< 2 Samuel 9 >

1 Alors David dit: Mais n'y a-t-il plus personne qui soit demeuré de reste de la maison de Saül, et je lui ferai du bien pour l'amour de Jonathan?
Davide anafunsa kuti, “Kodi alipo amene watsala mʼbanja la Sauli kuti ndimuchitire chifundo chifukwa cha Yonatani?”
2 Or il y avait dans la maison de Saül un serviteur nommé Tsiba, lequel on appela pour le faire venir vers David. Et le Roi lui dit: Es-tu Tsiba? et il répondit: Je suis ton serviteur [Tsiba].
Tsono panali mtumiki wina wa banja la Sauli wotchedwa Ziba. Iwo anamuyitana kuti aonekere pamaso pa Davide, ndipo mfumu inamufunsa kuti, “Kodi ndiwe Ziba?” Iyeyo anayankha kuti, “Ine mtumiki wanu.”
3 Et le Roi dit: N'y a-t-il plus personne de la maison de Saül, et j'userai envers lui d'une grande gratuité. Et Tsiba répondit au Roi: Il y a encore un des fils de Jonathan, qui est blessé aux pieds.
Mfumu inafunsa kuti, “Kodi palibe amene watsala wa banja la Sauli amene ndingamuchitire chifundo cha Mulungu?” Ziba anayankha mfumu kuti, “Alipo mwana wa Yonatani, koma ndi wolumala mapazi ake onse.”
4 Et le Roi lui dit: Où est-il? Et Tsiba répondit au Roi: Voilà, il est en la maison de Makir fils de Hammiel, à Lodébar.
Mfumu inafunsa kuti, “Ali kuti?” Ziba anayankha kuti, “Iye ali ku nyumba ya Makiri mwana wa Amieli ku Lodebara.”
5 Alors le Roi David envoya, et le fit amener de la maison de Makir, fils de Hammiel, de Lodébar.
Kotero mfumu inamubweretsa kuchokera ku Lodebara, ku nyumba ya Makiri mwana wa Amieli.
6 Et quand Méphiboseth, le fils de Jonathan fils de Saül, fut venu vers David, il s'inclina sur son visage, et se prosterna. Et David dit: Méphiboseth; et il répondit: Voici ton serviteur.
Mefiboseti mwana wa Yonatani, mwana wa Sauli atafika kwa Davide, anawerama pansi kupereka ulemu kwa iye. Davide anati, “Mefiboseti!” Iye anayankha kuti, “Ine mtumiki wanu.”
7 Et David lui dit: Ne crains point; car certainement je te ferai du bien pour l'amour de Jonathan ton père, et je te restituerai toutes les terres de Saül ton père, et tu mangeras toujours du pain à ma table.
Davide anati kwa iye, “Usachite mantha, pakuti ndidzakuchitira ndithu chifundo chifukwa cha abambo ako Yonatani. Ine ndidzakubwezera iwe dziko lonse limene linali la agogo ako Sauli, ndipo iweyo udzadya ndi ine nthawi zonse.”
8 Et [Méphiboseth] se prosterna, et dit: Qui suis-je moi ton serviteur, que tu aies regardé un chien mort, tel que je suis?
Mefiboseti anawerama pansi ndipo anati, “Mtumiki wanu ndine yani kuti musamale galu wakufa ngati ine?”
9 Et le Roi appela Tsiba serviteur de Saül, et lui dit: J'ai donné au fils de ton maître tout ce qui appartenait à Saül, et à toute sa maison.
Kenaka Davide anayitanitsa Ziba, mtumiki wa Sauli, ndipo anati, “Ine ndapereka kwa chidzukulu cha mbuye wako chilichonse chimene chinali cha Sauli ndi banja lake.
10 C'est pourquoi laboure pour lui ces terres-là, toi et tes fils, et tes serviteurs, et recueilles-en les fruits, afin que le fils de ton maître ait du pain à manger; mais quant à Méphiboseth, fils de ton maître, il mangera toujours du pain à ma table. Or Tsiba avait quinze fils, et vingt serviteurs.
Iwe ndi ana ndi antchito anu muzimulimira mʼdziko lake ndipo muzibweretsa zokololazo kuti chidzukulu cha mbuye wako chikhale ndi chakudya. Ndipo Mefiboseti, chidzukulu cha mbuye wako adzadya ndi ine nthawi zonse.” (Tsono Ziba anali ndi ana aamuna khumi ndi asanu ndi antchito makumi awiri).
11 Et Tsiba dit au Roi: Ton serviteur fera tout ce que le Roi mon Seigneur a commandé à son serviteur. Mais quant à Méphiboseth, (dit le Roi) il mangera à ma table, comme un des fils du Roi.
Ndipo Ziba anati kwa mfumu, “Mtumiki wanu adzachita chilichonse chimene mbuye wanga mfumu mudzalamulire wantchito wanu kuti achite.” Kotero Mefiboseti ankadya ndi Davide monga mmodzi wa ana a mfumu.
12 Or Méphiboseth avait un petit-fils nommé Mica; et tous ceux qui demeuraient dans la maison de Tsiba étaient des serviteurs de Méphiboseth.
Mefiboseti anali ndi mwana wamngʼono wamwamuna wotchedwa Mika, ndipo onse a banja la Ziba anali antchito a Mefiboseti.
13 Et Méphiboseth demeurait à Jérusalem, parce qu'il mangeait toujours à la table du Roi; et il était boiteux des deux pieds.
Ndipo Mefiboseti anakhala mu Yerusalemu chifukwa nthawi zonse amadya ndi mfumu. Iye anali wolumala mapazi ake onse.

< 2 Samuel 9 >