< Psaumes 24 >
1 Psaume de David. A l’Éternel la terre et ce qu’elle renferme, Le monde et ceux qui l’habitent!
Salimo la Davide. Dziko lapansi ndi la Yehova ndi zonse zimene zili mʼmenemo, dziko ndi onse amene amakhala mʼmenemo;
2 Car il l’a fondée sur les mers, Et affermie sur les fleuves.
pakuti Iye ndiye anayika maziko ake pa nyanja ndi kulikhazika pamwamba pa madzi.
3 Qui pourra monter à la montagne de l’Éternel? Qui s’élèvera jusqu’à son lieu saint?
Ndani angakwere phiri la Yehova? Ndani angathe kuyima pa malo ake opatulika?
4 Celui qui a les mains innocentes et le cœur pur; Celui qui ne livre pas son âme au mensonge, Et qui ne jure pas pour tromper.
Iye amene ali ndi mʼmanja moyera ndi mtima woyera, amene sapereka moyo wake kwa fano kapena kulumbira mwachinyengo.
5 Il obtiendra la bénédiction de l’Éternel, La miséricorde du Dieu de son salut.
Iyeyo adzalandira madalitso kwa Yehova ndipo Mulungu mpulumutsi wake adzagamula kuti alibe mlandu.
6 Voilà le partage de la génération qui l’invoque, De ceux qui cherchent ta face, Dieu de Jacob! (Pause)
Umenewo ndiwo mʼbado wa amene amafunafuna Yehova; amene amafunafuna nkhope yanu, Inu Mulungu wa Yakobo. (Sela)
7 Portes, élevez vos linteaux; Élevez-vous, portes éternelles! Que le roi de gloire fasse son entrée!
Tukulani mitu yanu inu zipata; tsekukani, inu zitseko zakalekalenu, kuti Mfumu yaulemerero ilowe.
8 Qui est ce roi de gloire? L’Éternel fort et puissant, L’Éternel puissant dans les combats.
Kodi Mfumu yaulemereroyo ndani? Yehova Wamphamvuzonse, Yehova ndiye wamphamvu pa nkhondo.
9 Portes, élevez vos linteaux; Élevez-les, portes éternelles! Que le roi de gloire fasse son entrée!
Tukulani mitu yanu, inu zipata; tsekukani, inu zitseko zakalekalenu, kuti Mfumu yaulemerero ilowe.
10 Qui donc est ce roi de gloire? L’Éternel des armées: Voilà le roi de gloire! (Pause)
Kodi Mfumu yaulemereroyo ndani? Yehova Wamphamvuzonse, Iye ndiye Mfumu yaulemerero. (Sela)