< 2 Chroniques 29 >

1 Ezéchias commença à régner étant âgé de vingt-cinq ans; et il régna vingt-neuf ans à Jérusalem. Sa mère avait nom Abija, et elle était fille de Zacharie.
Hezekiya anali wa zaka 25 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 29. Dzina la amayi ake linali Abiya mwana wa Zekariya.
2 Il fit ce qui est droit devant l'Eternel, selon tout ce qu'avait fait David son père.
Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova, monga momwe anachitira Davide abambo ake.
3 La première année de son règne, au premier mois, il ouvrit les portes de la maison de l'Eternel, et les répara.
Pa chaka choyamba cha ulamuliro wake, iye anatsekula zitseko za Nyumba ya Yehova ndipo anazikonza.
4 Il fit venir les Sacrificateurs et les Lévites, il les assembla dans la place Orientale,
Iye analowetsamo ansembe ndi Alevi ndipo anawasonkhanitsa ku bwalo lakummawa
5 Et leur dit: Ecoutez-moi, Lévites; sanctifiez-vous maintenant, et sanctifiez la maison de l'Eternel le Dieu de vos pères, et jetez hors du Sanctuaire les choses souillées.
ndipo anati: “Mverani, inu Alevi! Dziyeretseni tsopano ndiponso muyeretse Nyumba ya Yehova Mulungu wa makolo anu. Muchotse zodetsa zonse ku malo opatulika.
6 Car nos pères ont péché, et ont fait ce qui déplaît à l'Eternel notre Dieu, et l'ont abandonné; et ils ont détourné leurs faces du pavillon de l'Eternel, et lui ont tourné le dos.
Makolo athu anali osakhulupirika ndipo anachita zoyipa pa maso pa Yehova Mulungu wathu ndi kumusiya Yehovayo. Iwo anatembenuka ndi kusiya malo okhalako Yehova ndi kumufulatira.
7 Même ils ont fermé les portes du porche, et ont éteint les lampes, et n'ont point fait de parfum, et n'ont point offert d'holocauste dans le lieu Saint au Dieu d'Israël.
Iwowo anatsekanso zitseko zapakhonde ndi kuzimitsa nyale. Sanafukize lubani kapena kupereka nsembe zopsereza ku malo opatulika a Mulungu wa Israeli.
8 C'est pourquoi l'indignation de l'Eternel a été sur Juda et sur Jérusalem, et il les a livrés à être transportés [d'un lieu à l'autre], et pour être un sujet d'étonnement et de dérision, comme vous le voyez de vos yeux.
Kotero, Yehova anakwiyira Yuda ndi Yerusalemu. Iye anawasandutsa chinthu chochititsa mantha, choopsa ndiponso chonyozedwa monga momwe mukuonera ndi maso anuwa lero lino.
9 Car voici, nos pères sont tombés par l'épée; nos fils, nos filles, et nos femmes sont en captivité à cause de cela.
Ichi nʼchifukwa chake makolo athu anaperekedwa ku lupanga ndipo nʼchifukwa chake ana athu aamuna ndi aakazi ndi akazi athu ali ku ukapolo.
10 Maintenant donc j'ai dessein de traiter alliance avec l'Eternel le Dieu d'Israël, et l'ardeur de sa colère se détournera de nous.
Tsono ine ndikuganiza zochita pangano ndi Yehova Mulungu wa Israeli, kuti mkwiyo wake woopsawu utichokere.
11 Or, mes enfants, ne vous abusez point; car l'Eternel vous a choisis afin que vous vous teniez devant lui pour le servir, et pour être ses ministres, et lui faire le parfum.
Ana anga, musanyalanyaze tsopano, pakuti Yehova wakusankhani kuti muziyima pamaso pake ndi kumutumikira Iye, kugwira ntchito pamaso pake ndi kufukiza lubani.”
12 Les Lévites donc se levèrent, [savoir] Mahath fils de Hamasaï, et Joël fils de Hazaria, d'entre les enfants des Kehathites; et des enfants de Mérari, Kis fils de Habdi, et Hazaria fils de Jahalleleël; et des Guersonites, Joah fils de Zimma, et Héden fils de Joah;
Ndipo Alevi awa anakonzeka kugwira ntchito: Kuchokera ku banja la Kohati, Mahati mwana wa Amasai ndi Yoweli mwana wa Azariya; kuchokera ku banja la Merari, Kisi mwana wa Abidi ndi Azariya mwana wa Yehaleleli; kuchokera ku banja la Geresoni, Yowa mwana wa Zima ndi Edeni mwana wa Yowa;
13 Et des enfants d'Elitsaphan, Simri et Jéhiël; et des enfants d'Asaph, Zacharie, et Mattania;
kuchokera kwa zidzukulu za Elizafani, Simiri ndi Yeiyeli; kuchokera kwa zidzukulu za Asafu, Zekariya ndi Mataniya;
14 Et des enfants d'Hémad, Jéhiël, et Simhi; et des enfants de Jéduthun, Sémahia et Huziël.
kuchokera kwa zidzukulu za Hemani, Yehieli ndi Simei; kuchokera kwa zidzukulu za Yedutuni, Semaya ndi Uzieli.
15 Lesquels assemblèrent leurs frères, et se sanctifièrent, et ils entrèrent selon le commandement du Roi, conformément à la parole de l'Eternel, pour nettoyer la maison de l'Eternel.
Atasonkhanitsa abale awo ndi kudziyeretsa, iwo anapita kukayeretsa Nyumba ya Yehova, monga inalamulira mfumu, potsatira mawu a Yehova.
16 Ainsi les Sacrificateurs entrèrent dans la maison de l'Eternel, afin de la nettoyer, et portèrent dehors, au parvis de la maison de l'Eternel, toutes les choses immondes qu'ils trouvèrent au Temple de l'Eternel, lesquelles les Lévites prirent pour les emporter au torrent de Cédron.
Ansembe analowa ku malo opatulika a Yehova kukayeretsako. Anatulutsira ku bwalo la Nyumba ya Yehova chilichonse chodetsedwa chimene anachipeza mʼNyumba ya Yehova. Alevi anatenga zimenezo ndi kupita nazo ku chigwa cha Kidroni.
17 Et ils commencèrent à sanctifier [le Temple] le premier jour du premier mois; et le huitième jour du même mois ils entrèrent au porche de l'Eternel, et sanctifièrent la maison de l'Eternel pendant huit jours; et le seizième jour de ce premier mois ils eurent achevé.
Iwo anayamba mwambo woyeretsawu tsiku loyamba la mwezi woyamba ndipo pa tsiku lachisanu ndi chitatu la mweziwo anafika pa khonde la nyumba ya Yehova. Tsono anachita mwambo woyeretsa Nyumba ya Yehova ija masiku asanu ndi atatu, ndipo anamaliza pa tsiku la 16 mwezi woyamba.
18 Puis ils entrèrent dans la chambre du Roi Ezéchias, et dirent: Nous avons nettoyé toute la maison de l'Eternel, et l'autel des holocaustes, avec ses ustensiles; et la table des pains de proposition, avec tous ses ustensiles.
Ndipo anapita kwa mfumu Hezekiya ndi kukafotokoza kuti, “Ife tayeretsa Nyumba ya Mulungu yonse, guwa lansembe zopsereza ndi ziwiya zake zonse, ndiponso tebulo limene timayikapo buledi wopatulika pamodzi ndi zinthu zake zonse.
19 Et nous avons dressé et sanctifié tous les ustensiles que le Roi Achaz avait écartés durant son règne, dans le temps qu'il a péché, et voici, ils sont devant l'autel de l'Eternel.
Takonza ndi kuyeretsa zinthu zonse zimene mfumu Ahazi anazichotsa mwa kusakhulupirika kwake pamene anali mfumu. Taziyika kutsogolo kwa guwa la Yehova.”
20 Alors le Roi Ezéchias se levant dès le matin, assembla les principaux de la ville, et monta dans la maison de l'Eternel.
Mmamawa tsiku linalo, mfumu Hezekiya inasonkhanitsa pamodzi akuluakulu a mu mzindawo ndipo inapita ku Nyumba ya Yehova.
21 Et ils amenèrent sept veaux, sept béliers, sept agneaux, et sept boucs sans tare, [afin de les offrir] en sacrifice pour le péché, pour le Royaume, et pour le Sanctuaire, et pour Juda. Puis [le Roi] dit aux Sacrificateurs fils d'Aaron, qu'ils les offrissent sur l'autel de l'Eternel.
Iwo anabweretsa ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri ndi nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri, ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri, mbuzi zazimuna zisanu ndi ziwiri monga nsembe zoperekedwa chifukwa cha tchimo la ufumu, la malo opatulika ndi Yuda. Tsono mfumu inalamula ansembe, zidzukulu za Aaroni, kuti apereke zimenezi pa guwa lansembe la Yehova.
22 Et ainsi ils égorgèrent les veaux, et les Sacrificateurs en reçurent le sang, et le répandirent vers l'autel. Ils égorgèrent aussi les béliers, et en répandirent le sang vers l'autel; ils égorgèrent aussi les agneaux, et en répandirent le sang vers l'autel.
Choncho anthuwo anapha ngʼombe zazimunazo ndipo ansembe anatenga magazi ake ndi kuwawaza pa guwa lansembe, kenaka anapha nkhosa zazimuna zija ndipo anawaza magazi ake pa guwa lansembe; anaphanso ana ankhosa aja ndipo anawaza magazi ake pa guwa lansembe.
23 Puis on fit approcher les boucs pour le péché devant le Roi et devant l'assemblée, et ils posèrent leurs mains sur eux.
Mbuzi zoperekedwa chifukwa cha tchimo zija zinabweretsedwa pamaso pa mfumu ndi anthu onse, ndipo anasanjika manja awo pa izo.
24 Alors les Sacrificateurs les égorgèrent, et offrirent en expiation leur sang vers l'autel, afin de faire propitiation pour tout Israël; car le Roi avait ordonné cet holocauste et ce sacrifice pour le péché, pour tout Israël.
Kenaka ansembe anapha mbuzizo ndipo anapereka magazi ake pa guwa, kuti ukhale mwambo wofafanizira machimo a Aisraeli onse, pakuti mfumu inalamula kuti nsembe yopsereza ndi yopepesera machimo zichitike chifukwa cha Aisraeli onse.
25 Il fit aussi que les Lévites se tinssent en la maison de l'Eternel, avec des cymbales, des musettes, et des violons, selon le commandement de David, et de Gad le Voyant du Roi, et de Nathan le Prophète; car ce commandement [avait été donné] de la part de l'Eternel, par ses Prophètes.
Iye anayika Alevi mʼNyumba ya Yehova ali ndi ziwaya za malipenga, azeze ndi apangwe potsata lamulo la Davide, Gadi mlosi wa mfumu ndi mneneri Natani. Pakuti Yehova ndiye analamula zimenezi kudzera mwa aneneri.
26 Les Lévites donc y assistèrent avec les instruments de David, et les Sacrificateurs avec les trompettes.
Kotero Alevi anayima okonzekera atanyamula zoyimbira za Davide ndiponso ansembe atanyamula malipenga awo.
27 Alors Ezéchias commanda qu'on offrît l'holocauste sur l'autel; et à l'heure qu'on commença l'holocauste, le cantique de l'Eternel commença avec les trompettes, et avec les instruments ordonnés par David Roi d'Israël.
Hezekiya analamulira kuti apereke nsembe zopsereza pa guwa. Pamene amayamba kupereka nsembezo, kuyimbira Yehova kunayambikanso, pamodzi ndi malipenga ndi zipangizo zoyimbira za Davide mfumu ya Israeli.
28 Et toute l'assemblée était prosternée, et le cantique se chantait, et les trompettes sonnaient; et cela continua jusqu'à ce qu'on eût achevé d'offrir l'holocauste.
Anthu onse anawerama pansi ndi kulambira, pamene oyimba amayimba ndi malipenga. Izi zonse zinapitirira mpaka pa mapeto pa nsembe zopsereza.
29 Et quand on eut achevé d'offrir [l'holocauste], le Roi et tous ceux qui se trouvèrent avec lui s'inclinèrent et se prosternèrent.
Zopereka zitatha, mfumu ndi wina aliyense amene anali naye anagwada pansi ndi kulambira.
30 Puis le Roi Ezéchias et les principaux dirent aux Lévites, qu'ils louassent l'Eternel suivant les paroles de David, et d'Asaph le Voyant; et ils louèrent [l'Eternel] jusqu'à tressaillir de joie, et ils s'inclinèrent, et se prosternèrent.
Mfumu Hezekiya ndi akuluakulu ake analamulira Alevi kuti atamande Yehova potsata mawu a Davide ndi mlosi Asafu. Kotero anayimba nyimbo zamatamando mokondwera ndipo anaweramitsa mitu yawo ndi kulambira.
31 Alors Ezéchias prit la parole, et dit: Vous avez maintenant consacré vos mains à l'Eternel, approchez-vous, et offrez des sacrifices, et des louanges dans la maison de l'Eternel. Et ainsi l'assemblée offrit des sacrifices et des louanges, et tous ceux qui étaient d'un cœur volontaire [offrirent] des holocaustes.
Kenaka Hezekiya anati, “Inu mwadzipereka tsopano kwa Yehova. Bwerani ndipo mufike ndi nsembe ndi zopereka zachiyamiko ku Nyumba ya Yehova.” Choncho anthu onse anabweretsa nsembe ndi zopereka zachiyamiko, ndipo anthu onse amene anali ofuna mu mtima mwawo anabweretsa nsembe zopsereza.
32 Or le nombre des holocaustes que l'assemblée offrit, fut de soixante-dix bœufs, cent moutons, deux cents agneaux, le tout en holocauste à l'Eternel.
Chiwerengero cha nsembe zopsereza chimene anthu onse anabweretsa chinali ngʼombe zazimuna makumi asanu ndi awiri, nkhosa zazimuna 100, ana ankhosa aamuna 200 ndipo zonsezi zinali za nsembe yopsereza kwa Yehova.
33 Et les [autres] choses consacrées furent, six cents bœufs, et trois mille moutons.
Ziweto zimene zinapatulidwa kukhala nsembe zinalipo ngʼombe zazimuna 600, nkhosa ndi mbuzi 3,000.
34 Mais les Sacrificateurs étaient en petit nombre, de sorte qu'ils ne purent pas écorcher tous les holocaustes; c'est pourquoi les Lévites leurs frères les aidèrent, jusqu'à ce que cet ouvrage fût achevé, et que les [autres] Sacrificateurs se fussent sanctifiés; parce que les Lévites [furent] d'un cœur plus droit que les Sacrificateurs, pour se sanctifier.
Koma ansembe anali ochepa kuti asende zonse zopsereza. Choncho abale awo Alevi anawathandiza mpaka ntchito yonse inatha ndipo mpaka ansembe ena atadziyeretsa, pakuti Alevi anachita changu kudziyeretsa kulekana ndi momwe anachitira ansembe.
35 Et il y eut aussi un grand nombre d'holocaustes, avec les graisses des sacrifices de prospérités, et avec les aspersions des holocaustes. Ainsi le service de la maison de l'Eternel fut rétabli.
Panali nsembe zopsereza zochuluka, pamodzi ndi mafuta a nsembe yachiyanjano ndi nsembe yachakumwa imene imachitika pamodzi ndi nsembe yopsereza. Kotero ntchito ya mʼNyumba ya Mulungu inakhazikitsidwanso.
36 Et Ezéchias et tout le peuple se réjouirent de ce que Dieu avait disposé le peuple; car la chose fut faite promptement.
Hezekiya ndi anthu onse anakondwera pa zimene Mulungu anachitira anthu ake, chifukwa zinachita mwamsangamsanga.

< 2 Chroniques 29 >