< 1 Chroniques 28 >

1 Or David assembla à Jérusalem tous les Chefs d'Israël, les Chefs des Tribus, et les Chefs des départements qui servaient le Roi; et les Gouverneurs de milliers et de centaines, et ceux qui avaient la charge de tous les biens du Roi, et de tout ce qu il possédait, ses fils avec ses Eunuques, et les hommes puissants, et tous les hommes forts et vaillants;
Davide anayitana akuluakulu onse a Israeli kuti asonkhane ku Yerusalemu: akuluakulu a mafuko, olamulira magulu a ntchito ya mfumu, olamulira ankhondo 1,000, ndi olamulira ankhondo 100, ndiponso akuluakulu onse osunga katundu ndi ziweto za mfumu ndi ana ake, pamodzinso ndi akuluakulu a ku nyumba yaufumu, anthu amphamvu ndi asilikali onse olimba mtima.
2 Puis le Roi David se leva sur ses pieds, et dit: Mes frères, et mon peuple, écoutez-moi: J'ai désiré de bâtir une maison de repos à l'Arche de l'alliance de l'Eternel, et au marchepied de notre Dieu, et j'ai fait les préparatifs pour la bâtir.
Mfumu Davide inayimirira ndipo inati: “Tamverani abale anga ndi anthu anga. Ine ndinali ndi maganizo omanga nyumba monga malo okhalamo Bokosi la Chipangano la Yehova, malo oyikapo mapazi a Mulungu wathu, ndipo ndinakonza ndondomeko yomangira nyumbayo.”
3 Mais Dieu m'a dit: Tu ne bâtiras point de maison à mon Nom, parce que tu es un homme de guerre, et que tu as répandu beaucoup de sang.
Koma Mulungu anati kwa ine, “Usandimangire nyumba chifukwa ndiwe munthu wankhondo ndipo wakhala ukukhetsa magazi.”
4 Or comme l'Eternel le Dieu d'Israël m'a choisi de toute la maison de mon père pour être Roi sur Israël à toujours; car il a choisi Juda pour Conducteur, et de la maison de Juda la maison de mon père, et d'entre les fils de mon père il a pris son plaisir en moi, pour me faire régner sur tout Israël.
“Komabe Yehova Mulungu wa Israeli anasankha ine pakati pa onse a banja langa kukhala mfumu ya Israeli kwamuyaya. Iye anasankha Yuda kukhala mtsogoleri, ndipo pa banja la Yuda anasankha banja langa. Pakati pa ana aamuna a abambo anga, kunamukomera Iye kundikhazika mfumu ya Aisraeli onse.
5 Aussi d'entre tous mes fils ( car l'Eternel m'a donné plusieurs fils ) il a choisi Salomon mon fils, pour s'asseoir sur le trône du Royaume de l'Eternel sur Israël.
Pa ana anga ambiri onse amene Yehova wandipatsa, Iye wasankha mwana wanga Solomoni kuti akhale pa mpando waufumu wa ufumu wa Yehova kuti alamulire Israeli.”
6 Et il m'a dit: Salomon ton fils est celui qui bâtira ma maison et mes parvis; : car je me le suis choisi pour fils et je lui serai père.
Yehova anati kwa ine, “Solomoni mwana wako ndiye amene adzamanga nyumba yanga ndi mabwalo anga, pakuti Ine ndamusankha kuti akhale mwana wanga ndipo Ine ndidzakhala abambo ake.
7 Et j'affermirai son règne à toujours, s'il s'applique à faire mes commandements [et à observer] mes ordonnances, comme [il le fait] aujourd'hui.
Ine ndidzakhazikitsa ufumu wake kwamuyaya ngati iye saleka kutsatira malamulo ndi malangizo anga, monga momwe zikuchitikira leromu.”
8 Maintenant donc [je vous somme] en la présence de tout Israël, qui est l'assemblée de l'Eternel, et devant notre Dieu qui l'entend, que vous ayez à garder et à rechercher diligemment tous les commandements de l'Eternel votre Dieu, afin que vous possédiez ce bon pays, et que vous le fassiez hériter à vos enfants après vous, à jamais.
“Tsono lero ine ndikulamula inu pamaso pa Aisraeli onse ndi pa msonkhano wa Yehova, ndipo Mulungu wathu akumva: Mutsatire mosamala malamulo a Yehova Mulungu wathu, kuti dziko labwinoli likhale lanu ndi kuti mudzalipereke kwa zidzukulu zanu kukhala cholowa chawo kwamuyaya.”
9 Et toi Salomon mon fils, connais le Dieu de ton père, et sers-le avec un cœur droit, et une bonne volonté; car l'Eternel sonde tous les cœurs, et connaît toutes les imaginations des pensées. Si tu le cherches, il se fera trouver à toi; mais si tu l'abandonnes, il te rejettera pour toujours.
“Ndipo iwe mwana wanga Solomoni, umvere Mulungu wa abambo ako, umutumikire ndi mtima wodzipereka kwathunthu ndi mtima wako wonse, pakuti Yehova amasanthula mtima wa aliyense, ndipo amadziwa maganizo aliwonse a munthu. Ngati ufunafuna Yehova, Iye adzapezeka; koma ngati umutaya, Iye adzakukana kwamuyaya.
10 Considère maintenant, que l'Eternel t'a choisi pour bâtir une maison pour son sanctuaire; fortifie-toi donc, et applique-toi à y travailler.
Tsopano ganizira bwino, pakuti Yehova wakusankha iwe kuti umange Nyumba ya Mulungu monga malo ake opatulika. Khala wamphamvu ndipo ugwire ntchito.”
11 Et David donna à Salomon son fils le modèle du portique, de ses maisons, de ses cabinets, de ses chambres hautes, de ses cabinets de dedans, et du lieu du Propitiatoire.
Kotero Davide anapatsa Solomoni mwana wake mapulani a khonde la Nyumba ya Mulungu, nyumba zake, mosungiramo katundu, zipinda zake zamʼmwamba, zipinda zamʼkati ndi malo a nsembe zopepesera machimo.
12 Et le modèle de toutes les choses qui lui avaient été inspirées par l'Esprit qui était avec lui, pour les parvis de la maison de l'Eternel, pour les chambres d'alentour, pour les trésors de la maison de l'Eternel, et pour les trésors des choses saintes;
Iye anapatsa Solomoni mapulani a zonse zimene ankaziganizira za bwalo la Nyumba ya Yehova ndi zipinda zonse zozungulira, zipinda zosungiramo chuma cha Nyumba ya Mulungu ndi zinthu zoperekedwa kwa Yehova.
13 Et pour les départements des Sacrificateurs et des Lévites, et pour toute l'œuvre du service de la maison de l'Eternel, et pour tous les ustensiles du service de la maison de l'Eternel.
Davide anamulangiza za magulu a ansembe ndi Alevi ndi ntchito yonse yotumikira mʼNyumba ya Yehova, komanso za zinthu zonse zogwirira ntchito potumikira.
14 [Il lui donna aussi] de l'or à certain poids, pour les choses qui devaient être d'or, [savoir] pour tous les ustensiles de chaque service; [et de l'argent] à certain poids, pour tous les ustensiles d'argent, [savoir] pour tous les ustensiles de chaque service.
Iye anakonzeratu za kulemera kwa golide wopangira zida zonse zagolide zogwirira ntchito zosiyanasiyana, ndiponso kulemera kwa siliva wopangira zida zonse zasiliva zogwirira ntchito zosiyanasiyana:
15 Le poids des chandeliers d'or, et de leurs lampes d'or, selon le poids de chaque chandelier et de ses lampes; et [le poids] des chandeliers d'argent, selon le poids de chaque chandelier et de ses lampes, selon le service de chaque chandelier.
kulemera kwa golide wopangira choyikapo nyale chagolide ndi nyale zake; ndiponso kulemera kwa siliva wa choyikapo nyale chilichonse ndi nyale zake, molingana ndi kagwiritsidwe ka choyikapo nyale chilichonse;
16 Et le poids de l'or pesant ce qu'il fallait pour chaque table des pains de proposition; et de l'argent pour les tables d'argent.
kulemera kwa golide wa tebulo iliyonse yoyikapo buledi wopatulika; kulemera kwa siliva wopangira matebulo asiliva;
17 Et de l'or pur pour les fourchettes, pour les bassins, pour les gobelets, et pour les plats d'or, selon le poids de chaque plat; et [de l'argent] pour les plats d'argent, selon le poids de chaque plat.
muyeso wa golide woyengeka bwino wopangira mafoloko, mbale ndi zotungira; muyeso wa golide wa beseni lililonse la siliva;
18 Et de l'or affiné à certain poids pour l'autel des parfums; et de l'or pour le modèle du chariot des Chérubins qui étendaient [les ailes], et qui couvraient l'Arche de l'alliance de l'Eternel.
ndiponso muyeso wa golide wabwino wopangira guwa la zofukiza. Davide anamupatsanso ndondomeko ya mapangidwe a galeta, akerubi agolide atatambasula mapiko awo kuphimba Bokosi la Chipangano la Yehova.
19 Toutes ces choses, [dit-il], m'ont été données par écrit, de la part de l'Eternel, afin que j'eusse l'intelligence de tous les ouvrages de ce modèle.
Davide anati, “Zonsezi ndalemba kuchokera kwa Yehova, ndipo Iye wachita kuti ndimvetsetse zonse za mapulaniwa.”
20 C'est pourquoi David dit à Salomon son fils: Fortifie-toi, et prends courage, et travaille; ne crains point, et ne t'effraie de rien; car l'Eternel Dieu, mon Dieu, [sera] avec toi, il ne te délaissera point, et il ne t'abandonnera point, que tu n'aies achevé tout l'ouvrage du service de la maison de l'Eternel.
Davide anatinso kwa mwana wake Solomoni, “Khala wamphamvu ndi wolimba mtima ndipo uchite ntchitoyi. Usachite mantha kapena kutaya mtima pakuti Yehova Mulungu wanga ali nawe. Iye sadzakukhumudwitsa kapena kukusiya mpaka ntchito yonse ya Nyumba ya Mulungu itatha.
21 Et voici, [j'ai fait] les départements des Sacrificateurs et des Lévites pour tout le service de la maison de Dieu; et il y a avec toi pour tout cet ouvrage toutes sortes de gens prompts et experts, pour toute sorte de service; et les Chefs avec tout le peuple [seront prêts] pour exécuter tout ce que tu diras.
Magulu a ansembe ndi Alevi ndi okonzeka kugwira ntchito ya Nyumba ya Mulungu, ndipo munthu waluso aliyense wodzipereka adzakuthandiza pa ntchito yonse. Akuluakulu ndi anthu onse adzamvera chilichonse chomwe udzalamula.”

< 1 Chroniques 28 >