< 1 Samuel 2 >

1 Alors Anne pria, et dit: Mon cœur s'est réjoui en l'Eternel; ma corne a été élevée par l'Eternel; ma bouche s'est ouverte sur mes ennemis, parce que je me suis réjouie de ton salut.
Ndipo Hana anapemphera nati, “Moyo wanga ukukondwera mwa Yehova; Ndiyenda mwa tukumutukumu chifukwa cha Yehova. Pakamwa panga pakula ndi kuseka adani anga mowanyogodola. Ndikukondwa chifukwa mwandipulumutsa.
2 Il n'y a nul saint comme l'Eternel; car il n'y en a point d'autre que toi, et il n'y a point de Rocher tel que notre Dieu.
“Palibe wina woyera ngati Yehova, palibe wina koma inu nokha, palibe thanthwe lofanana ndi Mulungu wathu.
3 Ne proférez point tant de paroles hautaines, hautaines; qu'il ne sorte point de votre bouche des paroles rudes; car l'Eternel est le [Dieu] Fort des sciences; c'est à lui à peser les entreprises.
“Musandiyankhulenso modzitama, pakamwa panu pasatuluke zonyada, pakuti Yehova ndi Mulungu wanzeru, ndipo ndiye amene amayesa ntchito za anthu onse.
4 L'arc des forts a été brisé; mais ceux qui ne faisaient que chanceler, ont été ceints de force.
“Mauta a anthu ankhondo athyoka koma anthu ofowoka avala dzilimbe.
5 Ceux qui avaient accoutumé d'être rassasiés, se sont loués pour du pain; mais les affamés ont cessé [de l'être], et même la stérile en a enfanté sept; et celle qui avait beaucoup de fils est devenue languissante.
Amene kale anali okhuta tsopano akukagula chakudya, koma iwo amene anali ndi njala sakumvanso njala. Amene anali wosabereka, wabereka ana aamuna asanu ndi awiri, koma iye wobereka ana ambiri watsala yekha.
6 L'Eternel est celui qui fait mourir, et qui fait vivre; qui fait descendre au sépulcre, et qui [en] fait remonter. (Sheol h7585)
“Yehova amabweretsa imfa ndipo amaperekanso moyo, amatsitsira ku manda ndipo amawatulutsakonso. (Sheol h7585)
7 L'Eternel appauvrit, et enrichit; il abaisse et il élève.
Yehova amasaukitsa ndipo amalemeretsa, amatsitsa ndipo amakweza.
8 Il élève le pauvre de la poudre, et il tire le misérable de dessus le fumier, pour le faire asseoir avec les principaux, et il leur donne en héritage un trône de gloire; car les fondements de la terre sont à l'Eternel, et il a posé sur eux la terre habitable.
Iye amakweza osauka kuwachotsa pa fumbi, ndipo amachotsa anthu osowa pa dzala. Iye amawakhazika pamodzi ndi ana a mafumu, amawapatsa mpando waulemu. “Pakuti nsanamira za dziko lapansi ndi za Yehova, anakhazika dziko lapansi pa nsanamirazo.
9 Il gardera les pieds de ses bien-aimés, et les méchants se tairont dans les ténèbres; car l'homme ne sera point le plus fort par sa force.
Iye adzateteza moyo wa anthu okhulupirika koma anthu oyipa adzawonongedwa mu mdima. “Pakuti munthu sapambana ndi mphamvu zake.
10 Ceux qui contestent contre l'Eternel seront froissés; il tonnera des cieux sur chacun d'eux; l'Eternel jugera les bouts de la terre; et il donnera la force à son Roi, et élèvera la corne de son oint.
Yehova adzaphwanya omutsutsa. Adzawaopsa ndi bingu kuchokera kumwamba; Yehova adzaweruza mathero a dziko lapansi. “Koma adzapereka mphamvu kwa mfumu yake, adzakuza mphamvu za odzozedwa wake.”
11 Puis Elkana s'en alla à Rama en sa maison, et le jeune garçon vaquait au service de l'Eternel, en la présence d'Héli le Sacrificateur.
Tsono Elikana anapita ku mudzi kwawo ku Rama, koma mnyamatayo amatumikira Yehova pansi pa ulamuliro wa wansembe Eli.
12 Or les fils d'Héli étaient de méchants hommes; ils ne connaissaient point l'Eternel,
Ana a Eli anali ana achabechabe pakuti samasamala za Yehova.
13 Car le train ordinaire de ces Sacrificateurs-là envers le peuple, [était, que] quand quelqu'un faisait quelque sacrifice, le garçon du Sacrificateur venait lorsqu'on faisait bouillir la chair, ayant en sa main une fourchette à trois dents,
Ndipo chizolowezi cha ansembe pakati pa anthu chinali motere kuti pamene munthu aliyense ankapereka nsembe ndipo nyama ija ikuwira pa moto, mtumiki wa wansembe ankabwera ndi chifoloko cha mano atatu mʼdzanja lake.
14 Avec laquelle il frappait dans la chaudière, ou dans le chauderon, ou dans la marmite, ou dans le pot; [et] le Sacrificateur prenait pour soi tout ce que la fourchette enlevait; ils en faisaient ainsi à tous ceux d'Israël qui venaient là à Silo.
Iye ankachipisa mu mʼphikamo, ndipo wansembeyo amatenga chilichonse chimene folokoyo yabaya. Umu ndi mmene ansembewo amachitira ndi Aisraeli onse amene amabwera ku Silo.
15 Même avant qu'on fît fumer la graisse, le garçon du Sacrificateur venait, et disait à l'homme qui sacrifiait: Donne-moi de la chair à rôtir pour le Sacrificateur; car il ne prendra point de toi de chair bouillie, mais de la chair crue.
Ndipo ngakhale mafuta asanatenthedwe, mtumiki wansembe amabwera ndi kunena kwa munthu amene akupereka nsembeyo kuti, “Ndipatse nyama kuti ndiwotche, pakuti Yehova salandira nyama yophika koma yayiwisi.”
16 Que si l'homme lui répondait: Qu'on ne manque pas de faire fumer tout présentement la graisse; et après cela prends ce que ton âme souhaitera; alors il lui disait: Quoi qu'il en soit, tu en donneras maintenant; et si tu ne m'en donnes, j'en prendrai par force.
Ngati munthuyo anena kuti, “Apseretu mafuta poyamba, ndipo kenaka mutenge mmene mufunira,” mtumikiyo amayankha kuti, “Ayi ndipatse tsopano lino. Ngati sutero, ine nditenga molanda.”
17 Et le péché de ces jeunes hommes fut très-grand devant l'Eternel; car les gens en méprisaient l'oblation de l'Eternel.
Tchimo la ana a Eli linali lalikulu kwambiri pamaso pa Yehova pakuti iwo amanyoza nsembe za Yehova.
18 Or Samuel servait en la présence de l'Eternel, étant jeune garçon, vêtu d'un Ephod de lin.
Koma Samueli amatumikira pamaso pa Yehova atavala efodi ya nsalu yofewa yosalala.
19 Sa mère lui faisait un petit roquet, qu'elle lui apportait tous les ans, quand elle montait avec son mari pour offrir le sacrifice solennel.
Chaka chilichonse amayi ake ankamusokera kamkanjo ndi kukamupatsa akamapita ndi mwamuna wake kukapereka nsembe za pa chaka.
20 Et Héli bénit Elkana et sa femme, et dit: L'Eternel te fasse avoir des enfants de cette femme, pour le prêt qui a été fait à l'Eternel. Et ils s'en retournèrent chez eux.
Tsono Eli amadalitsa Elikana ndi mkazi wake ndi mawu akuti “Yehova akupatseni ana mwa mkazi uyu kulowa mʼmalo mwa amene anapempha ndi kumupereka kwa Yehova.”
21 Et l'Eternel visita Anne, laquelle conçut et enfanta trois fils et deux filles; et le jeune garçon Samuel devint grand en la présence de l'Eternel.
Ndipo Yehova anamukomera mtima Hana. Anakhala ndi pathupi ndi kubereka ana aamuna atatu ndi ana aakazi awiri. Ndipo Samueli ankakula pamaso pa Yehova.
22 Or Héli était fort vieux, et il apprit tout ce que faisaient ses fils à tout Israël, et qu'ils couchaient avec les femmes qui s'assemblaient par troupes à la porte du Tabernacle d'assignation.
Tsono Eli anakalamba kwambiri. Iye ankamva zonse zimene ana ake aamuna ankachitira Aisraeli onse, ndiponso kuti ankagona ndi akazi pa chipata cha tenti ya msonkhano.
23 Et il leur dit: Pourquoi faites-vous ces actions-là? car j'apprends vos méchantes actions; ces choses [me viennent] de tout le peuple.
Choncho anawafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani mukuchita zinthu zotere? Ine ndikumva kuchokera kwa anthu onse za zoyipa zanuzo.
24 Ne faites pas ainsi, mes fils; car ce que j'entends dire de vous n'est pas bon; vous faites pécher le peuple de l'Eternel.
Ayi, ana anga si mbiri yabwino imene ndikumva anthu a Mulungu akufalitsa.
25 Si un homme a péché contre un autre homme, le Juge en jugera; mais si quelqu'un pèche contre l'Eternel, qui est-ce qui priera pour lui? Mais ils n'obéirent point à la voix de leur père, parce que l'Eternel voulait les faire mourir.
Ngati munthu alakwira munthu mnzake, mwina Mulungu adzamupepesera, koma ngati munthu achimwira Yehova adzamupepesera ndani?” Koma ana ake sanamvere kudzudzula kwa abambo awo, pakuti chinali cholinga cha Yehova kuti awaphe.
26 Cependant le jeune garçon Samuel croissait et il était agréable à l'Eternel et aux hommes.
Ndipo mnyamata Samueli anapitirira kukula mu msinkhu, ndipo ankapeza kuyanja pamaso pa Yehova ndi anthu.
27 Or un homme de Dieu vint à Héli, et lui dit: Ainsi a dit l'Eternel: Ne me suis-je pas clairement manifesté à la maison de ton père, quand ils étaient en Egypte, en la maison de Pharaon?
Tsiku lina munthu wa Mulungu anabwera kwa Eli ndipo anamuwuza kuti, “Yehova akuti, ‘Kodi Ine sindinadziwulule ndekha kwa banja la kholo lako pamene iwo anali akapolo a Farao ku Igupto?
28 Je l'ai aussi choisi d'entre toutes les Tribus d'Israël pour être mon Sacrificateur, afin d'offrir sur mon autel, [et] faire fumer les parfums, [et] porter l'Ephod devant moi; et j'ai donné à la maison de ton père toutes les oblations des enfants d'Israël faites par le feu.
Ndipo ndinamusankha pakati pa mafuko a Israeli kuti akhale wansembe wanga ndi kuti azipita pa guwa langa la nsembe, kufukiza Lubani ndi kuvala efodi pamaso panga. Ndinapatsa banja la abambo ako gawo la nsembe zonse zopsereza zimene Aisraeli amapereka.
29 Pourquoi avez-vous regimbé contre mon sacrifice, et contre mon oblation que j'ai commandé de faire dans le Tabernacle? et [pourquoi] as-tu honoré tes fils plus que moi, pour vous engraisser du meilleur de toutes les offrandes d'Israël mon peuple?
Nʼchifukwa chiyani ukunyoza nsembe ndi zopereka zanga zimene ndinalamula? Nʼchifukwa chiyani ukupereka ulemu kwa ana ako kuposa Ine podzinenepetsa nokha ndi zopereka zabwino kwambiri za nsembe zimene Aisraeli amapereka?’”
30 C'est pourquoi l'Eternel le Dieu d'Israël dit: J'avais dit certainement que ta maison et la maison de ton père marcheraient devant moi éternellement; mais maintenant l'Eternel dit: Il ne sera pas dit que je fasse cela; car j'honorerai ceux qui m'honorent, mais ceux qui me méprisent seront traités avec le dernier mépris.
“Paja Ine Yehova Mulungu wa Israeli ‘Ndinalonjeza kuti anthu a pa banja lako ndi a pa banja la abambo ako azidzanditumikira nthawi zonse.’ Koma tsopano ndikuti, ‘Zonsezi zithe!’ Tsopano anthu amene amandilemekeza Inenso ndidzawalemekeza koma iwo amene amandinyoza Ine ndidzawanyoza.
31 Voici les jours viennent que je couperai ton bras, et le bras de la maison de ton père, tellement qu'il n'y aura aucun homme en ta maison qui devienne vieux.
Nthawi ikubwera imene ndidzachotsa anyamata ako ndi anyamata a pa banja la abambo ako, kotero kuti sipadzakhala munthu wokalamba pa banja lako.
32 Et tu verras un adversaire [établi dans] le Tabernacle, au temps que [Dieu] enverra toute sorte de biens à Israël; et il n'y aura jamais en ta maison aucun homme qui devienne vieux.
Pa mavuto ako udzayangʼana ndi maso ansanje zabwino zimene ndidzachitira Aisraeli ena. Mʼbanja lako simudzapezeka munthu wokalamba.
33 Et celui [de tes descendants que] je n'aurai point retranché d'auprès de mon autel, sera pour faire défaillir tes yeux, et affliger ton âme; et tous les enfants de ta maison mourront en la fleur de l'âge.
Komabe pa banja lako mmodzi yekha ndidzamuleka wosamuchotsa kuti azidzanditumikira. Iyeyu azidzakuliritsa ndi kukumvetsa chisoni. Koma ena onse pa banja lako adzafa akanali aangʼono.”
34 Et ceci t'en sera le signe, [savoir] ce qui arrivera à tes deux fils, Hophni et Phinées, c'est qu'ils mourront tous deux en un même jour.
“‘Ndipo chimene chidzachitike kwa ana ako awiriwa, Hofini ndi Finehasi, chidzakhala chizindikiro kwa iwe. Onse awiri adzafa pa tsiku limodzi.
35 Et je m'établirai un Sacrificateur assuré; il fera selon ce qui est en mon cœur, et selon mon âme; et je lui édifierai une maison assurée, et il marchera à toujours devant mon Oint.
Pambuyo pake ndidzasankha wansembe wokhulupirika, amene adzachita zimene zili mu mtima ndi mʼmaganizo mwanga. Ndidzakhazikitsa banja lako kolimba ndipo adzatumikira pamaso pa wodzozedwa wanga nthawi zonse.
36 Et il arrivera que quiconque sera resté de ta maison, viendra se prosterner devant lui pour avoir une pièce d'argent, [et] quelque pain, et dira: Donne-moi une place, je te prie, dans quelqu'une des charges de la Sacrificature, pour manger un morceau de pain.
Ndipo aliyense wotsala wa banja lako adzabwera ndi kugwada pamaso pake kupempha ndalama kapena chakudya.’ Adzati, ‘Chonde ndiloleni kuti ndizithandizako pa ntchito iliyonse ya unsembe kuti ndipeze chakudya.’”

< 1 Samuel 2 >