< Exode 28 >
1 Et toi fais approcher de toi Aaron ton frère, et ses fils avec lui, d'entre les enfants d'Israël, pour m'exercer la Sacrificature, [savoir] Aaron, et Nadab, Abihu, Eléazar et Ithamar, fils d'Aaron.
“Aaroni mʼbale wako ndi ana ake aamuna, Nadabu, Abihu, Eliezara ndi Itamara uwapatule pakati pa Aisraeli. Abwere kwa iwe kuti anditumikire monga ansembe.
2 Et tu feras à Aaron ton frère de saints vêtements pour gloire et pour ornement.
Umusokere mʼbale wako, Aaroni, zovala zopatulika kuti azioneka mwaulemerero ndi molemekezeka.
3 Et tu parleras à tous les hommes d'esprit, à chacun de ceux que j'ai remplis de l'esprit de science, afin qu'ils fassent des vêtements à Aaron pour le sanctifier, afin qu'il m'exerce la Sacrificature.
Uwawuze anthu onse aluso amene Ine ndawapatsa nzeru pa ntchito yosoka kuti apange zovala za Aaroni za pa mwambo womupatula, kuti iye anditumikire monga wansembe.
4 Et ce sont ici les vêtements qu'ils feront; le Pectoral, l'Ephod, le Rochet, la Tunique, qui tienne serré, la Tiare, et le Baudrier; ils feront donc les saints vêtements à Aaron ton frère, et à ses fils, pour m'exercer la Sacrificature.
Zovala zoti apange ndi izi: chovala chapachifuwa, efodi, mkanjo, mwinjiro wolukidwa, nduwira ndi lamba. Apangire mʼbale wako Aaroni ndi ana ake aamuna zovala zopatulikazi kuti iwo anditumikire monga ansembe.
5 Et ils prendront de l'or, de la pourpre, de l'écarlate, du cramoisi, et du fin lin.
Iwo agwiritse ntchito golide, nsalu yamtundu wa mtambo, yapepo, yofiira ndi yosalala yofewa.
6 Et ils feront l'Ephod d'or, de pourpre, d'écarlate, de cramoisi, et de fin lin retors, d'un ouvrage exquis.
“Apange efodi pogwiritsa ntchito golide, nsalu yamtundu wa mtambo, yapepo ndi yofiira yolukidwa mwaluso.
7 Il aura deux épaulières qui se joindront par les deux bouts, et il sera [ainsi] joint.
Efodiyo ikhale ndi timalamba tiwiri ta pa mapewa tosokerera ku msonga zake ziwiri kuti azitha kumanga.
8 Le ceinturon exquis dont il sera ceint, [et] qui sera par-dessus, sera de même ouvrage, et tiré de lui, [étant] d'or, de pourpre, d'écarlate, de cramoisi, et de fin lin retors.
Lamba womangira efodi akhale wolukidwa mwaluso ngati efodiyo. Akhale wopangidwa ndi golide, nsalu yamtundu wa mtambo, yapepo, yofiira, yofewa yosalala.
9 Et tu prendras deux pierres d'Onyx, et tu graveras sur elles les noms des enfants d'Israël;
“Utenge miyala iwiri ya onikisi ndipo uzokotepo mayina a ana a Israeli.
10 Six de leurs noms sur une pierre et les six noms des autres, sur l'autre pierre, selon leur naissance.
Mayina asanu ndi limodzi akhale pa mwala umodzi, ndipo mayina asanu ndi limodzi pa mwala winawo motsata mabadwidwe awo.
11 Tu graveras sur les deux pierres, d'ouvrage de lapidaire, de gravure de cachet, les noms des enfants d'Israël, et tu les enchâsseras dans des chatons d'or.
Mayina a ana a Israeli uwazokote pa miyala iwiriyo, monga momwe amachitira mmisiri wozokota miyala. Ndipo uyike miyalayo mu zoyikamo zake zagolide.
12 Et tu mettras les deux pierres sur les épaulières de l'Ephod, afin qu'elles soient des pierres de mémorial pour les enfants d'Israël; car Aaron portera leurs noms sur ses deux épaules devant l'Eternel, pour mémorial.
Umangirire miyala iwiriyi pa tinsalu ta mʼmapewa ta efodi tija ngati miyala ya chikumbutso cha ana a Israeli. Aaroni azinyamula mayinawo mʼmapewa ake kuti akhale chikumbutso pamaso pa Yehova.
13 Tu feras aussi des crampons d'or;
Upange zoyikamo za maluwa agolide,
14 Et deux chaînettes de fin or à bouts, en façon de cordon, et tu mettras les chaînettes ainsi faites à cordon dans les crampons.
ndiponso maunyolo awiri a golide wabwino kwambiri, wopetedwa ngati zingwe ndipo uwalumikize ku zoyikamozo.
15 Tu feras aussi le Pectoral de jugement d'un ouvrage exquis, comme l'ouvrage de l'Ephod, d'or, de pourpre, d'écarlate, de cramoisi, et de fin lin retors.
“Upange chovala chapachifuwa chogwiritsa ntchito poweruza mlandu ndipo uchipange mwaluso kwambiri. Uchipange ngati efodi pogwiritsa ntchito golide, nsalu yamtundu wa mtambo, yapepo, yofiira, yofewa yosalala ndi yolukidwa bwino.
16 Il sera carré [et] double; et sa longueur sera d'une paume, et sa largeur d'une paume.
Kutalika kwake kukhale kofanana mbali zonse, mulitali masentimita 23, mulifupi masentimita 23, ndipo chikhale chopinda pawiri.
17 Et tu le rempliras de remplage de pierrerie, à quatre rangées de pierres [précieuses]. A la première rangée on mettra une Sardoine, une Topaze, et une Emeraude.
Uyikepo mizere inayi ya miyala yokongola kwambiri. Mzere woyamba ukhale ndi miyala ya rubi, topazi ndi berili.
18 Et à la seconde rangée, une Escarboucle, un Saphir, et un Jaspe.
Mzere wachiwiri pakhale miyala ya emeradi, safiro ndi dayimondi;
19 Et à la troisième rangée, un Ligure, une Agathe, et une Améthyste.
mzere wachitatu pakhale miyala ya opera, agate ndi ametisiti.
20 Et à la quatrième rangée, un Chrysolithe, un Onyx et un Béryl, qui seront enchâssés dans de l'or, selon leurs remplages.
Mzere wachinayi pakhale miyala ya topazi, onikisi ndi yasipa. Miyalayi uyiike mu zoyikamo zagolide.
21 Et ces pierres-là seront selon les noms des enfants d'Israël, douze selon leurs noms, chacune d'elles gravée de gravure de cachet, selon le nom qu'elle en doit porter, [et] elles seront pour les douze Tribus.
Miyalayo ikhalepo khumi ndi iwiri, uliwonse kuyimira dzina limodzi la ana a Israeli. Mwala uliwonse uzokotedwe ngati chidindo dzina limodzi la mafuko khumi ndi awiri a Israeli.
22 Tu feras donc pour le Pectoral des chaînettes à bouts, en façon de cordon, qui seront de pur or.
“Upange timaunyolo tagolide wabwino kwambiri ta pa chovala chapachifuwa, topota ngati chingwe.
23 Et tu feras sur le Pectoral deux anneaux d'or, et tu mettras les deux anneaux aux deux bouts du Pectoral.
Upangenso mphete ziwiri zagolide ndipo uzimangirire pa ngodya ziwiri za pa chovala chapachifuwa.
24 Et tu mettras les deux chaînettes d'or faites à cordon, dans les deux anneaux à l'extrémité du Pectoral.
Umangirire timaunyolo tiwiri tagolide tija pa mphete za pa ngodya pa chovala chapachifuwacho.
25 Et tu mettras les deux autres bouts des deux chaînettes faites à cordon, aux deux crampons, et tu les mettras sur les épaulières de l'Ephod, sur le devant de l'Ephod.
Ndipo mbali ina ya timaunyoloto umangirire pa zoyikapo zake ziwiri zija ndi kulumikiza pa tinsalu takutsogolo kwa mapewa a efodi.
26 Tu feras aussi deux autres anneaux d'or, que tu mettras aux deux autres bouts du Pectoral, sur le bord qui sera du côté de l'Ephod en dedans.
Upangenso mphete ziwiri zagolide, ndipo uzilumikize ku ngodya ziwiri zamʼmunsi mwa chovala chapachifuwa, champhepete mwake, mʼkati pafupi ndi efodi ija.
27 Et tu feras deux autres anneaux d'or, que tu mettras aux deux épaulières de l'Ephod par le bas, répondant sur le devant, à l'endroit où il se joint, au-dessus du ceinturon exquis de l'Ephod.
Upangenso mphete zina ziwiri zagolide ndipo uzilumikize kumunsi kwa tinsalu takutsogolo kwa efodi, pafupi ndi msoko, pamwamba pangʼono pa lamba wamʼchiwuno wa efodi.
28 Et ils joindront le Pectoral élevé par ses anneaux, aux anneaux de l'Ephod, avec un cordon de pourpre, afin qu'il tienne au-dessus du ceinturon exquis de l'Ephod, et que le Pectoral ne bouge point de dessus l'Ephod.
Tsono umangirire mphete za pa chovala chapachifuwa zija ku mphete za efodi ndi chingwe chamtundu wa mtambo, kulumikiza lamba ndi chovala chapachifuwacho kuti chovala chapachifuwacho chisalekane ndi efodi.
29 [Ainsi] Aaron portera sur son cœur les noms des enfants d'Israël au Pectoral de jugement, quand il entrera dans le lieu Saint, pour mémorial devant l'Eternel, continuellement.
“Pamene Aaroni akulowa kumalo opatulika azivala chovala chapachifuwa cha zoweruzira chija chimene chalembedwa mayina a ana a Israeli kuti Yehova awakumbukire nthawi zonse.
30 Et tu mettras sur le Pectoral de jugement l'Urim et le Thummim, qui seront sur le cœur d'Aaron, quand il viendra devant l'Eternel; et Aaron portera le jugement des enfants d'Israël sur son cœur devant l'Eternel, continuellement.
Ndiponso uyike Urimu ndi Tumimu mu chovala chapachifuwa cha zoweruziracho, kuti zikhale pamtima pa Aaroni. Choncho Aaroniyo adzakhala akutenga nthawi zonse zida zomuthandizira kuweruza ana a Israeli pamene adzafika pamaso pa Yehova.
31 Tu feras aussi le Rochet de l'Ephod entièrement de pourpre.
“Uyipangire efodiyo mkanjo wamtundu wa mtambo.
32 Et l'ouverture où passe la tête sera au milieu, [et] il y aura un ourlet à son ouverture tout autour, d'ouvrage tissu, comme l'ouverture d'un corselet, afin qu'il ne se déchire point.
Mkanjowo ukhala ndi malo opisapo mutu pakati pakepo. Pa chibowopo pakhale chibandi chosokedwa mochita ngati kuluka monga muja akhalira malaya kuti chibowocho chilimbe, chisangʼambike.
33 Et tu feras à ses bords des grenades de pourpre, d'écarlate, et de cramoisi tout autour, et des clochettes d'or entre elles tout autour.
Pa mpendero wamʼmunsi wa mkanjowo, upange mphonje zokhala ngati makangadza za nsalu yamtundu wa mtambo, yapepo ndi yofiira zokhala ndi maberu agolide pakati pake.
34 Une clochette d'or, puis une grenade; une clochette d'or, puis une grenade; aux bords du Rochet tout autour.
Choncho pazikhala mphonje imodzi kenaka belu limodzi, kuzungulira mpendero wa mkanjo wonse.
35 Et Aaron en sera revêtu quand il fera le service, et on en entendra le son lorsqu'il entrera dans le lieu Saint devant l'Eternel, et quand il en sortira, afin qu'il ne meure pas.
Aaroni azivala mkanjowo pamene akutumikira ngati wansembe. Kulira kwa maberu kuzimveka pamene akulowa mʼmalo opatulika pamaso pa Yehova ndiponso pamene akutuluka, kuti asafe.
36 Et tu feras une lame de pur or, sur laquelle tu graveras [ces mots], de gravure de cachet: LA SAINTETÉ A L'ETERNEL.
“Upange duwa lagolide wabwino kwambiri kukhala ngati chidindo ndipo uzokotepo mawu akuti, Cohoperekedwa kwa Yehova.
37 Laquelle tu poseras avec un cordon de pourpre, et elle sera sur la Tiare, répondant sur le devant de la Tiare.
Ulimange ndi chingwe cha nsalu yamtundu wa mtambo pa nduwira ya Aaroni, ndipo duwalo likhale kutsogolo kwa nduwirayo.
38 Et elle sera sur le front d'Aaron; et Aaron portera l'iniquité des saintes offrandes que les enfants d'Israël auront offertes, dans tous les dons de leurs saintes offrandes, et elle sera continuellement sur son front, pour les rendre agréables devant l'Eternel.
Lidzakhala pa mphumi ya Aaroni, motero iye adzasenza cholakwa chilichonse cha pa zopereka zilizonse zimene Aisraeli amazipatulira Yehova. Aaroni azivala chikwangwanichi pa mphumi pake nthawi zonse kuti Yehova alandire zopereka za anthu ake.
39 Tu feras aussi une chemise de fin lin qui s'appliquera sur le corps, et tu feras aussi la Tiare de fin lin; mais tu feras le baudrier d'ouvrage de broderie.
“Uluke mwinjiro wa nsalu yofewa yosalala ndiponso upange nduwira ya nsalu yofewa yosalala. Lamba wake akhale wolukidwa bwino ndi munthu waluso.
40 Tu feras aussi aux enfants d'Aaron des chemises, des baudriers, et des calottes pour leur gloire et pour leur ornement.
Upangirenso ana a Aaroni mwinjiro, malamba ndi nduwira kuti azioneka mwaulemu ndi molemekezeka.
41 Et tu en revêtiras Aaron ton frère, et ses fils avec lui; tu les oindras, tu les consacreras et tu les sanctifieras; puis ils m'exerceront la Sacrificature.
Zovala zimenezi umuveke Aaroni, mʼbale wako ndi ana ake. Kenaka uwadzoze, uwapatse udindo ndi kuwapatula kuti anditumikire ngati ansembe anga.
42 Et tu leur feras des caleçons de lin, pour couvrir leur nudité, qui tiendront depuis les reins jusqu'au bas des cuisses.
“Uwapangire akabudula a nsalu yofewa oyambira mʼchiwuno kulekeza mʼntchafu kuti asamaonetse maliseche.
43 Et Aaron et ses fils seront ainsi habillés quand ils entreront au Tabernacle d'assignation, ou quand ils approcheront de l'autel pour faire le service dans le lieu Saint; et ils ne porteront point la peine d'aucune iniquité, et ne mourront point. Ce sera une ordonnance perpétuelle pour lui et pour sa postérité après lui.
Aaroni ndi ana ake ayenera kuvala akabudulawo pamene akulowa mu tenti ya msonkhano kapena pamene akupita ku guwa lansembe kukatumikira malo oyera kuopa kuti angachimwe ndi kufa. “Ili likhale lamulo la nthawi zonse kwa Aaroni ndi zidzukulu zake.”