< 2 Chroniques 26 >

1 Alors tout le peuple de Juda prit Hozias, qui était âgé de seize ans, et ils l'établirent Roi en la place d'Amatsia son père.
Kenaka anthu onse a ku Yuda anatenga Uziya amene anali wa zaka 16, namuyika kukhala mfumu mʼmalo mwa Amaziya abambo ake.
2 Il bâtit Eloth, l'ayant remise en la puissance de Juda, après que le Roi se fut endormi avec ses pères.
Iye anamanganso mzinda wa Eloti ndi kuwubwezeranso ku Yuda abambo ake atamwalira.
3 Hozias [était] âgé de seize ans quand il commença à régner, et régna cinquante-deux ans à Jérusalem. Sa mère avait nom Jécolia, [et] elle était de Jérusalem.
Uziya anali wa zaka 16 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 70. Dzina la amayi ake linali Yekoliya wa ku Yerusalemu.
4 Il fit ce qui est droit devant l'Eternel, comme avait fait Amatsia son père.
Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova, monga momwe anachitira Amaziya abambo ake.
5 Il s'appliqua à rechercher Dieu pendant les jours de Zacharie, [homme] intelligent dans les visions de Dieu; et pendant les jours qu'il rechercha l'Eternel, Dieu le fit prospérer.
Iye anapembedza Mulungu nthawi ya Zekariya, amene ankamulangiza za kuopa Mulungu amene anamupatsa chipambano.
6 Car il sortit et fit la guerre contre les Philistins, et fit brèche à la muraille de Gath, et à la muraille de Jabné, et à la muraille d'Asdod; et il bâtit des villes [dans le pays] d'Asdod, et entre les [autres] Philistins.
Iyeyo anapita kukachita nkhondo ndi Afilisti ndipo anagwetsa makoma a Gati, Yabine ndi Asidodi. Ndipo kenaka anamanganso mizinda ya pafupi ndi Asidodi ndi malo ena pafupi ndi Afilisti.
7 Et Dieu lui donna du secours contre les Philistins, et contre les Arabes qui habitaient à Gur-bahal, et contre les Méhunites.
Mulungu anamuthandiza polimbana ndi Afilisti ndi Aarabu amene amakhala ku Guri-Baala ndiponso polimbana ndi Ameuni.
8 Et même les Hammonites donnaient des présents à Hozias; de sorte que sa réputation se répandit jusqu'à l'entrée d'Egypte; car il s'était rendu fort puissant.
Aamoni ankabweretsa msonkho kwa Uziya ndipo mbiri yake inamveka mpaka ku malire a dziko la Igupto chifukwa anali wamphamvu kwambiri.
9 Et Hozias bâtit des tours à Jérusalem, sur la porte du coin, et sur la porte de la vallée, et sur l'encoignure, et les fortifia.
Uziya anamanga nsanja ku Yerusalemu ku Chipata Chapangodya, ku Chigwa cha Chipata ndi pokhotera mpanda, ndipo anayikamo chitetezo.
10 Il bâtit aussi des tours au désert, et creusa plusieurs puits, parce qu'il avait beaucoup de bétail dans la plaine et dans la campagne; et des laboureurs et des vignerons dans les montagnes, et en Carmel; car il aimait l'agriculture.
Iye anamanganso nsanja ku chipululu ndi kukumbanso zitsime zambiri chifukwa anali ndi ziweto zambiri mʼmbali mwa phiri ndi ku zigwa. Iye anali ndi anthu amene ankagwira ntchito mʼminda yake ndiponso mʼminda yake ya mphesa mʼphiri ndi malo achonde, pakuti ankakonda nthaka.
11 Et Hozias avait une armée composée de gens dressés à la guerre, qui marchaient en bataille par bandes, selon le compte de leur dénombrement, fait par Jéhiël scribe, et Mahaséja prévôt, sous la conduite de Hanania, l'un des principaux capitaines du Roi.
Uziya anali ndi gulu lankhondo lophunzitsidwa bwino, lokonzekera kupita ku nkhondo mʼmagulu monga mwa chiwerengero chawo chimene mlembi Yeiyeli ndi Maaseya anasonkhanitsa motsogozedwa ndi Hananiya mmodzi mwa akuluakulu a mfumu.
12 Tout le nombre des Chefs des pères, d'entre ceux qui étaient forts et vaillants, était de deux mille et six cents.
Chiwerengero chonse cha atsogoleri a mʼmabanja oyangʼanira anthu ochita nkhondo chinali 2,600.
13 Et il y avait sous leur conduite une armée de trois cent sept mille et cinq cents combattants, tous gens aguerris, forts et vaillants, pour aider le Roi contre l'ennemi.
Pansi pa ulamuliro wawo panali asilikali 307,500 ophunzitsidwa nkhondo, gulu lamphamvu lothandiza mfumu kulimbana ndi adani ake.
14 Et Hozias leur prépara, [savoir] à toute cette armée-là, des boucliers, des javelines, des casques, des cuirasses, des arcs, et des pierres de fronde.
Uziya anawapangira asilikaliwo zishango, mikondo, zipewa zankhondo, malaya ankhondo achitsulo, mauta ndi miyala yogendera.
15 Et il fit à Jérusalem des machines de l'invention d'un ingénieur, afin qu'elles fussent sur les tours, et sur les coins, pour jeter des flèches, et de grosses pierres. Ainsi sa réputation alla fort loin; car il fut extrêmement aidé jusqu'à ce qu'il fût devenu fort puissant.
Mu Yerusalemu anapanga makina okonzedwa ndi anthu aluso amene amagwiritsidwa ntchito pa malo otetezera a pa nsanja ndi pa ngodya kuponyera mivi ndi kugubuduzira miyala. Mbiri yake inamveka kutali ndi ponseponse pakuti anathandizidwa kwambiri mpaka anakhala wamphamvu kwambiri.
16 Mais sitôt qu'il fut devenu fort puissant, son cœur s'éleva pour sa perte, et il commit un [grand] péché contre l'Eternel son Dieu; car il entra dans le Temple de l'Eternel pour faire le parfum sur l'autel des parfums.
Koma pamene Uziya anakhala wamphamvu kwambiri, kunyada kwake kunamuwononga. Iye sanakhulupirike kwa Yehova Mulungu wake, ndipo analowa mʼNyumba ya Yehova kukafukiza lubani pa guwa lofukizira.
17 Mais Hazaria le Sacrificateur [y] entra après lui, accompagné des Sacrificateurs de l'Eternel, au nombre de quatre-vingts vaillants hommes;
Wansembe Azariya pamodzi ndi ansembe a Yehova ena 80 olimba mtima anamutsatira.
18 Qui s'opposèrent au Roi Hozias, et lui dirent: Hozias! il ne t'appartient pas de faire le parfum à l'Eternel; car cela appartient aux Sacrificateurs, fils d'Aaron, qui sont consacrés pour faire le parfum. Sors du Sanctuaire, car tu as péché; et ceci ne te sera point honorable de la part de l'Eternel Dieu.
Iwo anatsutsana naye ndipo anati, “Sibwino kuti inu mfumu muzifukiza lubani koma zidzukulu za Aaroni, zimene zinapatulidwa kuti zizifukiza lubani. Chokani pa malo opatulika ano, pakuti inu mwakhala osakhulupirika, ndipo simudzalemekezedwa ndi Yehova Mulungu.”
19 Alors Hozias, qui avait en sa main le parfum pour faire des encensements, se mit en colère; et comme il s'irritait contre les Sacrificateurs, la lèpre s'éleva sur [son] front, en la présence des Sacrificateurs, dans la maison de l'Eternel, près de l'autel des parfums.
Uziya, amene anali ndi chofukizira mʼmanja mwake wokonzeka kuti afukize lubani, anapsa mtima. Iye anakwiyira ansembewo. Ndipo ansembe aja akuona patsogolo pa guwa lofukizira lubani mʼNyumba ya Mulungu, khate linayamba pamphumi pake.
20 Alors Hazaria le principal Sacrificateur le regarda avec tous les sacrificateurs, et voilà, il était lépreux en son front, et ils le firent incessamment sortir; et il se hâta de sortir, parce que l'Eternel l'avait frappé.
Azariya, mkulu wa ansembe pamodzi ndi ansembe ena onse atamuyangʼana anaona kuti anali ndi khate pamphumi pake, ndipo anamutulutsa mofulumira. Ndipo iye mwini anafulumira kutuluka, chifukwa Yehova anamulanga.
21 Et ainsi le Roi Hozias fut lépreux, jusqu'au jour qu'il mourut; et il demeura lépreux dans une maison écartée; même il fut retranché de la maison de l'Eternel, et Jotham son fils avait la charge de la maison du Roi, jugeant le peuple du pays.
Mfumu Uziya anali ndi khate mpaka tsiku limene anamwalira. Iye amakhala mʼnyumba ya yekha ngati wakhate, ndipo samalowa mʼNyumba ya Yehova. Yotamu mwana wake ndiye amayangʼanira nyumba yaufumu ndipo ankalamulira anthu a mʼdzikomo.
22 Or Esaïe fils d'Amots, Prophète, a écrit le reste des faits d'Hozias, tant les premiers que les derniers.
Ntchito zina za mfumu Uziya, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, zinalembedwa ndi mneneri Yesaya mwana wa Amozi.
23 Et Hozias s'endormit avec ses pères, et fut enseveli avec eux dans le champ des sépulcres des Rois; car, ils dirent, il est lépreux; et Jotham son fils régna en sa place.
Uziya analondola makolo ake, ndipo anamuyika pamodzi ndi makolo ake ku malo a manda a mafumu, koma osati mʼmanda mwawomo poti anthu anati, “Iyeyu anali ndi khate.” Ndipo Yotamu mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.

< 2 Chroniques 26 >