< Esther 7 >
1 Le Roi donc et Haman vinrent au festin avec la Reine Esther.
Choncho mfumu ndi Hamani anabwera kudzadya phwando la mfumukazi Estere.
2 Et le Roi dit à Esther encore ce second jour, au vin de la collation: Quelle est ta demande, Reine Esther? et elle te sera octroyée; et quelle est ta prière? fût-ce jusqu'à la moitié du Royaume, cela sera fait.
Pa tsiku lachiwiri akumwa vinyo, mfumu inafunsanso kuti, “Kodi iwe mfumukazi Estere, chimene ufuna kupempha nʼchiyani? Chimene uti upemphe ndidzakupatsa. Choncho ukufuna chiyani? Ngakhale utafuna theka la ufumu ndidzakupatsa.”
3 Alors la Reine Esther répondit, et dit: Si j'ai trouvé grâce devant toi, ô Roi! et si le Roi le trouve bon, que ma vie me soit donnée à ma demande, et que mon peuple [me soit donné] à ma prière.
Kenaka mfumukazi Estere anayankha kuti, “Ngati mwandikomera mtima, inu mfumu, ndipo ngati chingakukomereni mfumu, pempho ndi chokhumba changa ndi ichi, mulole kuti ine ndi abale anga tisungidwe tonse ndi moyo.
4 Car nous avons été vendus, moi et mon peuple, pour être exterminés, tués et détruits. Que si nous avions été vendus pour être serviteurs et servantes, je me fusse tue; bien que l'oppresseur ne récompenserait point le dommage que le Roi en recevrait.
Popeza ine ndi anthu a mtundu wanga tagulitsidwa kuti atiwononge, atiphe ndi kutifafaniziratu. Akanangotigulitsa kokha tikanakhala chete, chifukwa chimene mdani wathuyo akanakupatsani mfumu sibwenzi mutasowa nacho mtendere.”
5 Et le Roi Assuérus parla et dit à la Reine Esther: Qui est et où est cet homme, qui a été si téméraire que de faire cela?
Mfumu Ahasiwero anamufunsa mfumukazi Estere, “Kodi iyeyu ndi ndani ndipo ali kuti amene saopa kuchita chinthu chotere?”
6 Et Esther répondit: l'oppresseur et l'ennemi est ce méchant Haman ici. Alors Haman fut troublé de la présence du Roi et de la Reine.
Estere anati, “Wotizunza ndiponso mdani wathu! Munthu woyipayo ndi Hamani.” Kenaka Hamani anagwidwa ndi mantha pamaso pa mfumu ndi mfumukazi.
7 Et le Roi en colère se leva du vin de la collation, et il entra dans le jardin du palais; mais Haman resta, afin de prier pour sa vie la Reine Esther; car il voyait bien que le Roi était résolu de le perdre.
Mfumu itakwiya kwambiri inanyamuka pa phwando nipita ku munda wa maluwa wa nyumba yaufumu. Koma Hamani, pozindikira kuti mfumu yaganiza kale kumuchitira choyipa, anatsalira mʼnyumba kupempha Estere kuti apulumutse moyo wake.
8 Puis le Roi retourna du jardin du palais au lieu où l'on avait présenté le vin de la collation; (or Haman s'était jeté sur le lit où était Esther) et le Roi dit: Forcerait-il bien encore sous mes yeux la Reine en cette maison? Dès que la parole fut sortie de la bouche du Roi, aussitôt on couvrit le visage d'Haman.
Mfumu itabwerera kuchokera ku munda wa maluwa wa nyumba yaufumu uja ndi kulowanso mʼchipinda chaphwando, anapeza Hamani atagona chafufumimba pa mpando wa khutagone pomwe Estere anakhalapo. Mfumu inayankhula mokweza kuti, “Kodi afunanso kuvula mfumukazi momukakamiza pamene ine ndili mʼnyumba?” Mfumu isanatsirize kuyankhula mawu awa, atumiki ake anaphimba nkhope ya Hamani.
9 Et Harbona l'un des Eunuques dit en la présence du Roi: Voilà même le gibet qu'Haman a fait faire pour Mardochée, qui donna ce bon avis pour le Roi, est tout dressé dans la maison d'Haman, haut de cinquante coudées; et le Roi dit: Pendez-l'y.
Haribona, mmodzi wa adindo ofulidwa amene ankatumikira mfumu anati, “Mtanda wotalika mamita 23 uli mʼnyumba ya Hamani. Mtandawu, Hamani anapangira Mordekai, uja amene anapulumutsa mfumu ku chiwembu.” Mfumu inati, “Mpachikeni pamenepo!”
10 Et ils pendirent Haman au gibet qu'il avait préparé pour Mardochée; et la colère du Roi fut apaisée.
Choncho anamupachika Hamani pa mtanda umene anakonzera Mordekai. Kenaka mkwiyo wa mfumu unatsika.