< 1 Jean 4 >
1 Mes bien-aimés, ne croyez point à tout esprit; mais éprouvez les esprits, [pour savoir] s'ils sont de Dieu; car plusieurs faux prophètes sont venus au monde.
Anzanga okondedwa, musakhulupirire mzimu uliwonse, koma yesani mizimu ngati ikuchokera kwa Mulungu, chifukwa aneneri onama ambiri afalikira mʼdziko lapansi.
2 Connaissez à cette marque l'Esprit de Dieu: tout esprit qui confesse que Jésus-Christ est venu en chair, est de Dieu.
Mungathe kuzindikira Mzimu wa Mulungu motere: Mzimu uliwonse umene umavomereza kuti Yesu Khristu anabwera mʼthupi, ndi wochokera kwa Mulungu,
3 Et tout esprit qui ne confesse point que Jésus-Christ est venu en chair, n'est point de Dieu; or tel est l'esprit de l'Antechrist, duquel vous avez ouï dire qu'il viendra; et il est même déjà maintenant au monde.
koma mzimu uliwonse umene suvomereza Yesu, siwochokera kwa Mulungu. Uwu ndi mzimu wa wokana Khristu umene munawumva kuti ukubwera ndipo ngakhale tsopano wabwera kale mʼdziko lapansi.
4 Mes petits enfants, vous êtes de Dieu, et vous les avez vaincus; parce que celui qui est en vous, est plus grand que celui qui est au monde.
Inu ana okondedwa, ndinu ochokera kwa Mulungu ndipo mwawagonjetsa aneneri onyengawa, chifukwa Iye amene ali mwa inu ndi wamkulu kuposa amene ali mʼdziko lapansi.
5 Ils sont du monde, c'est pourquoi ils parlent du monde, et le monde les écoute.
Aneneri onyengawa ndi ochokera mʼdziko lapansi, nʼchifukwa chake amayankhula za dziko lapansi, ndipo dziko lapansi limawamvera.
6 Nous sommes de Dieu; celui qui connaît Dieu, nous écoute; [mais] celui qui n'est point de Dieu, ne nous écoute point; nous connaissons à ceci l'esprit de vérité et l'esprit d'erreur.
Ife ndi ochokera kwa Mulungu, ndipo aliyense amene amadziwa Mulungu amamvera zimene timayankhula. Koma aliyense amene sachokera kwa Mulungu samvera zimene timayankhula. Mmenemu ndiye mmene timasiyanitsira pakati pa mzimu wachoonadi ndi Mzimu wachinyengo.
7 Mes bien-aimés, aimons-nous l'un l'autre; car la charité est de Dieu; et quiconque aime [son prochain] est né de Dieu, et connaît Dieu.
Anzanga okondedwa, tiyeni tikondane wina ndi mnzake, pakuti chikondi chimachokera kwa Mulungu. Aliyense amene ali ndi chikondi ndi mwana wa Mulungu ndipo amadziwa Mulungu.
8 Celui qui n'aime point [son prochain], n'a point connu Dieu; car Dieu est charité.
Aliyense amene alibe chikondi sadziwa Mulungu, chifukwa Mulungu ndiye chikondi.
9 En ceci est manifestée la charité de Dieu envers nous, que Dieu a envoyé son Fils unique au monde, afin que nous vivions par lui.
Mmene Mulungu anaonetsera chikondi chake pakati pathu ndi umu: Iye anatumiza Mwana wake mmodzi yekha ku dziko lapansi kuti mwa Iyeyo tikhale ndi moyo.
10 En ceci est la charité, non que nous ayons aimé Dieu, mais en ce qu'il nous a aimés, et qu'il a envoyé son Fils pour être la propitiation pour nos péchés.
Chikondi ndi ichi: osati kuti ife ndife amene tinamukonda Mulungu, koma kuti Iyeyo ndiye amene anatikonda ndipo anatumiza Mwana wake kuti akhale nsembe yopepesera machimo athu.
11 Mes bien-aimés, si Dieu nous a ainsi aimés, nous devons aussi nous aimer l'un l'autre.
Anzanga okondedwa, popeza Mulungu anatikonda chotere, ifenso tiyenera kukondana wina ndi mnzake.
12 Personne n'a jamais vu Dieu; si nous nous aimons l'un l'autre, Dieu demeure en nous, et sa charité est accomplie en nous.
Palibe amene anaonapo Mulungu, koma tikakondana wina ndi mnzake, ndiye kuti Mulungu amakhala mwa ife ndipo chikondi chake chafika pachimake penipeni mwa ife.
13 A ceci nous connaissons que nous demeurons en lui, et lui en nous, c'est qu'il nous a donné de son Esprit.
Ife tikudziwa kuti timakhala mwa Iye ndipo Iyeyo amakhala mwa ife chifukwa anatipatsa Mzimu wake.
14 Et nous l'avons vu, et nous témoignons que le Père a envoyé le Fils pour être le sauveur du monde.
Ndipo taona ndipo tikuchitira umboni, kuti Atate anatuma Mwana wake kuti akhale Mpulumutsi wa dziko lapansi.
15 Quiconque confessera que Jésus est le Fils de Dieu, Dieu demeure en lui, et lui en Dieu.
Ngati aliyense avomereza kuti Yesu ndi Mwana wa Mulungu, Mulungu amakhala mwa iye ndipo iyeyo amakhala mwa Mulungu.
16 Et nous avons connu et cru la charité que Dieu a pour nous. Dieu est charité; et celui qui demeure dans la charité, demeure en Dieu, et Dieu en lui.
Tikudziwa ndipo timadalira chikondi chimene Mulungu ali nacho pa ife. Mulungu ndiye chikondi. Aliyense amene amakhala moyo wachikondi, ali mwa Mulungu ndipo Mulungu amakhala mwa iye.
17 En ceci est accomplie la charité envers nous, afin que nous ayons de la confiance pour le jour du Jugement, si tel qu'il est, nous sommes tels en ce monde.
Chikondi chafika pachimake penipeni pakati pathu, kotero kuti pa tsiku lachiweruzo tidzakhala olimba mtima chifukwa mʼdziko lapansi moyo wathu uli ngati wa Khristu.
18 Il n'y a point de crainte dans la charité, mais la parfaite charité bannit la crainte; car la crainte cause de la peine; or celui qui craint, n'est pas accompli dans la charité.
Mulibe mantha mʼchikondi. Koma chikondi ndi changwiro chimachotsa mantha, chifukwa mantha amabwera chifukwa choopa chilango. Munthu amene ali ndi mantha, chikondi chake sichangwiro.
19 Nous l'aimons, parce qu'il nous a aimés le premier.
Ife timakonda Mulungu chifukwa ndiye anayamba kutikonda.
20 Si quelqu'un dit: j'aime Dieu, et cependant il hait son frère, il est un menteur; car comment celui qui n'aime point son frère, qu'il voit, peut-il aimer Dieu, lequel il ne voit point?
Ngati wina anena kuti, “Ine ndimakonda Mulungu,” koma namadana ndi mʼbale wake ndi wabodza ameneyo. Pakuti aliyense amene sakonda mʼbale wake, amene akumuona, sangathenso kukonda Mulungu amene sanamuone.
21 Et nous avons ce commandement de sa part, que celui qui aime Dieu, aime aussi son frère.
Ndipo Iye anatipatsa lamulo lakuti: Aliyense amene amakonda Mulungu ayenera kukondanso mʼbale wake.