< Exode 6 >
1 Et l'Eternel dit à Moïse: tu verras maintenant ce que je ferai à Pharaon; car il les laissera aller, y [étant contraint] par main forte, [étant, dis-je, contraint] par main forte, il les chassera de son pays.
Yehova anawuza Mose kuti, “Tsopano udzaona zimene ndimuchite Farao: Chifukwa cha dzanja langa lamphamvu adzalola anthu anga kuti atuluke. Chifukwa cha dzanja langa lamphamvu adzawatulutsa mʼdziko lake.”
2 Dieu parla encore à Moïse, et lui dit: je suis l'Eternel.
Mulungu anatinso kwa Mose, “Ine ndine Yehova.
3 Je suis apparu à Abraham, à Isaac, et à Jacob, comme le [Dieu] Fort, Tout-puissant, mais je n'ai point été connu d'eux par mon nom d'Eternel.
Ndinaonekera kwa Abrahamu, kwa Isake ndi kwa Yakobo monga Mulungu Wamphamvuzonse, koma sindinawadziwitse dzina langa kuti ndine Yehova.
4 J'ai fait [aussi] cette alliance avec eux, que je leur donnerai le pays de Chanaan, le pays de leurs pèlerinages, dans lequel ils ont demeuré comme étrangers.
Ndinakhazikitsa pangano langa ndi iwo kuwalonjeza kuti ndidzawapatsa dziko la Kanaani kumene anakhalako kale ngati alendo.
5 Et j'ai entendu les sanglots des enfants d'Israël, que les Egyptiens tiennent esclaves, et je me suis souvenu de mon alliance.
Ndamvanso kubuwula kwa Aisraeli, amene Aigupto awayesa akapolo ndipo ndakumbukira pangano langa.”
6 C'est pourquoi dis aux enfants d'Israël: je suis l'Eternel, et je vous retirerai de dessous les charges des Egyptiens, et je vous délivrerai de leur servitude, je vous rachèterai à bras étendu, et par de grands jugements.
“Nʼchifukwa chake nena kwa Aisraeli kuti, ‘Ine ndine Yehova, ndipo ndidzakutulutsani mʼgoli la Aigupto. Ndidzakumasulani mu ukapolo, ndidzakuwombolani ndi dzanja langa lotambasuka ndi kuchita ntchito zachiweruzo.
7 Et je vous prendrai pour être mon peuple, je vous serai Dieu, et vous connaîtrez que je suis l'Eternel votre Dieu, qui vous retire de dessous les charges des Égyptiens.
Ndidzakutengani kukhala anthu anga, ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wanu. Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu amene ndinakutulutsani mʼgoli la Aigupto.
8 Et je vous ferai entrer au pays touchant lequel j'ai levé ma main, que je le donnerais à Abraham, à Isaac, et à Jacob, et je vous le donnerai en héritage: Je suis l'Eternel.
Ndipo ndidzakufikitsani ku dziko limene ndinalumbira kuti ndidzalipereka kwa Abrahamu, kwa Isake ndi kwa Yakobo. Ndidzakupatsani dziko limenelo kuti likhale lanu. Ine ndine Yehova.’”
9 Moïse donc parla en cette manière aux enfants d'Israël. Mais ils n'écoutèrent point Moïse, à cause de l'angoisse de leur esprit, et à cause de leur dure servitude.
Mose anawafotokozera Aisraeli zimenezi, koma iwo sanamumvere chifukwa cha kukhumudwa ndi goli lankhanza.
10 Et l'Eternel parla à Moïse, en disant:
Kenaka Yehova anati kwa Mose,
11 Va, et dis à Pharaon Roi d'Egypte, qu'il laisse sortir les enfants d'Israël de son pays.
“Pita ukawuze Farao mfumu ya Igupto kuti awalole Aisraeli atuluke mʼdziko lake.”
12 Alors Moïse parla devant l'Eternel, en disant: voici, les enfants d'Israël ne m'ont point écouté, et comment Pharaon m'écoutera-t-il, moi, qui suis incirconcis de lèvres?
Koma Mose ananena kwa Yehova kuti, “Ngati Aisraeli sanandimvere, Farao akandimvera chifukwa chiyani, pajatu sinditha kuyankhula bwino?”
13 Mais l'Eternel parla à Moïse et à Aaron, et leur commanda [d'aller trouver] les enfants d'Israël, et Pharaon Roi d'Egypte, pour retirer les enfants d'Israël du pays d'Egypte.
Ndipo Yehova analamula Mose ndi Aaroni kuti awuze Aisraeli ndi Farao mfumu ya Igupto kuti Aisraeli ayenera kutuluka mʼdziko la Igupto.
14 Ce sont ici les Chefs des maisons de leurs pères: Les enfants de Ruben, premier-né d'Israël, Hénoc et Pallu, Hetsron et Carmi; ce [sont] là les familles de Ruben.
Atsogoleri a mafuko awo anali awa: Ana a Rubeni mwana wachisamba wa Israeli anali Hanoki, Palu, Hezironi ndi Karimi. Awa anali mafuko a Rubeni.
15 Et les enfants de Siméon, Jémuel, Jamin, Ohad, Jakin, Tsohar, et Saül, fils d'une Chananéenne; ce sont là les familles de Siméon.
Ana a Simeoni anali Yemueli, Yamini, Ohadi, Yakini, Zohari ndi Saulo mwana wa kwa mkazi wa Chikanaani. Awa anali mafuko a Simeoni.
16 Et ce sont ici les noms des enfants de Lévi selon leur naissance: Guerson, Kéhath et Mérari. Et les années de la vie de Lévi furent cent trente-sept.
Mayina a ana a Levi pamodzi ndi zidzukulu zawo anali awa: Geresoni, Kohati ndi Merari. Levi anakhala ndi moyo kwa zaka 137.
17 Les enfants de Guerson, Libni et Simhi, selon leurs familles.
Ana a Geresoni, mwa mafuko awo, anali Libini ndi Simei.
18 Et les enfants de Kéhath, Hamram, Jitshar, Hébron, et Huziel. Et les années de la vie de Kéhath furent cent trente-trois.
Ana a Kohati anali Amramu, Izihari, Hebroni ndi Uzieli. Kohati anakhala ndi moyo zaka 133.
19 Et les enfants de Mérari, Mahli et Musi; ce sont là les familles de Lévi selon leurs générations.
Ana a Merari anali Mali ndi Musi. Awa anali mafuko a Levi monga mwa mibado yawo.
20 Or Hamram prit Jokébed sa tante pour femme, qui lui enfanta Aaron et Moïse; et les années de la vie de Hamram furent cent trente-sept.
Amramu anakwatira Yokobedi mlongo wa abambo ake, amene anabereka Aaroni ndi Mose. Amramu anakhala ndi moyo kwa zaka 137.
21 Et les enfants de Jitshar, Coré, Népheg, et Zicri.
Ana a Izihari anali Kora, Nefegi ndi Zikiri.
22 Et les enfants de Huziel, Misaël, Eltsaphan, et Sithri.
Ana a Uzieli anali Misaeli, Elizafani ndi Sitiri.
23 Et Aaron prit pour femme Elisébah, fille de Hamminadab, sœur de Nahasson, qui lui enfanta Nadab, Abihu, Eléazar, et Ithamar.
Aaroni anakwatira Eliseba, mwana wamkazi wa Aminadabu, mlongo wa Nasoni ndipo Iye anabereka Nadabu, Abihu, Eliezara ndi Itamara.
24 Et les enfants de Coré, Assir, Elkana, et Abiasaph. Ce sont là les familles des Corites.
Ana a Kora anali Asiri, Elikana ndi Abiasafu. Awa ndiwo mafuko a Kora.
25 Mais Eléazar fils d'Aaron prit pour femme une des filles de Puthiel, qui lui enfanta Phinées. Ce sont là les Chefs des pères des Lévites selon leurs familles.
Eliezara mwana wa Aaroni anakwatira mmodzi mwa ana aakazi a Putieli, ndipo anabereka Finehasi. Awa anali atsogoleri a mabanja a Levi, monga mwa mafuko awo.
26 [Or c'est là cet Aaron et ce Moïse auxquels l'Eternel dit: retirez les enfants d'Israël du pays d'Egypte selon leurs bandes.
Aaroni ndi Mose ndi aja amene Yehova anawawuza kuti, “Tulutsani Aisraeli mu Igupto mʼmagulu awo.”
27 Ce sont eux qui parlèrent à Pharaon Roi d'Egypte, pour retirer d'Egypte les enfants d'Israël. C'est ce Moïse, et c'est cet Aaron.
Mose ndi Aaroni ndiwo amene anayankhula ndi Farao mfumu ya Igupto kuti atulutse Aisraeli mu Igupto.
28 Il arriva donc le jour que l'Eternel parla à Moïse au pays d'Egypte,
Tsopano pamene Yehova anayankhula kwa Mose mu Igupto,
29 Que l'Eternel parla à Moïse, en disant: je suis l'Eternel; dis à Pharaon Roi d'Egypte toutes les paroles que je t'ai dites.
anati, “Ine ndine Yehova. Umuwuze Farao mfumu ya Igupto zonse zimene Ine ndikuwuze iwe.”
30 Et Moïse dit devant l'Eternel: voici, je suis incirconcis de lèvres, et comment Pharaon m'écoutera-t-il?
Koma Mose anati kwa Yehova, “Farao akandimvera bwanji, pakuti ine sinditha kuyankhula bwino?”