< Exode 8 >
1 Après cela l'Eternel dit à Moïse: va vers Pharaon, et lui dis: ainsi a dit l'Eternel: laisse aller mon peuple, afin qu'ils me servent.
Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Ukamuwuze Farao kuti, Lolani anthu anga kuti apite, akandipembedze.
2 Que si tu refuses de le laisser aller, voici, je m'en vais frapper de grenouilles toutes tes contrées.
Ndipo ngati simulola kuti apite Ine ndidzalanga dziko lonse la Igupto polidzaza ndi achule.
3 Et le fleuve fourmillera de grenouilles, qui monteront et entreront dans ta maison, et dans la chambre où tu couches, et sur ton lit, et dans la maison de tes serviteurs, et parmi tout ton peuple, dans tes fours, et dans tes maies.
Mtsinje wa Nailo udzadzaza ndi achule. Achulewo adzatuluka ndi kukalowa mʼnyumba yaufumu, ku chipinda chogona ndi pa bedi lako, mʼnyumba za nduna zako ndi pa anthu ako ndi mophikira buledi ndiponso mopangira bulediyo.
4 Ainsi les grenouilles monteront sur toi, sur ton peuple, et sur tous tes serviteurs.
Achulewo adzakulumphira iwe ndi anthu ako ndiponso nduna zako.”
5 L'Eternel donc dit à Moïse: dis à Aaron: étends ta main avec ta verge sur les fleuves, sur les rivières, et sur les marais, et fais monter les grenouilles sur le pays d'Egypte.
Ndipo Yehova anati kwa Mose, “Uza Aaroni kuti, ‘Loza ndodo yako ku mitsinje, ku ngalande ndi ku zithaphwi ndipo pakhale achule pa dziko lonse la Igupto.’”
6 Et Aaron étendit sa main sur les eaux de l'Egypte, et les grenouilles montèrent, et couvrirent le pays d'Egypte.
Kotero Aaroni analoza dzanja lake pa madzi a ku Igupto, ndipo achule anatuluka nadzaza dziko lonse la Igupto.
7 Mais les magiciens firent de même par leurs enchantements, et firent monter des grenouilles sur le pays d'Egypte.
Koma amatsenga anachita zinthu zomwezo mʼmatsenga awo. Iwonso anatulutsa achule mʼdziko lonse la Igupto.
8 Alors Pharaon appela Moïse et Aaron, et leur dit: fléchissez l'Eternel par [vos] prières, afin qu'il retire les grenouilles de dessus moi et de dessus mon peuple; et je laisserai aller le peuple, afin qu'ils sacrifient à l'Eternel.
Kenaka, Farao anayitanitsa Mose ndi Aaroni ndipo anati, “Pemphera kwa Yehova kuti achulewa achoke kwa ine ndi anthu anga, ndipo ine ndidzalola kuti anthu anu apite kukapereka nsembe kwa Yehova.”
9 Et Moïse dit à Pharaon: glorifie-toi sur moi. Pour quel temps fléchirai-je par mes prières [l'Eternel] pour toi et pour tes serviteurs, et pour ton peuple, afin qu'il chasse les grenouilles loin de toi, et de tes maisons? Il en demeurera seulement dans le fleuve.
Mose anati kwa Farao, “Inu mungonditchulira nthawi imene mukufuna kuti ndikupempherereni, nduna zanu pamodzi ndi anthu anu kuti achule achoke mʼnyumba zanu ndi kuti atsale okhawo ali mu mtsinje wa Nailo.”
10 Alors il répondit: pour demain. Et [Moïse] dit: [il sera fait] selon ta parole, afin que tu saches qu'il n'y a nul [Dieu] tel que l'Eternel notre Dieu.
Farao anati, “Mawa.” Mose anamuyankha kuti, “Chabwino zidzakhala monga mwaneneramu, kuti mudzadziwe kuti palibe wina wofanana ndi Yehova Mulungu wathu.
11 Les grenouilles donc se retireront de toi, et de tes maisons, et de tes serviteurs, et de ton peuple; il en demeurera seulement dans le fleuve.
Achule adzachoka mʼnyumba yanu, mʼnyumba za nduna zanu pamodzi ndi za anthu anu. Koma adzatsala mu mtsinje wa Nailo basi.”
12 Alors Moïse et Aaron sortirent d'avec Pharaon; et Moïse cria à l'Eternel au sujet des grenouilles qu'il avait fait venir sur Pharaon.
Mose ndi Aaroni anachoka, ndipo Mose anapemphera kwa Yehova kuti achotse achule amene anatumiza kwa Farao.
13 Et l'Eternel fit selon la parole de Moïse. Ainsi les grenouilles moururent; et il n'y en eut plus dans les maisons, ni dans les villages, ni à la campagne.
Ndipo Yehova anachita zomwe Mose anapempha. Achule amene anali mʼnyumba, mʼmabwalo ndi mʼminda anafa
14 Et on les amassa par monceaux, et la terre en fut infectée.
Aigupto anawunjika achulewo milumilu ndipo dziko linanunkha.
15 Mais Pharaon voyant qu'il avait du relâche, endurcit son cœur, et ne les écouta point, selon que l'Eternel [en] avait parlé.
Koma Farao ataona kuti zinthu zinayambanso kukhala bwino, anawumitsanso mtima wake ndipo sanamverenso mawu a Mose ndi Aaroni, monga momwe Yehova ananenera.
16 Et l'Eternel dit à Moïse: dis à Aaron: étends ta verge, et frappe la poussière de la terre, et elle deviendra des poux par tout le pays d'Egypte.
Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Uza Aaroni kuti akweze ndodo yake ndi kumenya fumbi la pa nthaka, ndipo fumbilo lidzasanduka nsabwe pa dziko lonse la Igupto.”
17 Et ils firent ainsi. Et Aaron étendit sa main avec sa verge, et frappa la poussière de la terre, et elle devint des poux, sur les hommes, et sur les bêtes; toute la poussière du pays devint des poux en tout le pays d'Egypte.
Iwo anachita momwemo, ndipo pamene Aaroni anakweza ndodo yake ndi kumenya fumbi, nsabwe zinafika pa munthu aliyense ndi pa ziweto. Fumbi lonse la mʼdziko la Igupto linasanduka nsabwe.
18 Et les magiciens voulurent faire de même par leurs enchantements, pour produire des poux, mais ils ne purent. Les poux furent donc tant sur les hommes que sur les bêtes.
Koma amatsenga atayesa kupanga nsabwe mwa matsenga awo, analephera. Ndipo nsabwezo zinali pa munthu aliyense ndi pa ziweto zawo.
19 Alors les magiciens dirent à Pharaon: c'est ici le doigt de Dieu. Toutefois le cœur de Pharaon s'endurcit et il ne les écouta point, selon que l'Eternel [en] avait parlé.
Amatsenga anati kwa Farao, “Izi wachita ndi Mulungu.” Koma mtima wa Farao unali wowumabe ndipo sanamvere zonena za Mose ndi Aaroni monga momwe Yehova ananenera.
20 Puis l'Eternel dit à Moïse: lève-toi de bon matin, et te présente devant Pharaon; voici, il sortira vers l'eau, et tu lui diras: ainsi a dit l'Eternel: laisse aller mon peuple, afin qu'ils me servent.
Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Mmawa, upite ukakumane ndi Farao maso ndi maso pamene azidzapita ku madzi ndipo ukanene kuti, ‘Yehova akuti, Lola anthu anga kuti apite akandipembedze.
21 Car si tu ne laisses pas aller mon peuple, voici, je m'en vais envoyer contre toi, contre tes serviteurs, contre ton peuple, et contre tes maisons, un mélange d'insectes; et les maisons des Egyptiens seront remplies de ce mélange, et la terre aussi sur laquelle ils seront.
Koma ngati suwalola anthu anga kuti apite, Ine ndidzatumiza pa iwe ntchentche zoluma ndi pa nduna zako ndi anthu ako ndi mʼnyumba zanu. Mʼnyumba za Aigupto mudzadzaza ntchentche zoluma. Ngakhale pa nthaka pamene akhalapo padzadzaza ndi ntchentche zoluma.’”
22 Mais je distinguerai en ce jour-là le pays de Goscen, où se tient mon peuple, tellement qu'il n'y aura nul mélange d'insectes, afin que tu saches que je [suis] l'Eternel au milieu de la terre.
“Koma pa tsikulo ndidzapatula dera la Goseni, kumene kumakhala anthu anga, motero kuti sikudzakhala ntchentche zoluma. Choncho iwe udzadziwa kuti Ine Yehova ndi amene ndikulamulira dziko lino.
23 Et je mettrai de la différence entre ton peuple et mon peuple; demain ce signe-là se fera.
Ndidzasiyanitsa pakati pa anthu anga ndi anthu ako. Chizindikiro chozizwitsa ichi chidzachitika mawa.”
24 Et l'Eternel [le] fit ainsi; et un grand mélange d'insectes entra dans la maison de Pharaon, et dans chaque maison de ses serviteurs, et dans tout le pays d'Egypte, [de sorte que] la terre fut gâtée par ce mélange.
Ndipo Yehova anachita zimenezi: Ntchentche zoluma zochuluka zinalowa mʼnyumba yaufumu ya Farao ndi nyumba za nduna zake. Choncho ntchentche zolumazi zinawononga dziko lonse la Igupto.
25 Et Pharaon appela Moïse et Aaron, et [leur] dit: allez, sacrifiez à votre Dieu dans ce pays.
Kenaka Farao anayitanitsa Mose ndi Aaroni nati, “Pitani kaperekeni nsembe kwa Mulungu wanu mʼdziko lomwe lino.”
26 Mais Moïse dit: il n'est pas à propos de faire ainsi; car nous sacrifierions à l'Eternel notre Dieu l'abomination des Egyptiens. Voici, si nous sacrifions l'abomination des Égyptiens devant leurs yeux, ne nous lapideraient-ils pas?
Koma Mose anati, “Sitingathe kutero pakuti nsembe zathu kwa Yehova Mulungu ndi zowayipira Aigupto. Ngati tipereke nsembe zowayipira Aigupto mʼmaso mwawo, adzatiponya miyala kuti tife.
27 Nous irons le chemin de trois jours au désert, et nous sacrifierons à l'Eternel notre Dieu, comme il nous dira.
Ife tiyenera kuyenda ulendo wa masiku atatu kupita ku chipululu kukapereka nsembe kwa Yehova Mulungu wathu monga anatilamulira.”
28 Alors Pharaon dit: je vous laisserai aller pour sacrifier dans le désert à l'Eternel votre Dieu; toutefois vous ne vous éloignerez nullement en vous en allant. Fléchissez [l'Eternel] pour moi par vos prières.
Farao anati, “Ine ndikulolani kuti mupite ku chipululu kukapereka nsembe kwa Yehova Mulungu wanu, koma musapite kutali kwambiri. Tsopano ndipempherereni.”
29 Et Moïse dit: voici, je sors d'avec toi, et je fléchirai par prières l'Eternel, afin que le mélange d'insectes se retire demain de Pharaon, de ses serviteurs, et de son peuple. Mais que Pharaon ne continue point à se moquer, en ne laissant point aller le peuple pour sacrifier à l'Eternel.
Mose anayankha kuti, “Ine ndikangochoka pano, ndikapemphera kwa Yehova ndipo mawa lomweli ntchentche zoluma zidzachoka kwa Farao, nduna zake pamodzi ndi anthu ake. Koma Farao, onetsetsani kuti musachitenso zachinyengo ndi kuwakaniza anthu kuti asakapereke nsembe kwa Yehova.”
30 Alors Moïse sortit d'avec Pharaon, et fléchit l'Eternel par prières.
Choncho Mose anasiyana ndi Farao nakapemphera kwa Yehova.
31 Et l'Eternel fit selon la parole de Moïse; et le mélange d'insectes se retira de Pharaon, et de ses serviteurs, et de son peuple; il ne resta pas un seul [insecte].
Ndipo Yehova anachita zomwe Mose anapempha: Ntchentche zoluma zinachoka kwa Farao ndi nduna zake ndiponso kwa anthu ake. Palibe ngakhale imodzi yomwe inatsala.
32 Mais Pharaon endurcit son cœur encore cette fois, et ne laissa point aller le peuple.
Koma nthawi imeneyinso Farao anawumitsa mtima wake ndipo sanalole kuti anthu atuluke.