< 2 Rois 21 >
1 Manassé [était] âgé de douze ans, quand il commença à régner, et il régna cinquante-cinq ans à Jérusalem; sa mère avait nom Hephtsiba.
Manase anakhala mfumu ali ndi zaka khumi ndi ziwiri ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 55. Amayi ake anali Hefiziba.
2 Et il fit ce qui déplaît à l'Eternel, selon les abominations des nations que l'Eternel avait chassées de devant les enfants d'Israël.
Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova, potsatira mchitidwe wonyansa wa mitundu imene Yehova anayipirikitsa pofika Aisraeli.
3 Car il rebâtit les hauts lieux qu'Ezéchias son père avait détruits, et redressa des autels à Bahal, et fit un bocage, comme avait fait Achab Roi d'Israël, il se prosterna devant toute l'armée des cieux, et il les servit.
Iyetu anamanganso malo opembedzera mafano amene Hezekiya abambo ake anawawononga. Anamangira Baala maguwa a nsembe ndi mtengo wa fano la Asera monga anachitira Ahabu mfumu ya Israeli ndipo ankapembedza zolengedwa zonse zamlengalenga.
4 Il bâtit aussi des autels dans la maison de l'Eternel, de laquelle l'Eternel avait dit: Je mettrai mon Nom dans Jérusalem.
Anamanga maguwa ansembewa mʼNyumba ya Yehova, mʼmene Yehova ananena kuti, “Mu Yerusalemu ndidzayikamo Dzina langa.”
5 Il bâtit, dis-je, des autels à toute l'armée des cieux dans les deux parvis de la maison de l'Eternel.
Mʼmabwalo onse awiri a Nyumba ya Yehova, Manase anamangamo maguwa opembedzerapo zinthu zamlengalenga.
6 Il fit aussi passer son fils par le feu, et il pronostiquait les temps, et observait les augures; il dressa un [oracle] d'esprit de Python, et de diseurs de bonne aventure; il faisait de plus en plus ce qui déplaît à l'Eternel pour l'irriter.
Iye anapsereza mwana wake pa moto ngati nsembe, ankachita za matsenga, ankawombeza mawula, ankapita kwa woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa ndiponso ankapembedza mizimu. Iyeyo anachita zoyipa zambiri pamaso pa Yehova ndipo anakwiyitsa Yehovayo.
7 Il posa aussi l'image du bocage qu'il avait fait, dans la maison dont l'Eternel avait dit à David, et à Salomon son fils: Je mettrai à perpétuité mon Nom dans cette maison, et dans Jérusalem, que j'ai choisie d'entre toutes les Tribus d Israël.
Iye anatenga fano losema la Asera limene analipanga ndi kuliyika mʼNyumba ya Yehova, Nyumba imene Yehova ananena kwa Davide ndi mwana wake Solomoni kuti, “Mʼnyumba iyi ndi mu Yerusalemu ndiwo malo amene ndasankha pakati pa mafuko onse a Aisraeli kuyikamo Dzina langa kwamuyaya.
8 Et je ne ferai plus sortir les Israëlites hors de cette terre que j'ai donnée à leurs pères, pourvu seulement qu'ils prennent garde à faire selon tout ce que je leur ai commandé, et selon toute la Loi que Moïse mon serviteur leur a ordonnée.
Sindidzalola kuti Aisraeli achotsedwe mʼdziko lawo limene ndinapatsa makolo awo ngati iwowo adzasamala kuchita zinthu zonse zimene ndinawalamula ndi kusunga malamulo onse amene mtumiki wanga Mose anawapatsa.”
9 Mais ils n'obéirent point; car Manassé les fit égarer, jusqu'à faire pis que les nations que Dieu avait exterminées de devant les enfants d'Israël.
Koma anthu sanamvere. Manase anawasocheretsa, kotero kuti anachita zoyipa zambiri kupambana anthu a mitundu ina amene Yehova anawawononga pamene Aisraeli ankafika.
10 Et l'Eternel parla par le moyen de ses serviteurs les Prophètes, en disant:
Yehova anayankhula kudzera mwa atumiki ake, aneneri kuti,
11 Parce que Manassé Roi de Juda a commis ces abominations, faisant pis que tout ce qu'ont fait les Amorrhéens qui ont été avant lui, et parce aussi qu'il a fait pécher Juda par ses dieux de fiente:
“Manase mfumu ya Yuda wachita machimo onyansawa ndipo wachita zoyipa kupambana Aamori amene analipo kale iye asanabadwe ndi kuchimwitsa anthu a ku Yuda ndi mafano ake.
12 A cause de cela l'Eternel le Dieu d'Israël, dit ainsi: Voici, je m'en vais faire venir un mal sur Jérusalem et sur Juda, tel que quiconque en entendra parler, les deux oreilles lui en corneront.
Choncho Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Taonani, ndikubweretsa pa Yerusalemu ndi Yuda mavuto akuti aliyense amene adzawamve adzathedwa nzeru.
13 Car j'étendrai sur Jérusalem le cordeau de Samarie, et le niveau de la maison d'Achab; et je torcherai Jérusalem comme une écuelle qu'on torche, et laquelle, après qu'on l'a torchée, on renverse sur son fond.
Ndidzalanga Yerusalemu ndi Yuda pogwiritsa ntchito muyeso umene ndinalangira Samariya ndi Ahabu pamodzi ndi nyumba yake. Ndidzayeretsa Yerusalemu monga mmene munthu amachitira popukuta mbale ndipo atayipukuta amayivundikira pansi.
14 Et j'abandonnerai le reste de mon héritage, et je les livrerai entre les mains de leurs ennemis; et ils seront en pillage, et en proie à tous leurs ennemis.
Ndidzawataya anthu otsala amene ndi cholowa changa ndipo ndidzawapereka mʼmanja mwa adani awo. Adzachotsedwa ndipo adaniwo adzawalanda zinthu zonse
15 Parce qu'ils ont fait ce qui me déplaît, et qu'ils m'ont irrité depuis le jour que leurs pères sont sortis d'Egypte, même jusqu'à ce jour-ci.
chifukwa anachita zoyipa pamaso panga ndipo akhala akundikwiyitsa kuchokera tsiku limene makolo awo anatuluka mu Igupto mpaka lero lino.’”
16 Davantage Manassé répandit une grande abondance de sang innocent, jusqu'à en remplir Jérusalem d'un bout à l'autre, outre son péché par lequel il fit pécher Juda; tellement qu'il fit ce qui déplaît à l'Eternel.
Kuwonjezera apo, Manase anakhetsa kwambiri magazi a anthu osalakwa mpaka magaziwo kuyenderera mu Yerusalemu kuyambira mbali ina mpaka mbali ina, kuphatikiza pa kuchimwitsa Yuda, kotero kuti anthu anachita zoyipa pamaso pa Yehova.
17 Le reste des faits de Manassé, tout ce, dis-je, qu'il a fait; et le péché qu'il commit, n'est-il pas écrit au Livre des Chroniques des Rois de Juda?
Ntchito zina za Manase ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
18 Puis Manassé s'endormit avec ses pères, et fut enseveli au jardin de sa maison, au Jardin de Huza; et Amon son fils régna en sa place.
Manase anagona ndi makolo ake ndipo anayikidwa mʼmanda mʼmunda wa Uza, ku nyumba yaufumu. Ndipo Amoni mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
19 Amon était âgé de vingt-deux ans, quand il commença à régner, et il régna deux ans à Jérusalem; sa mère avait nom Messullémet, fille de Haruts de Jotba.
Amoni anakhala mfumu ali ndi zaka 22 ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka ziwiri. Amayi ake anali Mesulemeti mwana wa Haruzi, wochokera ku Yotiba.
20 Il fit ce qui déplaît à l'Eternel comme avait fait Manassé son père.
Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova monga anachitira Manase abambo ake.
21 Car il suivit tout le train que son père avait tenu, et servit les dieux de fiente que son père avait servis, et se prosterna devant eux.
Anatsatira makhalidwe onse a abambo ake. Ankapembedza mafano amene abambo akewo ankawapembedza ndipo ankawagwadira.
22 Il abandonna l'Eternel le Dieu de ses pères, et il ne marcha point dans la voie de l'Eternel.
Iyeyo anasiya Yehova Mulungu wa makolo ake ndipo sanayende mʼnjira ya Yehova.
23 Or les serviteurs d'Amon firent une conspiration contre lui, et tuèrent le Roi dans sa maison.
Nduna za Amoni zinamuchita chiwembu ndipo zinamupha mʼnyumba yake.
24 Mais le peuple du pays frappa tous ceux qui avaient conspiré contre le Roi Amon, et ils établirent Josias son fils Roi en sa place.
Koma anthu a mʼdzikomo anapha onse amene anachitira chiwembu Mfumu Amoni, nayika Yosiya mwana wake kukhala mfumu mʼmalo mwake.
25 Le reste des faits d'Amon, lesquels il a fait, n'est-il pas écrit au Livre des Chroniques des Rois de Juda?
Ntchito zina za Amoni ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
26 Or on l'ensevelit dans son sépulcre au Jardin de Huza; et Josias son fils régna en sa place.
Iye anayikidwa mʼmanda ake mʼmunda wa Uza. Ndipo Yosiya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.