< Psaumes 150 >
1 Louez l’Éternel! Louez Dieu dans son sanctuaire! Louez-le dans l’étendue, où éclate sa puissance!
Tamandani Yehova. Tamandani Mulungu mʼmalo ake opatulika; mutamandeni ku thambo lake lamphamvu.
2 Louez-le pour ses hauts faits! Louez-le selon l’immensité de sa grandeur!
Mutamandeni chifukwa cha machitidwe ake amphamvu; mutamandeni chifukwa cha ukulu wake wopambana.
3 Louez-le au son de la trompette! Louez-le avec le luth et la harpe!
Mutamandeni poyimba malipenga, mutamandeni ndi pangwe ndi zeze.
4 Louez-le avec le tambourin et avec des danses! Louez-le avec les instruments à cordes et le chalumeau!
Mutamandeni ndi matambolini ndi kuvina, mutamandeni ndi zingwe ndi zitoliro.
5 Louez-le avec les cymbales sonores! Louez-le avec les cymbales retentissantes!
Mutamandeni ndi ziwaya zolira za malipenga, mutamandeni ndi ziwaya zolira kwambiri.
6 Que tout ce qui respire loue l’Éternel! Louez l’Éternel!
Chamoyo chilichonse chopuma chitamande Yehova. Tamandani Yehova.