʼmayiko onse. Ndidzakuwonongani, ndipo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova!’”
8 Ainsi a dit le Seigneur l'Eternel: parce que Moab et Séhir ont dit: voici, la maison de Juda est comme toutes les autres nations.
“Ambuye Yehova akuti, ‘Anthu a ku Mowabu ndi a ku Seiri ananena kuti anthu a ku Yuda ali ngati mayiko ena onse.’
9 A cause de cela voici, je m'en vais ouvrir le quartier de Moab du côté des villes, du côté, dis-je, de ses villes frontières, la noblesse du pays de Bethjésimoth, de Bahal-Méhon et de Kirjathajim,
Nʼchifukwa chake ndidzagumula mbali ina ya Mowabu, kuyambira ku mizinda yake ya kumalire; mizinda yokongola ya Beti-Yesimoti, Baala-Meoni ndi Kiriataimu.
10 Aux enfants d'Orient, qui sont au delà du pays des enfants de Hammon, lequel je leur ai donné en héritage, afin qu'on ne se souvienne plus des enfants de Hammon parmi les nations.
Ndidzapereka Amowabu pamodzi ndi Aamoni mʼmanja mwa anthu akummawa kotero kuti Aamoni adzayiwalikiratu pakati pa anthu a mitundu ina.
11 J'exercerai aussi des jugements contre Moab, et ils sauront que je suis l'Eternel.
Ndidzawalangadi Amowabuwo. Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
12 Ainsi a dit le Seigneur l'Eternel: à cause de ce qu'Edom a fait quand il s'est inhumainement vengé de la maison de Juda, et parce qu'il s'est rendu fort coupable en se vengeant d'eux.
“Ambuye Yehova akuti, ‘Pakuti Edomu analipsira Ayuda, ndiye kuti analakwa kwambiri pochita zimenezi.
13 A cause de cela, le Seigneur l'Eternel dit ainsi: j'étendrai ma main sur Edom, j'en retrancherai les hommes et les bêtes, et je le réduirai en désert; depuis Théman et de devers Dédan ils tomberont par l'épée.
Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzatambasula dzanja langa kulanga Edomu ndi kupha anthu ake ndiponso nyama zawo. Ndidzawonongeratu Edomu ndipo adzaphedwa ndi lupanga kuchokera ku Temani mpaka ku Dedani.
14 J'exercerai ma vengeance sur Edom à cause de mon peuple d'Israël, et on traitera Edom selon ma colère, et selon ma fureur, et ils sentiront ce que c'est que de ma vengeance, dit le Seigneur l'Eternel.
Ndidzalanga Edomu ndi dzanja la anthu anga Aisraeli. Adzalanga anthu a ku Edomu molingana ndi mkwiyo ndi ukali wanga. Choncho adzaona kulipsira kwanga akutero Ambuye Yehova.’”
15 Ainsi a dit le Seigneur l'Eternel: à cause que les Philistins ont agi par vengeance, et qu'ils se sont inhumainement vengés avec plaisir [et] avec mépris, jusqu'à [tout] détruire par une inimitié immortelle;
“Ambuye Yehova akuti, ‘Afilisti analanga anthu anga mwankhanza ndi kuwalipsira.
16 A cause de cela le Seigneur l'Eternel dit ainsi: voici, je m'en vais étendre ma main sur les Philistins, j'exterminerai les Kéréthiens, et je ferai périr le reste de [leurs] ports de mer.
Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzatambasula dzanja langa kukantha Afilistiwo. Ndidzafafaniza Akereti ndi kuwononga iwo amene amakhala mʼmbali mwa nyanja.
17 Et je déploierai sur eux de grandes vengeances par des châtiments de fureur; et ils sauront que je suis l'Eternel, quand j'aurai exécuté sur eux ma vengeance.
Ndidzawabwezera chilango choopsa ndipo ndidzawalanga mu mkwiyo wanga. Ndikadzawalipsira ndipo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’”