< 1 Chroniques 10 >
1 Or les Philistins combattirent contre Israël, et ceux d'Israël s'enfuirent devant les Philistins, et tombèrent blessés à mort en la montagne de Guilboah.
Tsono Afilisti anachitanso nkhondo ndi Aisraeli ndipo Aisraeli anathawa Afilistiwo, kotero kuti ambiri anaphedwa pa phiri la Gilibowa.
2 Et les Philistins poursuivirent et atteignirent Saül et ses fils, et tuèrent Jonathan, Abinadab et Malki-suah, les fils de Saül.
Afilisti anapanikiza kwambiri Sauli ndi ana ake, ndipo anapha Yonatani, Abinadabu ndi Maliki-Suwa.
3 Et le combat se renforça contre Saül, de sorte que ceux qui tiraient de l'arc le trouvèrent, et il eut peur de ces archers.
Nkhondo inakula kwambiri mozungulira Sauli ndipo pamene anthu amauta anamupeza, anamuvulaza.
4 Alors Saül dit à celui qui portait ses armes: Tire ton épée, et m'en transperce, de peur que ces incirconcis ne viennent, et ne fassent de moi selon leur volonté; mais celui qui portait ses armes ne le voulut point faire; parce qu'il craignait beaucoup. Saül donc prit [son] épée, et se jeta dessus.
Tsono Sauli anawuza mnyamata wake wonyamula zida zake kuti, “Solola lupanga lako undiphe, kuopa kuti anthu osachita mdulidwewa angabwere ndi kudzandizunza ine.” Koma mnyamata wonyamula zida uja anachita mantha kwambiri ndipo sanathe kutero. Choncho Sauli anatenga lupanga lake lomwe nagwerapo.
5 Alors celui qui portait les armes de Saül, ayant vu que Saül était mort, se jeta aussi sur son épée, et mourut.
Mnyamata wonyamula zida zake uja ataona kuti Sauli wafa, nayenso anadzigwetsera pa lupanga lake nafa.
6 Ainsi mourut Saül, et ses trois fils; et tous ses gens moururent avec lui.
Motero Sauli ndi ana ake atatu anafa, pamodzi ndi banja lake lonse anafera limodzi.
7 Et tous ceux d'Israël, qui étaient dans la vallée, ayant vu qu'ils s'en étaient fuis, et que Saül et ses fils étaient morts, abandonnèrent leurs villes, et s'enfuirent, de sorte que les Philistins y entrèrent, et y habitèrent.
Pamene Aisraeli onse amene anali mʼchigwa anaona kuti gulu lankhondo lathawa komanso kuti Sauli ndi ana ake aphedwa, nawonso anathawa kusiya mizinda yawo. Ndipo Afilisti anabwera kudzakhalamo.
8 Or il arriva que dès le lendemain les Philistins vinrent pour dépouiller les morts, et ils trouvèrent Saül et ses fils étendus en la montagne de Guilboah.
Mmawa mwake, Afilisti atabwera kudzatenga zinthu za anthu ophedwa, anapeza Sauli ndi ana ake atafa pa phiri la Gilibowa.
9 Et l'ayant dépouillé, ils lui ôtèrent la tête, et ses armes, et les envoyèrent au pays des Philistins tout à l'environ, pour en faire savoir les nouvelles à leurs dieux, et au peuple.
Iwo anamuvula zovala zake, natenga mutu wake ndi zida zake zankhondo. Ndipo anatumiza amithenga mʼdziko lonse la Afilisti kukafalitsa nkhani yabwinoyi kwa mafano awo ndi kwa anthu awo.
10 Ils mirent ses armes au temple de leur dieu, et ils attachèrent sa tête en la maison de Dagon.
Iwo anayika zida zake zankhondo mʼnyumba zopembedzera milungu yawo ndipo anapachika mutu wake mʼnyumba ya Dagoni.
11 Or tous ceux de Jabés de Galaad ayant appris tout ce que les Philistins avaient fait à Saül,
Pamene anthu onse okhala ku Yabesi Giliyadi anamva zimene Afilisti anachitira Sauli,
12 Tous les vaillants hommes [d'entr'eux] se levèrent, et enlevèrent le corps de Saül, et les corps de ses fils, et les apportèrent à Jabés, et ils ensevelirent leurs os sous un chêne à Jabés, et jeûnèrent pendant sept jours.
anthu awo onse olimba mtima anapita kukatenga mitembo ya Sauli ndi ana ake ndipo anabwera nayo ku Yabesi. Anakwirira mafupa awo pansi pa mtengo wabwemba ku Yabesi, ndipo anasala kudya masiku asanu ndi awiri.
13 Saül donc mourut pour le crime qu'il avait commis contre l'Eternel, en ce qu'il n'avait point gardé la parole de l'Eternel, et qu'il avait même consulté l'esprit de Python pour [savoir ce qui lui devait arriver].
Sauli anafa chifukwa anali wosakhulupirika pamaso pa Yehova. Iye sanasunge mawu a Yehova, pakuti anakafunsira nzeru kwa woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa,
14 Il ne s'était point adressé à l'Eternel; c'est pourquoi [l'Eternel] le fit mourir, et transporta le Royaume à David fils d'Isaï.
sanafunsire nzeruzo kwa Yehova. Choncho Yehova anamupha ndi kupereka ufumu kwa Davide mwana wa Yese.