< Psaumes 147 >
1 Louez l’Éternel! Car il est beau de célébrer notre Dieu, Car il est doux, il est bienséant de le louer.
Tamandani Yehova. Nʼkwabwino kwambiri kuyimba nyimbo zamatamando kwa Mulungu wathu, nʼkokondweretsa ndi koyenera kumutamanda!
2 L’Éternel rebâtit Jérusalem, Il rassemble les exilés d’Israël;
Yehova akumanga Yerusalemu; Iye akusonkhanitsa amʼndende a Israeli.
3 Il guérit ceux qui ont le cœur brisé, Et il panse leurs blessures.
Akutsogolera anthu osweka mtima ndi kumanga mabala awo.
4 Il compte le nombre des étoiles, Il leur donne à toutes des noms.
Amadziwa chiwerengero cha nyenyezi, ndipo iliyonse amayitchula dzina.
5 Notre Seigneur est grand, puissant par sa force, Son intelligence n’a point de limite.
Yehova ndi wamkulu ndi wamphamvu kwambiri; nzeru zake zilibe malire.
6 L’Éternel soutient les malheureux, Il abaisse les méchants jusqu’à terre.
Yehova amagwiriziza anthu odzichepetsa, koma amagwetsa pansi anthu oyipa.
7 Chantez à l’Éternel avec actions de grâces, Célébrez notre Dieu avec la harpe!
Imbirani Yehova ndi mayamiko; imbani nyimbo kwa Mulungu ndi pangwe.
8 Il couvre les cieux de nuages, Il prépare la pluie pour la terre; Il fait germer l’herbe sur les montagnes.
Iye amaphimba mlengalenga ndi mitambo; amapereka mvula ku dziko lapansi ndi kumeretsa udzu mʼmapiri.
9 Il donne la nourriture au bétail, Aux petits du corbeau quand ils crient,
Iye amapereka chakudya kwa ngʼombe ndi kwa ana a makwangwala pamene akulira chakudya.
10 Ce n’est pas dans la vigueur du cheval qu’il se complaît, Ce n’est pas dans les jambes de l’homme qu’il met son plaisir;
Chikondwerero chake sichili mʼmphamvu za kavalo, kapena mʼmiyendo ya anthu amphamvu.
11 L’Éternel aime ceux qui le craignent, Ceux qui espèrent en sa bonté.
Yehova amakondwera ndi amene amamuopa, amene chiyembekezo chawo chili mʼchikondi chake chosasinthika.
12 Jérusalem, célèbre l’Éternel! Sion, loue ton Dieu!
Lemekeza Yehova, iwe Yerusalemu; tamanda Mulungu wako, iwe Ziyoni,
13 Car il affermit les barres de tes portes, Il bénit tes fils au milieu de toi;
pakuti Iye amalimbitsa mipiringidzo ya zipata zako ndi kudalitsa anthu ako mwa iwe.
14 Il rend la paix à ton territoire, Il te rassasie du meilleur froment.
Iye amabweretsa mtendere mʼmalire mwako ndi kukukhutitsa ndi ufa wa tirigu wosalala.
15 Il envoie ses ordres sur la terre: Sa parole court avec vitesse.
Iyeyo amapereka lamulo pa dziko lapansi; mawu ake amayenda mwaliwiro.
16 Il donne la neige comme de la laine, Il répand la gelée blanche comme de la cendre;
Amagwetsa chisanu ngati ubweya ndi kumwaza chipale ngati phulusa.
17 Il lance sa glace par morceaux; Qui peut résister devant son froid?
Amagwetsa matalala ngati miyala. Kodi ndani angathe kupirira kuzizira kwake?
18 Il envoie sa parole, et il les fond; Il fait souffler son vent, et les eaux coulent.
Amatumiza mawu ake ndipo chisanucho chimasungunuka; amawombetsa mphepo ndipo madzi amayenda.
19 Il révèle sa parole à Jacob, Ses lois et ses ordonnances à Israël;
Iye anawulula mawu ake kwa Yakobo, malamulo ake ndi zophunzitsa zake kwa Israeli.
20 Il n’a pas agi de même pour toutes les nations, Et elles ne connaissent point ses ordonnances. Louez l’Éternel!
Sanachitepo zimenezi kwa mtundu wina uliwonse wa anthu; anthu enawo sadziwa malamulo ake. Tamandani Yehova.