< Amos 6 >

1 Hola! vous qui êtes à votre aise en Sion, et vous qui vous confiez en la montagne de Samarie, [lieux] les plus renommés d'entre les principaux des nations, auxquels va la maison d'Israël.
Tsoka kwa amene simukulabadira kanthu ku Ziyoni, ndiponso kwa inu amene mukukhala mwamtendere pa Phiri la Samariya, inu anthu otchuka ochokera ku mtundu wa anthu omveka, kumene Aisraeli amafikako!
2 Passez jusqu'à Calne, et regardez; et vous en allez de là à Hamath la grande; puis descendez à Gath des Philistins; n'étaient-ils pas plus excellents que ces Royaumes-ci? Leur pays n'était-il pas plus étendu que votre pays?
Pitani ku mzinda wa Kaline mukawuyangʼane; mukapitenso ku Hamati-raba mzinda waukulu uja, ndipo mukatsikirenso ku Gati kwa Afilisti. Kodi mizinda imeneyi ndi yopambana maufumu anu awiriwa? Kodi dziko lawo ndi lalikulu kupambana lanu?
3 Vous qui éloignez les jours de la calamité, et qui approchez de vous le siège de violence;
Inu simulabadirako kuti tsiku loyipa lidzafika, zochita zanu zimafulumizitsa ulamuliro wankhanza.
4 Qui vous couchez sur des lits d'ivoire, et vous étendez sur vos couches; qui mangez les agneaux [choisis] du troupeau, et les veaux pris du lieu où on les engraisse;
Mumagona pa mabedi owakongoletsa ndi minyanga ya njovu, mumagona pa mipando yanu ya wofuwofu. Mumadya ana ankhosa onona ndi ana angʼombe onenepa.
5 Qui fredonnez au son de la musette; qui inventez des instruments de musique, comme David;
Mumayimba azeze anu ndi kumangopeka nyimbo pa zingʼwenyengʼwenye ngati Davide.
6 Qui buvez le vin dans des bassins, et vous parfumez des parfums les plus exquis, et qui n'êtes point malades pour la plaie de Joseph.
Mumamwera vinyo mʼzipanda zodzaza ndipo mumadzola mafuta abwino kwambiri, koma simumva chisoni ndi kuwonongeka kwa Yosefe.
7 A cause de cela ils s'en iront incessamment en captivité, entre les premiers qui s'en iront en captivité, et le luxe de ces personnes voluptueuses prendra fin.
Nʼchifukwa chake inu mudzakhala mʼgulu la anthu oyamba kupita ku ukapolo; maphwando ndi zikondwerero zanu zidzatheratu.
8 Le Seigneur l'Eternel a juré par soi-même, l'Eternel Dieu des armées dit ainsi: J'ai en détestation l'orgueil de Jacob, et j'ai en haine ses palais, c'est pourquoi je livrerai la ville, et tout ce qui est en elle.
Ambuye Yehova walumbira mʼdzina lake. Yehova Mulungu Wamphamvuzonse walengeza kuti, “Ndimanyansidwa ndi kunyada kwa Yakobo, ndimadana ndi nyumba zake zaufumu; Ine ndidzawupereka mzindawu pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo.”
9 Et s'il arrive qu'il y ait dix hommes de reste dans une maison, ils mourront.
Ngati anthu khumi otsala adzabisala mʼnyumba imodzi, nawonso adzafa ndithu.
10 Et l'oncle de chacun d'eux les prendra, et les brûlera pour en mettre les os hors de la maison; et il dira à celui qui sera au fond de la maison: y a-t-il encore quelqu'un avec toi? Et il répondra: C'en est la fin. Puis [son oncle lui] dira: Tais-toi; car [aussi] ils n'eussent point fait commémoration du nom de l'Eternel.
Ndipo ngati mʼbale wake wa wina wakufayo, woyenera kusamala za maliro, adzafika kudzatulutsa mitembo mʼnyumbamo nʼkufunsa aliyense amene akubisalabe mʼnyumbamo kuti, “Kodi uli ndi wina wamoyo mʼmenemo?” Ndipo munthu wobisalayo ndi kuyankha kuti, “Ayi,” mʼbaleyo adzanena kuti, “Khala chete! Ife tisayerekeze kutchula dzina la Yehova.”
11 Car voici l'Eternel commande, et il frappera les grandes maisons par des débordements d'eau, et les petites maisons par des fentes.
Pakuti Yehova walamula kuti nyumba zikuluzikulu Iye adzazigamulagamula, ndipo nyumba zazingʼono zidzasanduka maduka okhaokha.
12 Les chevaux courront-ils par les rochers? ou y labourera-t-on avec des bœufs? mais vous avez changé le jugement en fiel, et le fruit de la justice en absinthe.
Kodi akavalo amathamanga pa thanthwe? Kodi wina amatipula ndi ngʼombe mʼnyanja? Koma chiweruzo cholungama mwachisandutsa kukhala zinthu zakupha ndipo chipatso cha chilungamo mwachisandutsa kukhala chowawa.
13 Vous vous réjouissez en des choses de néant, [et] vous dites: Ne nous sommes-nous pas acquis de l'élévation par notre force?
Inu amene mukunyadira kuti munagonjetsa Lo Debara ndipo mukunena kuti, “Kodi sitinatenge Karinaimu ndi mphamvu zathu zokha?”
14 Mais, ô maison d'Israël! voici, j'élèverai contre vous une nation, dit l'Eternel le Dieu des armées, laquelle vous opprimera depuis l'entrée de Hamath jusqu'au torrent du désert.
Koma Yehova Mulungu Wamphamvuzonse akulengeza kuti, “Inu nyumba ya Israeli, ndidzakudzutsirani mtundu wina wa anthu umene udzakuzunzani kuchokera ku Lebo Hamati mpaka ku Chigwa cha Araba.”

< Amos 6 >