< Psaumes 75 >
1 Au chef des chantres. “Ne détruis pas.” Psaume d’Asaph. Cantique. Nous te louons, ô Dieu! Nous te louons; Ton nom est dans nos bouches; Nous publions tes merveilles.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe, potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Salimo la Asafu. Nyimbo. Tikuthokoza Inu Mulungu, tikuthokoza, pakuti dzina lanu lili pafupi nafe, anthutu amafotokoza za ntchito zanu zodabwitsa.
2 Au temps que j’aurai fixé, Je jugerai avec droiture.
Mumati, “Ine ndimayika nthawi yoyenera, ndine amene ndimaweruza mwachilungamo.
3 La terre tremble avec tous ceux qui l’habitent: Moi, j’affermis ses colonnes. (Pause)
Pamene dziko lapansi ndi anthu ake onse anjenjemera, ndine amene ndimagwiriziza mizati yake molimba. (Sela)
4 Je dis à ceux qui se glorifient: Ne vous glorifiez pas! Et aux méchants: N’élevez pas la tête!
Kwa odzitama ndikuti, ‘Musadzitamenso,’ ndipo kwa oyipa, ‘Musatukulenso nyanga zanu.
5 N’élevez pas si haut votre tête, Ne parlez pas avec tant d’arrogance!
Musatukule nyanga zanu motsutsana ndi kumwamba; musayankhule ndi khosi losololoka.’”
6 Car ce n’est ni de l’orient, ni de l’occident, Ni du désert, que vient l’élévation.
Kugamula milandu sikuchokera kummawa kapena kumadzulo kapena ku chipululu.
7 Mais Dieu est celui qui juge: Il abaisse l’un, et il élève l’autre.
Koma ndi Mulungu amene amaweruza: Iyeyo amatsitsa wina, nakwezanso wina.
8 Il y a dans la main de l’Éternel une coupe, Où fermente un vin plein de mélange, Et il en verse: Tous les méchants de la terre sucent, boivent jusqu’à la lie.
Mʼdzanja la Yehova muli chikho chodzaza ndi vinyo wochita thovu, wosakanizidwa ndi zokometsera; Iye amamutsanulira pansi ndipo onse oyipa a dziko lapansi amamwa ndi senga zake zonse.
9 Je publierai ces choses à jamais; Je chanterai en l’honneur du Dieu de Jacob.
Kunena za ine, ndidzalengeza izi kwamuyaya; ndidzayimba matamando kwa Mulungu wa Yakobo.
10 Et j’abattrai toutes les forces des méchants; Les forces du juste seront élevées.
Ndidzadula nyanga za onse oyipa koma nyanga za olungama zidzakwezedwa.