< 1 Chroniques 12 >

1 Or ce sont ici ceux qui allèrent trouver David à Tsiklag, lorsqu'il y était encore enfermé à cause de Saül fils de Kis, et qui étaient des plus vaillants, pour donner du secours dans la guerre,
Nawa anthu amene anabwera kwa Davide ali ku Zikilagi pamene iye anathamangitsidwa ndi Sauli mwana wa Kisi (iwowo anali mʼgulu la asilikali amene ankamuthandiza pa nkhondo.
2 Equipés d'arcs, se servant de la main droite et de la gauche à jeter des pierres, et à tirer des flèches avec l'arc. D'entre les parents de Saül, qui étaient de Benjamin,
Iwo anali ndi mauta ndipo amadziwa kuponya mivi komanso miyala, ndipo amatha kuponyera dzanja lamanja kapena lamanzere. Iwo anali abale ake a Sauli ochokera ku fuko la Benjamini.
3 Ahihézer le Chef, et Joas, enfants de Sémaha, qui était de Guibha, et Jéziël, et Pelet enfants de Hazmaveth, et Beraca, et Jéhu Hanathothite,
Mtsogoleri wawo anali Ahiyezeri ndi Yowasi ana a Semaya wa ku Gibeya; Yezieli ndi Peleti ana a Azimaveti; Beraka, Yehu wa ku Anatoti,
4 Et Jismahja Gabaonite, vaillant entre les trente, et même plus que les trente, et Jérémie, Jahaziël, Johanan, et Jozabad Guédérothite,
ndi Isimaiya wa ku Gibiyoni, munthu wamphamvu mʼgulu la anthu makumi atatu aja, yemwenso anali mtsogoleri wawo; Yeremiya, Yahazieli, Yohanani, Yozabadi wa ku Gederi,
5 Elhuzaï, Jérimoth, Béhalia, Sémaria, et Séphatia Haruphien,
Eluzai, Yerimoti, Bealiya, Semariya ndi Sefatiya Mharufi;
6 Elkana, Jisija, Hazaréël, Johézer et Jasobham Corites,
Elikana, Isiya, Azareli, Yowezeri ndi Yasobeamu a ku banja la Kora;
7 Et Johéla et Zébadia, enfants de Jéroham de Guédor.
ndi Yowela ndi Zebadiya ana a Yerohamu wa ku Gedori.
8 Quelques-uns aussi des Gadites se retirèrent vers David, dans la forteresse au désert, hommes forts et vaillants, experts à la guerre, [et] maniant le bouclier et la lance. Leurs visages étaient [comme] des faces de lion, et ils semblaient des daims sur les montagnes, tant ils couraient légèrement.
Asilikali ena a fuko la Gadi anathawira kwa Davide ku linga lake ku chipululu. Iwo anali asilikali olimba mtima, okonzekera nkhondo ndipo amadziwa kugwiritsa ntchito chishango ndi mkondo. Iwowo anali woopsa ngati mikango ndipo anali aliwiro ngati ngoma zamʼmapiri.
9 Hézer le premier, Hobadia le second, Eliab le troisième,
Mtsogoleri wawo anali Ezeri, wotsatana naye anali Obadiya, wachitatu anali Eliabu,
10 Mismanna le quatrième, Jérémie le cinquième,
wachinayi anali Misimana, Yeremiya anali wachisanu,
11 Hattaï le sixième; Eliël le septième,
wachisanu ndi chimodzi anali Atai, Elieli anali wachisanu ndi chiwiri,
12 Johanan le huitième, Elzabad le neuvième,
wachisanu ndi chitatu anali Yohanani, Elizabadi anali wachisanu ndi chinayi,
13 Jérémie le dixième, Macbannaï le onzième.
wakhumi anali Yeremiya ndipo Makibanai anali wa 11.
14 Ceux-là d'entre les enfants de Gad furent Capitaines de l'armée; le moindre avait la charge de cent hommes, et le plus distingué, de mille.
Anthu a fuko la Gadi amenewa anali atsogoleri; angʼonoangʼono amalamulira anthu 100 pamene akuluakulu amalamulira anthu 1,000.
15 Ce sont ceux qui passèrent le Jourdain au premier mois, au temps qu'il a accoutumé de se déborder sur tous ses rivages; et ils chassèrent ceux qui demeuraient dans les vallées, vers l'Orient et l'Occident.
Awa ndi amene anawoloka Yorodani mwezi woyamba pamene mtsinje unali utasefukira mbali zonse, ndipo anathamangitsa aliyense amene amakhala mʼchigwa, mbali ya kumadzulo ndi kummawa.
16 Il vint aussi des enfants de Benjamin et de Juda vers David à la forteresse.
Anthu ena a fuko la Benjamini ndi ena ochokera ku Yuda anabweranso kwa Davide pamene anali ku linga lake.
17 Et David sortit au devant d'eux et prenant la parole, il leur dit: Si vous êtes venus en paix vers moi pour m'aider, mon cœur vous sera uni; mais si c'est pour me trahir, [et me livrer] à mes ennemis, quoique je ne sois coupable d'aucune violence, que le Dieu de nos pères le voie, et qu'il en fasse la punition.
Davide anapita kukakumana nawo ndipo anati, “Ngati mwabwera kwa ine mwamtendere, kuti mundithandize, ndakonzeka kugwirizana nanu. Koma ngati mwabwera kudzandipereka kwa adani anga, ngakhale kuti sindinalakwe, Mulungu wa makolo anthu aone izi ndipo akuweruzeni.”
18 Et l'esprit revêtit Hamasaï un des principaux Capitaines, [qui dit]: Que la paix soit avec toi, ô David! qu'elle soit avec toi, fils d'Isaï! que la paix soit à ceux qui t'aident, puisque ton Dieu t'aide! Et David les reçut, et les établit entre les Capitaines de ses troupes.
Kenaka Mzimu anabwera pa Amasai, mtsogoleri wa anthu makumi atatu aja ndipo anati: “Inu Davide, ife ndife anu! Tili nanu limodzi, inu mwana wa Yese! Kupambana, Kupambana kwa inu, ndiponso kupambana kukhale kwa iwo amene akukuthandizani pakuti Mulungu wanu adzakuthandizani.” Kotero Davide anawalandira ndipo anawayika kukhala atsogoleri a magulu ake a ankhondo.
19 Il y en eut aussi de ceux de Manassé qui s'allèrent rendre à David, quand il vint avec les Philistins pour combattre contre Saül; mais ils ne leur donnèrent point de secours, parce que les Gouverneurs des Philistins, après en avoir délibéré entr'eux, le renvoyèrent, en disant: Il se tournera vers son Seigneur Saül, au péril de nos têtes.
Anthu ena a fuko la Manase anathawira kwa Davide pamene anapita ndi Afilisti kukamenyana ndi Sauli. (Iye ndi anthu ake sanathandize Afilisti chifukwa, atsogoleri awo atakambirana, anamubweza Davide. Iwo anati, “Ife tidzawonongedwa ngati uyu adzabwerera kwa mbuye wake Sauli).”
20 Quand donc il retournait à Tsiklag, Hadna, Jozabad, Jédihaël, Micaël, Jozabad, Elihu, et Tsillethaï, Chefs des milliers qui étaient en Manassé, se tournèrent vers lui.
Davide atapita ku Zikilagi, anthu a fuko la Manase amene anathawira kwa iye anali awa: Adina, Yozabadi, Yediaeli, Mikayeli, Yozabadi, Elihu ndi Ziletai; atsogoleri a magulu a anthu 1,000 a ku Manase.
21 Et ils aidèrent David contre la troupe des Hamalécites, car ils étaient tous forts et vaillants, et ils furent faits Capitaines dans l'armée.
Iwowa anathandiza Davide kulimbana ndi magulu achifwamba, pakuti onsewa anali asilikali olimba mtima ndipo anali atsogoleri mʼgulu lake la ankhondo.
22 Et même à toute heure il venait des gens vers David pour l'aider, de sorte qu'il eut une grande armée, comme une armée de Dieu.
Tsiku ndi tsiku anthu amabwera kudzathandiza Davide, mpaka anakhala ndi gulu lalikulu la ankhondo, ngati gulu la ankhondo a Mulungu.
23 Or ce sont ici les dénombrements des hommes équipés pour la guerre, qui vinrent vers David à Hébron, afin de faire tomber sur lui le Royaume de Saül, suivant le commandement de l'Eternel.
Nachi chiwerengero cha magulu a anthu ankhondo amene anabwera kwa Davide ku Hebroni kudzapereka ufumu wa Sauli kwa iye, monga momwe ananenera Yehova:
24 Des enfants de Juda, qui portaient le bouclier et la javeline, six mille huit cents, équipés pour la guerre.
Anthu a fuko la Yuda onyamula chishango ndi mkondo analipo 6,800;
25 Des enfants de Siméon, forts et vaillants pour la guerre, sept mille et cent.
Anthu a fuko la Simeoni, asilikali okonzekera nkhondo analipo 7,100;
26 Des enfants de Lévi, quatre mille six cents.
Anthu a fuko la Levi analipo 4,600,
27 Et Jéhojadah, conducteur de ceux d'Aaron et avec lui trois mille sept cents.
mtsogoleri Yehoyada wa banja la Aaroni anabweranso ndi anthu 3,700,
28 Et Tsadoc, jeune homme fort et vaillant, et vingt et deux des principaux de la maison de son père.
ndi Zadoki, mnyamata wankhondo wolimba mtima, anabwera ndi akuluakulu 22 ochokera mʼbanja lake;
29 Des enfants de Benjamin, parents de Saül, trois mille; car jusqu'alors la plus grande partie d'entr'eux avait tâché de soutenir la maison de Saül.
Anthu a fuko la Benjamini, abale ake a Sauli analipo 3,000 ndipo ambiri anali ndi Sauli ku nyumba yake pa nthawiyi;
30 Des enfants d'Ephraïm vingt mille huit cents, forts et vaillants, [et] hommes de réputation dans la maison de leurs pères.
Anthu a fuko la Efereimu, asilikali olimba mtima, otchuka pa mabanja awo analipo 20,800;
31 De la demi-Tribu de Manassé dix-huit mille, qui furent nommés par leur nom pour aller établir David Roi.
Anthu a fuko latheka la Manase amene anawayitana kuti adzakhazikitse nawo ufumu wa Davide analipo 18,000;
32 Des enfants d'Issacar, fort intelligents dans la connaissance des temps, pour savoir ce que devait faire Israël, deux cents de leurs Chefs, et tous leurs frères se conduisaient par leur avis.
Anthu a fuko la Isakara amene ankazindikira nthawi ndipo amadziwa zimene Israeli ankayenera kuchita, analipo atsogoleri 200 pamodzi ndi abale awo onse amene amawatsogolera.
33 De Zabulon, cinquante mille combattants, rangés en bataille avec toutes sortes d'armes, et gardant leur rang d'un cœur assuré.
Anthu a fuko la Zebuloni, analipo 5,000. Iwowa anali asilikali odziwa bwino nkhondo, okhala ndi zida za mtundu uliwonse, okonzekera kudzathandiza Davide ndi mtima umodzi.
34 De Nephthali, mille capitaines, et avec eux trente-sept mille, portant le bouclier et la hallebarde.
Anthu a fuko la Nafutali, analipo atsogoleri 1,000 pamodzi ndi anthu 37,000 onyamula zishango ndi mikondo;
35 Des Danites, vingt-huit mille six cents, rangés en bataille.
Anthu a fuko la Dani, okonzekera nkhondo analipo 28,600.
36 D'Aser, quarante mille combattants, et gardant leur rang en bataille.
Anthu a fuko la Aseri, asilikali odziwa bwino nkhondo, okonzekeradi nkhondo analipo 40,000;
37 De ceux de delà le Jourdain, [savoir] des Rubénites, des Gadites, et de la demi-Tribu de Manassé, six-vingt mille, avec tous les instruments de guerre pour combattre.
Ndipo kuchokera kummawa kwa Yorodani, anthu a fuko la Rubeni, Gadi ndi theka la fuko la Manase, amene anali ndi zida za mtundu uliwonse analipo 120,000.
38 Tous ceux-ci, gens de guerre, rangés en bataille, vinrent tous de bon cœur à Hébron, pour établir David Roi sur tout Israël; et tout le reste d'Israël était aussi d'un même sentiment pour établir David Roi.
Onsewa anali anthu odziwa kumenya nkhondo amene anadzipereka ku magulu awo. Iwo anabwera ku Hebroni ali otsimikiza kudzamuyika Davide kukhala mfumu ya Aisraeli. Aisraeli ena onse anali ndi mtima umodzinso womuyika Davide kukhala mfumu.
39 Et ils furent là avec David, mangeant et buvant pendant trois jours; car leurs frères leur avaient préparé des vivres.
Anthuwa anakhala ndi Davide masiku atatu akudya ndi kumwa pakuti mabanja awo anawapatsa zakudya.
40 Et même ceux qui étaient les plus proches d'eux jusqu'à Issacar, et Zabulon, et Nephthali, apportaient du pain sur des ânes et sur des chameaux, sur des mulets, et sur des bœufs, de la farine, des figues sèches, des raisins secs, du vin, [et] de l'huile, [et ils amenaient] des bœufs, et des brebis en abondance; car il y avait joie en Israël.
Komanso anthu oyandikana nawo ochokera ku Isakara, Zebuloni ndi Nafutali anabweretsa zakudya pa abulu, ngamira, nyulu ndi ngʼombe. Panali ufa wambiri, makeke ankhuyu, ntchintchi za mphesa, vinyo, mafuta, ngʼombe, nkhosa ndi mbuzi, popeza munali chimwemwe mu Israeli.

< 1 Chroniques 12 >