< Esther 1 >

1 Or il arriva au temps d'Assuérus, qui régnait depuis les Indes jusqu'en Ethiopie, sur cent vingt-sept provinces;
Izi ndi zimene zinachitika pa nthawi ya ufumu wa Ahasiwero, amene analamulira zigawo 127 kuyambira ku India mpaka ku Kusi.
2 [Il arriva, dis-je], en ce temps-là, que le Roi Assuérus étant assis sur le trône de son règne à Susan, la ville capitale;
Pa nthawi imeneyi nʼkuti mfumu Ahasiwero atakhazikika pa mpando wake wa ufumu mu mzinda wa Susa,
3 La troisième année de son règne, il fit un festin à tous les principaux Seigneurs de ses pays, et à ses serviteurs, de sorte que la puissance de la Perse et de la Médie, [savoir] les plus grands Seigneurs, et les Gouverneurs des provinces étaient devant lui;
ndipo mʼchaka chachitatu cha ufumu wake anakonza phwando la olemekezeka ndi nduna zake. Atsogoleri a nkhondo a ku Peresiya ndi Mediya, anthu olemekezeka pamodzi ndi nduna za mʼzigawo zonse anasonkhana kwa iye.
4 Pour montrer les richesses de la gloire de son Royaume, et la splendeur de l'excellence de sa grandeur, durant plusieurs jours; [savoir] cent quatre-vingts jours.
Pa nthawi yomweyi kwa masiku 180 a phwando mfumu inkaonetsa kulemera kwa ulemerero wa ufumu wake ndiponso kukongola ndi kukula kwa ufumu wake.
5 Et au bout de ces jours-là, le Roi fît un festin pendant sept jours, dans le parvis du jardin du palais Royal, à tout le peuple qui se trouva dans Susan, la ville capitale, depuis le plus grand jusqu'au plus petit.
Atatha masiku amenewa, kwa masiku ena asanu ndi awiri mfumu inakonzanso phwando la anthu onse okhala mu mzinda wa Susa kuyambira anthu olemekezeka mpaka anthu wamba ku bwalo la munda la nyumba yake yaufumu.
6 [Les tapisseries] de blanc, de vert et de pourpre tenaient avec des cordons de fin lin et d'écarlate à des anneaux d'argent, et à des piliers de marbre; les lits étaient d'or et d'argent sur un pavé de porphyre, de marbre, d'albâtre, et de marbre tacheté.
Bwalo la mundali analikongoletsa ndi makatani a nsalu zoyera ndi za mtundu wamtambo zimene anazimangirira ndi zingwe za nsalu zoyera ndi zapepo ku mphete za siliva zimene anazikoloweka pa nsanamira za maburo. Anayika mipando yopumirapo yagolide ndi siliva pabwalo la miyala yoyala yamtengowapatali yofiira, ya marabulo, ndi yonyezimira.
7 Et on donnait à boire en vaisselle d'or, qui était en diverses façons; et il y avait du vin Royal en abondance, selon l'opulence du Roi.
Anapereka zakumwa mʼchikho zagolide zamitundumitundu, ndipo vinyo waufumu anali wochuluka kwambiri monga mwa kukoma mtima kwa mfumu.
8 Et la manière de boire fut telle qu'on l'avait ordonné. On ne contraignait personne; car le Roi avait ainsi expressément commandé à tous ses maîtres d'hôtel, de faire selon la volonté de chacun.
Monga mwa lamulo la mfumu aliyense anamwa mʼmene anafunira, pakuti mfumu inawuza otumikira ake kuti apatse aliyense monga mwa kukonda kwake.
9 Et Vasti la Reine fit aussi un festin aux femmes dans la maison Royale, qui [était] au Roi Assuérus.
Mkazi wa mfumu Vasiti nayenso anakonzera phwando amayi ku nyumba ya ufumu ya mfumu Ahasiwero.
10 Or au septième jour, comme le Roi avait le cœur gai de vin, il commanda à Méhuman, Bizta, Harbona, Bigtha, Abagtha, Zéthar, et Carcas, les sept Eunuques qui servaient devant le Roi Assuérus,
Pa tsiku la chisanu ndi chiwiri, pamene mfumu Ahasiwero inaledzera ndi vinyo, inalamula adindo ofulidwa asanu ndi awiri amene ankamutumikira: Mehumani, Bizita, Haribona, Bigita, Abagita, Zetara, ndi Karikasi
11 Qu'ils amenassent devant lui la Reine Vasti, portant la couronne Royale, afin de faire voir sa beauté aux peuples et aux Seigneurs; car elle était belle à voir.
kuti abwere naye mfumukazi Vasiti pamaso pa mfumu atavala chipewa chaufumu. Cholinga cha mfumu chinali choti adzamuonetse kwa anthu onse ndi olemekezeka, chifukwa anali wokongola kwambiri.
12 Mais la Reine Vasti refusa de venir au commandement que le Roi lui fit faire par les Eunuques; et le Roi se mit en fort grande colère, et sa colère s'embrasa au dedans de lui.
Koma antchito atapereka uthenga wa mfumu kwa mfumukazi, Vasiti anakana kubwera. Tsono mfumu inakwiya ndi kupsa mtima.
13 Alors le Roi dit aux Sages qui avaient la connaissance des temps, (car le Roi communiquait ainsi avec tous ceux qui connaissaient les lois et le droit;
Mfumu inayankhula ndi anthu anzeru ndi ozindikira choyenera kuchita popeza chinali chikhalidwe chake kufunsa uphungu kwa akatswiri pa nkhani za malamulo ndi kuweruza kolungama.
14 Et alors Carséna, Séthar, Admatha, Tarsis, Mérès, Marséna, [et] Mémucan, sept Seigneurs de Perse et de Médie, étaient proches de lui, qui voyaient la face du Roi, et ils avaient les premiers sièges dans le Royaume.)
Anthu amene ankakhala pafupi ndi mfumu anali awa: Karisena, Setara, Adimata, Tarisisi, Meresi, Marisena ndi Memukani, olemekezeka asanu ndi awiri a ku Peresiya ndi Medina amene ankaloledwa mwapadera kuonana ndi mfumu ndipo anali pamwamba kwambiri mu ufumuwo.
15 Qu'y a-t-il à faire selon les lois à la Reine Vasti, pour n'avoir pas exécuté le commandement que le Roi Assuérus lui a envoyé faire par les Eunuques?
Mfumu inafunsa kuti, “Kodi titani naye mfumukazi Vasiti mwa lamulo, popeza sanamvere lamulo la ine mfumu Ahasiwero limene adindo ofulidwa anakamuwuza?”
16 Alors Mémucan parla en présence du Roi et des Seigneurs, [disant]: La Reine Vasti n'a pas seulement mal agi contre le Roi, mais aussi contre tous les Seigneurs, et contre tous les peuples qui sont dans toutes les provinces du Roi Assuérus.
Ndipo Memukani anayankha pa maso pa mfumu ndi olemekezeka anzake kuti, “Mfumukazi Vasiti sanalakwire mfumu yokha, koma walakwiranso olemekezeka onse ndi anthu onse okhala mʼzigawo zonse za mfumu Ahasiwero.
17 Car l'action de la Reine viendra [à la connaissance] de toutes les femmes, pour leur faire mépriser leurs maris, quand on dira: Le Roi Assuérus avait commandé qu'on lui amenât la Reine, et elle n'y est pas venue.
Pakuti amayi onse adzadziwa zimene wachita mfumukazi ndipo kotero adzapeputsa amuna awo ndi kunena kuti, ‘Mfumu Ahasiwero analamulira kuti abwere naye mfumukazi Vasiti kwa iye koma sanapite.’
18 Et aujourd'hui les Dames de Perse et de Médie qui auront appris la réponse de la Reine, répondront [ainsi] à tous les Seigneurs [des pays] du Roi; et comme ce sera une marque de mépris, ce sera aussi un sujet d'emportement.
Lero lomwe lino amayi olemekezeka a ku Peresiya ndi Mediya amene amva zimene wachita mfumukazi adzaganiza zochita chimodzimodzi kwa nduna zonse za mfumu. Ndipo kupeputsana ndi kukongola zidzapitirira.”
19 Si le Roi donc le trouve ainsi bon, qu'un Edit Royal soit publié de sa part, et qu'il soit écrit entre les ordonnances de Perse et de la Médie, et qu'il soit irrévocable; [savoir] que Vasti ne vienne plus devant le Roi Assuérus; et que le Roi donne son Royaume à sa compagne, [qui sera] meilleure qu'elle.
“Choncho, ngati chikukomerani mfumu, lamulirani kuti Vasiti asadzaonekerenso pamaso pa mfumu Ahasiwero. Lamuloli lilembedwe mʼmabuku a malamulo a Aperezi ndi Amedi kuti lisadzasinthike. Pamalo pa Vasiti ngati mfumukazi payikidwepo mkazi wina amene ali bwino kuposa iye.
20 Et l'Edit, que le Roi aura fait ayant été su par tout son Royaume, quelque grand qu'il soit, toutes les femmes honoreront leurs maris, depuis le plus grand jusqu'au plus petit.
Ndipo lamulo la mfumuli lilengezedwa mʼdziko lake lonse ngakhale lili lalikulu, amayi onse adzapereka ulemu kwa amuna awo, amuna olemekezeka mpaka amuna wamba.”
21 Et cette parole plut au Roi et aux Seigneurs; et le Roi fit selon la parole de Mémucan.
Mfumu ndi nduna zake anakondwera ndi uphungu uwu, kotero mfumu inachita monga momwe ananenera Memukani.
22 Il envoya des lettres par toutes les provinces du Roi, à chaque province selon sa manière d'écrire, et à chaque peuple selon sa langue, afin que chacun fût maître en sa maison, et parlant selon la langue de son peuple.
Mfumu inatumiza makalata ku madera onse a ufumu wake, chigawo chilichonse mʼzilembo zawo ndi ku mtundu uliwonse mʼchiyankhulo chawochawo kulengeza kuti mwamuna ayankhule chilichonse chimene chikumukomera.

< Esther 1 >