< Psaumes 146 >
1 Louez l’Éternel! Mon âme, loue l’Éternel!
Tamandani Yehova. Tamanda Yehova, iwe moyo wanga.
2 Je louerai l’Éternel tant que je vivrai, Je célébrerai mon Dieu tant que j’existerai.
Ndidzatamanda Yehova ndi moyo wanga wonse; ndidzayimba nyimbo zamatamando kwa Mulungu wanga nthawi yonse ya moyo wanga.
3 Ne vous confiez pas aux grands, Aux fils de l’homme, qui ne peuvent sauver.
Musamadalire mafumu, anthu osakhalitsa, amene sangathe kupulumutsa.
4 Leur souffle s’en va, ils rentrent dans la terre, Et ce même jour leurs desseins périssent.
Pamene mizimu yawo yachoka, iwo amabwerera ku dothi; zimene ankafuna kuchita zimatha tsiku lomwelo.
5 Heureux celui qui a pour secours le Dieu de Jacob, Qui met son espoir en l’Éternel, son Dieu!
Wodala ndi amene thandizo lake ndi Mulungu wa Yakobo.
6 Il a fait les cieux et la terre, La mer et tout ce qui s’y trouve. Il garde la fidélité à toujours.
Wolenga kumwamba ndi dziko lapansi, nyanja ndi zonse zili mʼmenemo; Yehova, amene ndi wokhulupirika kwamuyaya.
7 Il fait droit aux opprimés; Il donne du pain aux affamés; L’Éternel délivre les captifs;
Iye amachitira chilungamo anthu oponderezedwa ndipo amapereka chakudya kwa anthu anjala. Yehova amamasula amʼndende,
8 L’Éternel ouvre les yeux des aveugles; L’Éternel redresse ceux qui sont courbés; L’Éternel aime les justes.
Yehova amatsekula maso anthu osaona, Yehova amadzutsa onse amene awerama pansi, Yehova amakonda anthu olungama.
9 L’Éternel protège les étrangers, Il soutient l’orphelin et la veuve, Mais il renverse la voie des méchants.
Yehova amasamalira alendo ndipo amathandiza ana ndi akazi amasiye, koma amasokoneza njira za anthu oyipa.
10 L’Éternel règne éternellement; Ton Dieu, ô Sion! Subsiste d’âge en âge! Louez l’Éternel!
Yehova ndiye Mfumu mpaka muyaya, Mulungu wako iwe Ziyoni, pa mibado yonse. Tamandani Yehova.