< 2 Rois 19 >

1 Et il arriva que dès que le Roi Ezéchias eut entendu ces choses, il déchira ses vêtements, et se couvrit d'un sac, et entra dans la maison de l'Eternel.
Mfumu Hezekiya atamva zimenezi, anangʼamba zovala zake navala chiguduli ndipo analowa mʼNyumba ya Yehova.
2 Puis il envoya Eliakim, Maître d'hôtel, et Sebna le Secrétaire, et les anciens d'entre les Sacrificateurs, couverts de sacs, vers Esaïe le Prophète fils d'Amots.
Iye anatuma Eliyakimu, woyangʼanira nyumba ya mfumu, Sebina mlembi wa bwalo ndi ansembe akuluakulu, onse atavala ziguduli, kwa mneneri Yesaya mwana wa Amozi.
3 Et ils lui dirent: Ainsi a dit Ezéchias: Ce jour est un jour d'angoisse, et de répréhension, et de blasphème; car les enfants sont venus jusqu'à l'ouverture de la matrice, mais il n'y a point de force pour enfanter.
Iwo anamuwuza kuti, “Hezekiya akunena kuti, ‘Lero ndi tsiku lamavuto, lachilango ndi lamanyazi. Ife lero tili ngati mayi woyembekezera amene pofika nthawi yoti achire akupezeka kuti alibe mphamvu zoberekera.
4 Peut-être que l'Eternel ton Dieu aura entendu toutes les paroles de Rab-saké, que le Roi des Assyriens son Maître a envoyé pour blasphémer le Dieu vivant, et pour l'outrager par les paroles que l'Eternel ton Dieu a entendues; fais donc une prière pour le reste qui se trouve encore.
Mwina Yehova Mulungu wanu adzamva mawu onse a Rabusake amene mbuye wake, mfumu ya ku Asiriya anamutuma kudzanyoza Mulungu wamoyo, ndipo Mulunguyo adzamulanga chifukwa cha mawu amene Yehova Mulungu wanu wamva. Choncho pemphererani anthu otsala amene akanali ndi moyo.’”
5 Les serviteurs donc du Roi Ezéchias vinrent vers Esaïe.
Akuluakulu a Mfumu Hezekiya atafika kwa Yesaya,
6 Et Esaïe leur dit, vous direz ainsi à votre Maître: Ainsi a dit l'Eternel: Ne crains point pour les paroles que tu as entendues, par lesquelles les serviteurs du Roi des Assyriens m'ont blasphémé.
Yesaya anawawuza kuti, “Kawuzeni mbuye wanu kuti, ‘Yehova akunena kuti: Usachite mantha ndi zimene wamva, mawu amene nthumwi za mfumu ya ku Asiriya zandinyoza nawo Ine.
7 Voici, je m'en vais mettre en lui un tel esprit, qu'ayant entendu un certain bruit, il retournera en son pays, et je le ferai tomber par l'épée dans son pays.
Tamverani! Ine ndidzayika mwa mfumuyo mzimu wina kotero kuti akadzamva mphekesera ya nkhondo, adzabwerera ku dziko lake ndipo Ine ndidzachititsa kuti aphedwe ndi lupanga kwawo komweko.’”
8 Or quand Rab-saké s'en fut retourné, il alla trouver le Roi des Assyriens qui battait Libna; car il avait appris qu'il était parti de Lakis.
Rabusake atamva kuti mfumu ya ku Asiriya yachoka ku Lakisi, iye anabwerera mʼmbuyo ndipo anakapeza mfumu ikuchita nkhondo ndi mzinda wa Libina.
9 Le [Roi] donc [des Assyriens] eut des nouvelles touchant Tirhaca Roi d'Ethiopie: Voilà, [lui disait-on], il est sorti pour te combattre. C'est pourquoi il s'en retourna, mais il envoya des messagers à Ezéchias, en leur disant:
Nthawi imeneyi Senakeribu analandira uthenga wakuti Tirihaka, mfumu ya ku Kusi, akubwera kudzachita naye nkhondo. Choncho iye anatumanso amithenga kwa Hezekiya ndi mawu awa:
10 Vous parlerez ainsi à Ezéchias Roi de Juda, et lui direz: Que ton Dieu, en qui tu te confies, ne t'abuse point en te disant: Jérusalem ne sera point livrée entre les mains du Roi des Assyriens.
“Kawuzeni Hezekiya mfumu ya Yuda kuti: Usalole kuti Mulungu amene ukumudalira akupusitse ponena kuti, ‘Yerusalemu sadzaperekedwa mʼmanja mwa mfumu ya ku Asiriya.’
11 Voilà, tu as entendu ce que les Rois des Assyriens ont fait à tous les pays en les détruisant entièrement; et tu échapperais?
Ndithu iwe unamva chimene mafumu a Asiriya anachita ku mayiko ena onse, kuti anawawononga kotheratu. Ndipo kodi iwe nʼkupulumuka?
12 Les dieux des nations que mes ancêtres ont détruites, [savoir] de Gozan, de Caran, de Retseph, et des enfants d'Héden, qui sont en Thélasar, les ont-ils délivrées?
Kodi milungu ya mitundu imene makolo anga anayigonjetsa, milungu ya anthu a ku Gozani, Harani, Rezefi ndi Aedeni amene anali ku Teli Asara, inawapulumutsa?
13 Où est le Roi de Hamath, le Roi d'Arpad, et le Roi de la ville de Sépharvajim, Hanath, et Hiwah?
Kodi mafumu a Hamati, Aripadi ndi mafumu a mizinda ya Sefaravaimu, Hena ndi Iva, ali kuti?”
14 Et quand Ezéchias eut reçu les Lettres de la main des messagers, et les eut lues, il monta dans la maison de l'Eternel, et Ezéchias les déploya devant l'Eternel.
Hezekiya analandira kalata kwa amithenga aja nayiwerenga. Pomwepo anapita ku Nyumba ya Yehova nayika kalatayo pamaso pa Yehova.
15 Puis Ezéchias fit sa prière devant l'Eternel, et dit: Ô Eternel Dieu d'Israël! qui es assis entre les Chérubins, toi seul es le Dieu de tous les Royaumes de la terre; tu as fait les cieux et la terre.
Ndipo Hezekiya anapemphera kwa Yehova nati, “Inu Yehova Mulungu wa Israeli, Inu amene mumakhala pa Akerubi, Inu nokha ndinu Mulungu wolamulira maufumu onse a dziko lapansi. Inu munalenga kumwamba ndi dziko lapansi.
16 Ô Eternel! incline ton oreille, et écoute; ouvre tes yeux, et regarde; et écoute les paroles de Sanchérib, [et] de celui qu'il a envoyé pour blasphémer le Dieu vivant.
Inu Yehova, tcherani khutu lanu ndipo mumve Yehova tsekulani maso anu ndipo muone, imvani mawu onse amene Senakeribu watumiza kunyoza Inu Mulungu wamoyo.
17 Il est vrai, ô Eternel! que les Rois des Assyriens ont détruit ces nations-là, et leurs pays;
“Inu Yehova, nʼzoonadi kuti mafumu a Asiriya anawononga mitundu iyi ndi mayiko awo.
18 Et qu'ils ont jeté qu feu leurs dieux, car ce n'étaient point des dieux, mais des ouvrages de main d'homme, du bois, et de la pierre, c'est pourquoi ils les ont détruits.
Iwo anaponya milungu yawo pa moto ndi kuyiwononga pakuti sinali milungu koma mitengo ndi miyala chabe, yopangidwa ndi anthu.
19 Maintenant donc, ô Eternel notre Dieu! je te prie, délivre-nous de la main de Sanchérib, afin que tous les Royaumes de la terre sachent que c'est toi, ô Eternel! qui es le seul Dieu.
Ndipo tsopano Inu Yehova Mulungu wathu, tipulumutseni ndithu mʼdzanja lake, kuti maufumu onse a dziko lapansi adziwe kuti Inu nokha, Inu Yehova, ndinu Mulungu.”
20 Alors Esaïe fils d'Amots, envoya vers Ezéchias, pour lui dire: Ainsi a dit l'Eternel le Dieu d'Israël: Je t'ai exaucé dans ce que tu m'as demandé touchant Sanchérib Roi des Assyriens.
Ndipo Yesaya mwana wa Amozi anatumiza uthenga kwa Hezekiya wakuti, “Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ndamva pemphero lako lonena za Senakeribu mfumu ya ku Asiriya.’”
21 [C'est] ici la parole que l'Eternel a prononcée contre lui. La vierge fille de Sion t'a méprisé, et s'est moquée de toi; la fille de Jérusalem a hoché la tête après toi.
Mawu amene Yehova wayankhula wotsutsana naye ndi awa: “Namwali wa Ziyoni akukunyoza ndi kukuseka iwe. Mwana wamkazi wa Yerusalemu akupukusa mutu wake kumbuyo kwako.
22 Qui as-tu outragé et blasphémé? contre qui as-tu élevé la voix, et levé les yeux en haut? c'est contre le Saint d'Israël.
Kodi iweyo wanyoza ndi kuchitira chipongwe yani? Kodi ndani amene wamufuwulira mawu ako ndi kumuyangʼana monyada? Wachitiratu izi Woyera wa Israeli!
23 Tu as outragé le Seigneur par le moyen de tes messagers, et tu as dit: Avec la multitude de mes chariots je suis monté tout au haut des montagnes aux côtés du Liban; je couperai les plus hauts cèdres, et les plus beaux sapins qui y soient, et j'entrerai dans les logis qui sont à ses bouts, et dans la forêt de son Carmel.
Kudzera mwa amithenga ako wonyoza Ambuye. Ndipo wanena kuti, ‘Ndi magaleta ochuluka ndinakwera mapiri ataliatali, pa msonga za mapiri a Lebanoni. Ndigwetsa mitengo yake ya mkungudza yayitali kwambiri, mitengo yake ya payini yabwino kwambiri. Ndalowanso mʼkati mwake mwenimweni, mwa nkhalango yake yowirira kwambiri.
24 J'ai creusé des sources après avoir bu les eaux étrangères; et j'ai tari avec la plante de mes pieds tous les ruisseaux des forteresses.
Ndakumba zitsime ku mayiko achilendo ndipo ndinamwa madzi a kumeneko. Ndi mapazi anga ndawumitsa mitsinje yonse ya ku Igupto.’”
25 N'as-tu pas appris qu'il y a déjà longtemps que j'ai fait cette ville, et qu'anciennement je l'ai ainsi formée? et l'aurais-je maintenant amenée au point d'être réduite en désolation, [et] les villes munies, en monceaux de ruines?
“‘Kodi sunamvepo? Zimenezi ndinazikhazikitsa kalekale. Ndinazikonzeratu masiku amakedzana; tsopano ndachita kuti zichitikedi, iwe kwako kunali kungosandutsa mizinda yotetezedwa kukhala milu ya miyala.
26 Il est vrai que leurs habitants étant sans force ont été épouvantés, et confus, et qu'ils sont devenus [comme] l'herbe des champs, [comme] l'herbe verte, [et] le foin des toits, et [comme] la moisson qui a été touchée de la brûlure, avant qu elle soit crue en épi.
Anthu a kumeneko ndi opanda mphamvu, athedwa nzeru ndipo ali ndi manyazi. Ali ngati mbewu za mʼmunda, ngati udzu wanthete, ali ngati udzu womera pa denga, umene umawuma usanakule nʼkomwe.’”
27 Mais je sais ta demeure, ta sortie et ton entrée, [et] comment tu es forcené contre moi.
“‘Koma Ine ndimadziwa kukhala kwako, kutuluka kwako ndi kulowa kwako, ndi mkwiyo wako pa Ine.
28 Or parce que tu es forcené contre moi, et que ton insolence est montée à mes oreilles, je mettrai ma boucle en tes narines, et mon mors dans tes mâchoires, et je te ferai retourner par le chemin par lequel tu es venu.
Chifukwa chakuti wandikwiyira ndipo ndamva za mwano wako, ndidzakola mphuno yako ndi mbedza ndi kuyika chitsulo changa mʼkamwa mwako, ndipo ndidzakubweza pokudzeretsa njira yomwe unadzera pobwera.’
29 Et ceci te sera pour signe, [ô Ezéchias!] c'est qu'on mangera cette année ce qui viendra de soi-même aux champs; et la seconde année, ce qui croîtra encore sans semer; mais la troisième année, vous sèmerez, et vous moissonnerez; vous planterez des vignes, et vous en mangerez le fruit.
“Koma iwe Hezekiya, chizindikiro chako chidzakhala ichi: “Chaka chino mudzadya tirigu wamphulumukwa, ndipo chaka chamawa mudzadya tirigu wongodzimerera. Koma chaka chachitatu mudzadzala ndi kukolola, mudzawoka mphesa ndipo mudzadya zipatso zake.
30 Et ce qui est réchappé et demeuré de reste dans la maison de Juda, étendra sa racine par dessous, et elle produira son fruit par dessus.
Anthu a nyumba ya Yuda amene adzatsale adzazika mizu ndi kubereka zipatso.
31 Car de Jérusalem sortira quelque reste, et de la montagne de Sion quelques réchappés; la jalousie de l'Eternel des armées fera cela.
Pakuti ku Yerusalemu kudzachokera anthu otsala, ndi ku phiri la Ziyoni kudzachokera gulu la anthu opulumuka.” “Changu cha Yehova Wamphamvuzonse chidzachita zimenezi.
32 C'est pourquoi ainsi a dit l'Eternel touchant le Roi des Assyriens: Il n'entrera point dans cette ville, il n'y jettera même aucune flèche, et il ne se présentera point contr'elle avec le bouclier, et il ne dressera point de terrasse contr'elle.
“Choncho chimene Yehova akunena za mfumu ya ku Asiriya ndi ichi: “‘Iye sadzalowa mu mzinda umenewu kapena kuponyamo muvi. Sadzayandikira mzindawu ndi zishango zake kapena kumanga nthumbira ya nkhondo.
33 Il s'en retournera par le chemin par lequel il est venu, et n'entrera point dans cette ville, dit l'Eternel.
Adzabwerera potsata njira imene anadzera pobwera; sadzalowa mu mzinda umenewu, akutero Yehova.
34 Car je garantirai cette ville, afin de la délivrer, pour l'amour de moi, et pour l'amour de David mon serviteur.
Ndidzateteza mzinda umenewu kuwupulumutsa, chifukwa cha Ine mwini ndiponso chifukwa cha Davide mtumiki wanga.’”
35 Il arriva donc cette nuit-là qu'un Ange de l'Eternel sortit, et tua cent quatre-vingt et cinq mille hommes au camp des Assyriens; et quand on se fut levé de bon matin, voilà, c'étaient tous corps morts.
Usiku umenewo mngelo wa Yehova anapita ku misasa ya ku Asiriya ndi kupha ankhondo 185,000. Ndipo pamene anthu anadzuka mmawa, taonani, mitembo inali ngundangunda!
36 Et Sanchérib Roi des Assyriens partit de là, et s'en alla, et s'en retourna, et se tint à Ninive.
Choncho Senakeribu mfumu ya ku Asiriya anapasula misasa ndi kuchoka. Anabwerera ku Ninive nakakhala kumeneko.
37 Et il arriva, comme il était prosterné dans la maison de Nisroc son Dieu, qu'Adrammélec et Saréetser ses fils le tuèrent avec l'épée, puis ils se sauvèrent au pays d'Ararat; et Esarhaddon son fils régna en sa place.
Tsiku lina, pamene Senakeribu ankapembedza mʼnyumba ya Nisiroki mulungu wake, ana ake Adirameleki ndi Sarezeri anamupha ndi lupanga ndipo anathawira ku dziko la Ararati. Tsono Esrahadoni, mwana wake, analowa ufumu mʼmalo mwake.

< 2 Rois 19 >