< 1 Chroniques 16 >
1 Ils amenèrent donc l'Arche de Dieu, et la posèrent dans le tabernacle que David lui avait tendu; et on offrit devant Dieu des holocaustes et des sacrifices de prospérités.
Iwo anabwera nalo Bokosi la Mulungu ndipo analiyika pamalo pake mʼkati mwa tenti imene Davide anayimika ndipo iwo anapereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano pamaso pa Mulungu.
2 Et quand David eut achevé d'offrir les holocaustes et les sacrifices de prospérités, il bénit le peuple au Nom de l'Eternel.
Davide atatsiriza kupereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano, iye anadalitsa anthu mʼdzina la Yehova.
3 Et il distribua à chacun, tant aux hommes qu'aux femmes, un pain, et une pièce de chair, et une bouteille de vin.
Kenaka anagawira Mwisraeli aliyense, wamwamuna ndi wamkazi, aliyense buledi mmodzi, nthuli yanyama ndiponso keke yamphesa zowuma.
4 Et il établit quelques-uns des Lévites devant l'Arche de l'Eternel, pour y faire le service, pour célébrer, remercier, et louer le Dieu d'Israël.
Iye anasankha Alevi ena kuti azitumikira pamene panali Bokosi la Yehova, kuti azipemphera, azithokoza ndi kulemekeza Yehova Mulungu wa Israeli.
5 Asaph était le premier, et Zacharie le second, Jéhiël, Sémiramoth, Jéhiël, Mattitia, Eliab, Bénéja, Hobed-Edom, et Jéchiël, qui avaient des instruments de musique, [savoir] des musettes et des violons; et Asaph faisait retentir [sa voix] avec des cymbales.
Mtsogoleri wawo anali Asafu, wachiwiri anali Zekariya, kenaka Yeiyeli, Semiramoti, Yehieli, Matitiya, Eliabu, Benaya, Obedi-Edomu ndi Yeiyeli. Iwo amayimba azeze ndi apangwe, Asafu amayimba ziwaya za malipenga,
6 Et Bénéja et Jahaziël Sacrificateurs étaient continuellement avec des trompettes devant l'Arche de l'alliance de Dieu.
ndipo ansembe Benaya ndi Yahazieli amawomba malipenga nthawi zonse pamaso pa Bokosi la Chipangano la Mulungu.
7 Et en ce même jour David remit entre les mains d'Asaph et de ses frères, les [Psaumes suivants], pour commencer à célébrer l'Eternel.
Tsiku limeneli Davide anayamba nʼkusankha Asafu ndi anzake kuti ndiwo apereke nyimbo iyi ya matamando kwa Yehova:
8 CELEBREZ l'Eternel, invoquez son Nom, faites connaître parmi les peuples ses exploits.
Yamikani Yehova, itanani dzina lake; lalikani za ntchito zake pakati pa mitundu ya anthu.
9 Chantez lui, psalmodiez lui, parlez de toutes ses merveilles.
Imbirani Iye, muyimbireni nyimbo zamatamando; nenani za ntchito zake zonse zodabwitsa.
10 Glorifiez-vous du Nom de sa sainteté; que le cœur de ceux qui cherchent l'Eternel se réjouisse.
Nyadirani dzina lake loyera; ikondwere mitima ya iwo akufunafuna Yehova.
11 Recherchez l'Eternel et sa force, cherchez continuellement sa face.
Dalirani Yehova ndi mphamvu zake; funafunani nkhope yake nthawi zonse.
12 Souvenez-vous des merveilles qu'il a faites; de ses miracles, et des jugements de sa bouche.
Kumbukirani ntchito zodabwitsa wazichita, zozizwitsa zake, ndi kuweruza kwa mʼkamwa mwake,
13 La postérité d'Israël sont ses serviteurs; les enfants de Jacob sont ses
inu zidzukulu za Israeli mtumiki wake, inu ana a Yakobo, osankhidwa ake.
14 Il est l'Eternel notre Dieu; ses jugements sont par toute la terre.
Iye ndiye Yehova Mulungu wathu; chiweruzo chake chili pa dziko lonse lapansi.
15 Souvenez-vous toujours de son alliance, de la parole qu'il a prescrite en mille générations;
Iye amakumbukira pangano lake nthawi zonse, mawu amene Iye analamula, kwa mibado miyandamiyanda,
16 Du traité qu'il a fait avec Abraham; et de son serment fait à Isaac;
pangano limene anachita ndi Abrahamu, lonjezo limene analumbira kwa Isake.
17 Lequel il a confirmé à Jacob [et] à Israël, pour être une ordonnance et une alliance éternelle.
Iye analitsimikiza kwa Yakobo monga lamulo, kwa Israeli monga pangano lamuyaya.
18 En disant: Je te donnerai le pays de Canaan, pour le lot de ton héritage;
“Kwa iwe, ine ndidzapereka dziko la Kanaani monga cholowa chimene udzachilandira.”
19 Encore que vous soyez un petit nombre de gens, et même que vous y séjourniez depuis peu de temps, comme étrangers.
Ali anthu owerengeka, ochepa ndithu, komanso alendo mʼdzikomo,
20 Car ils étaient errants de nation en nation, et d'un Royaume vers un autre peuple.
iwo anayendayenda kuchoka ku mtundu wina kupita ku mtundu wina, ku ufumu wina kupita ku ufumu wina.
21 Il n'a pas souffert qu'aucun les outrageât; même il a châtié les Rois pour l'amour d'eux.
Iye sanalole munthu aliyense kuti awapondereze; chifukwa cha iwo, Iye anadzudzula mafumu:
22 [Et il a dit]: Ne touchez point à mes Oints, et ne faites point de mal à mes Prophètes.
“Musakhudze odzozedwa anga; musawachitire choyipa aneneri anga.”
23 TOUTE la terre, chantez à l'Eternel, prêchez chaque jour sa délivrance;
Imbirani Yehova, dziko lonse lapansi; lalikani za chipulumutso chake tsiku ndi tsiku.
24 Racontez sa gloire parmi les nations, [et] ses merveilles parmi tous les peuples.
Lengezani za ulemerero wake kwa mitundu yonse, ntchito zake zonse zodabwitsa kwa anthu onse.
25 Car l'Eternel est grand, et très-digne de louange, il est plus redoutable que tous les dieux.
Pakuti Yehova ndi wamkulu ndi woyenera kwambiri kumutamanda; Iyeyo ayenera kuopedwa kuposa milungu yonse.
26 Et en effet tous les dieux des peuples sont des idoles; mais l'Eternel a fait les cieux.
Pakuti milungu yonse ya anthu a mitundu ina ndi mafano wopanda pake, koma Yehova analenga kumwamba.
27 La Majesté et la magnificence [marchent] devant lui; la force et la joie sont dans le lieu où il habite.
Ulemerero ndi ufumu zili pamaso pake; mphamvu ndi chimwemwe zili pa malo pokhala Iye.
28 Familles des peuples, attribuez à l'Eternel, attribuez à l'Eternel gloire et force.
Perekani kwa Yehova, Inu mabanja a anthu a mitundu ina, perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu,
29 Attribuez à l'Eternel la gloire due à son Nom; apportez l'oblation, et présentez-vous devant lui; prosternez-vous devant l'Eternel avec une sainte magnificence.
perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake. Bweretsani chopereka ndipo mufike pamaso pake; pembedzani Yehova mu ulemerero wachiyero chake.
30 Vous tous les habitants de la terre tremblez, tout étonnés pour la présence de sa face; car la terre habitable est affermie [par lui], sans qu'elle soit ébranlée.
Njenjemerani pamaso pake, dziko lonse lapansi! Dziko linakhazikika kolimba; silingasunthidwe.
31 Que les cieux se réjouissent, que la terre s'égaye, et qu'on dise parmi les nations: L'Eternel règne.
Zakumwamba zisangalale, dziko lapansi likondwere; anene anthu a mitundu ina, “Yehova ndi mfumu!”
32 Que la mer et tout ce qu'elle contient bruie; que les champs et tout ce qui est en eux se réjouissent.
Nyanja ikokome, ndi zonse zili mʼmenemo; minda ikondwere, ndi zonse zili mʼmenemo!
33 Alors les arbres de la forêt crieront de joie au devant de l'Eternel, parce qu'il vient juger la terre.
Ndipo mitengo ya mʼnkhalango idzayimba, idzayimba chifukwa cha chimwemwe pamaso pa Yehova, pakuti akubwera kudzaweruza dziko lapansi.
34 Célébrez l'Eternel, car il est bon; parce que sa gratuité demeure à jamais.
Yamikani Yehova, pakuti Iye ndi wabwino; chikondi chake chikhala mpaka muyaya.
35 Et dites: Ô Dieu! de notre salut, sauve-nous, et nous rassemble, et nous retire d'entre les nations, pour célébrer ton saint Nom, [et] pour nous glorifier en ta louange.
Fuwulani kuti, “Tipulumutseni, Inu Mulungu wa chipulumutso chathu, mutisonkhanitse ndipo mutipulumutse kwa anthu a mitundu ina, kuti tiyamike dzina lanu loyera, kuti tikutamandeni.”
36 Béni soit l'Eternel le Dieu d'Israël, depuis un siècle jusqu'à l'autre! Et tout le peuple dit: Amen; et on loua l'Eternel.
Atamandike Yehova Mulungu wa Israeli, kuyambira muyaya mpaka muyaya. Ndipo anthu onse anati, “Ameni” ndipo “Tikutamandani Yehova.”
37 On laissa donc là devant l'Arche de l'alliance de l'Eternel, Asaph et ses frères, pour faire le service continuellement, selon ce qu'il y avait à faire chaque jour devant l'Arche.
Ndipo Davide anasiya Asafu pamodzi ndi anzake kumene kunali Bokosi la Chipangano la Yehova kuti azitumikira kumeneko nthawi zonse, monga mwa zoyenera kuchita pa tsiku lililonse.
38 Et Hobed-Edom, et ses frères, au nombre de soixante-huit, Hobed-Edom, dis-je, fils de Jéduthun, et Hosa pour portiers.
Iye anasiyanso Obedi-Edomu pamodzi ndi anzake 68 kuti azitumikira nawo pamodzi. Obedi-Edomu mwana wa Yedutuni ndi Hosa anali alonda a pa chipata.
39 Et [on laissa] Tsadoc le Sacrificateur, et ses frères Sacrificateurs, devant le pavillon de l'Eternel, dans le haut lieu qui était à Gabaon,
Davide anasiya wansembe Zadoki ndi ansembe anzake ku chihema cha Yehova ku malo achipembedzo ku Gibiyoni
40 Pour offrir des holocaustes à l'Eternel continuellement sur l'autel de l'holocauste, le matin, et le soir, et pour faire toutes les choses qui sont écrites dans la Loi de l'Eternel, lesquelles il avait commandées à Israël;
kuti azipereka nsembe zopsereza kwa Yehova pa guwa lansembe nthawi zonse mmawa ndi madzulo, potsata zonse zimene zinalembedwa mʼbuku la malamulo a Yehova, amene anawapereka kwa Aisraeli.
41 Et avec eux Héman et Jéduthun, et les autres qui furent choisis et marqués par leur nom, pour célébrer l'Eternel, parce que sa gratuité demeure éternellement.
Anthuwo anali pamodzi ndi Hemani ndi Yedutuni ndi onse amene anawasankha mowatchula dzina kuti apereke mayamiko kwa Yehova, “pakuti chikondi chake ndi chosatha.”
42 Et Héman et Jéduthun étaient avec ceux-là; il y avait aussi des trompettes, et des cymbales pour ceux qui faisaient retentir [leur voix], et des instruments pour chanter les cantiques de Dieu; et les fils de Jéduthun étaient portiers.
Hemani ndi Yedutuni anali oyangʼanira malipenga ndi ziwaya ndiponso zipangizo zina zoyimbira nyimbo zachipembedzo. Ana a Yedutuni anawayika kuti aziyangʼanira pa chipata.
43 Puis tout le peuple s'en alla chacun en sa maison, et David aussi s'en retourna pour bénir sa maison.
Kenaka anthu onse anachoka, aliyense kupita kwawo. Ndipo Davide anabwerera ku nyumba kwake kukadalitsa banja lake.