< Proverbes 3 >

1 Mon fils, n’oublie pas mes enseignements, Et que ton cœur garde mes préceptes;
Mwana wanga, usayiwale malangizo anga, mtima wako usunge malamulo anga.
2 Car ils prolongeront les jours et les années de ta vie, Et ils augmenteront ta paix.
Ukatero zaka za moyo wako zidzachuluka ndipo udzakhala pa mtendere.
3 Que la bonté et la fidélité ne t’abandonnent pas; Lie-les à ton cou, écris-les sur la table de ton cœur.
Makhalidwe ochitira ena chifundo ndi owonetsa kukhulupirika asakuchokere. Uwamangirire mʼkhosi mwako ngati mkanda ndi kuwalemba pa mtima pako.
4 Tu acquerras ainsi de la grâce et une raison saine, Aux yeux de Dieu et des hommes.
Ukatero udzapeza kuyanja ndi mbiri yabwino pamaso pa Mulungu ndi anthu.
5 Confie-toi en l’Éternel de tout ton cœur, Et ne t’appuie pas sur ta sagesse;
Uzikhulupirira Yehova ndi mtima wako wonse ndipo usadalire nzeru zako za kumvetsa zinthu.
6 Reconnais-le dans toutes tes voies, Et il aplanira tes sentiers.
Pa zochita zako zonse uvomereze kuti Mulungu alipo, ndipo Iye adzawongola njira zako.
7 Ne sois point sage à tes propres yeux, Crains l’Éternel, et détourne-toi du mal:
Usamadzione ngati wa nzeru. Uziopa Yehova ndi kupewa zoyipa.
8 Ce sera la santé pour tes muscles, Et un rafraîchissement pour tes os.
Ukatero thupi lako lidzakhala la moyo wabwino ndi mafupa ako adzakhala olimba.
9 Honore l’Éternel avec tes biens, Et avec les prémices de tout ton revenu:
Uzilemekeza Yehova ndi chuma chako chonse; zokolola zonse zoyamba kucha uzilemekeza nazonso Yehova.
10 Alors tes greniers seront remplis d’abondance, Et tes cuves regorgeront de moût.
Ukatero nkhokwe zako zidzadzaza ndi zinthu zambiri, ndiponso mitsuko yako idzadzaza ndi vinyo.
11 Mon fils, ne méprise pas la correction de l’Éternel, Et ne t’effraie point de ses châtiments;
Mwana wanga usanyoze malangizo a Yehova, ndipo usayipidwe ndi chidzudzulo chake.
12 Car l’Éternel châtie celui qu’il aime, Comme un père l’enfant qu’il chérit.
Paja Yehova amadzudzula amene amamukonda, monga abambo achitira mwana amene amakondwera naye.
13 Heureux l’homme qui a trouvé la sagesse, Et l’homme qui possède l’intelligence!
Wodala munthu amene wapeza nzeru, munthu amene walandira nzeru zomvetsa zinthu,
14 Car le gain qu’elle procure est préférable à celui de l’argent, Et le profit qu’on en tire vaut mieux que l’or;
pakuti phindu la nzeru ndi labwino kuposa la siliva, phindu lakelo ndi labwino kuposanso golide.
15 Elle est plus précieuse que les perles, Elle a plus de valeur que tous les objets de prix.
Nzeru ndi yoposa miyala yamtengowapatali; ndipo zonse zimene umazikhumba sizingafanane ndi nzeru.
16 Dans sa droite est une longue vie; Dans sa gauche, la richesse et la gloire.
Mʼdzanja lake lamanja muli moyo wautali; mʼdzanja lake lamanzere muli chuma ndi ulemu.
17 Ses voies sont des voies agréables, Et tous ses sentiers sont paisibles.
Njira zake ndi njira zosangalatsa, ndipo mu njira zake zonse muli mtendere.
18 Elle est un arbre de vie pour ceux qui la saisissent, Et ceux qui la possèdent sont heureux.
Nzeru ili ngati mtengo wopatsa moyo kwa oyigwiritsitsa; wodala munthu amene amayigwiritsa kwambiri.
19 C’est par la sagesse que l’Éternel a fondé la terre, C’est par l’intelligence qu’il a affermi les cieux;
Yehova anakhazikitsa dziko lapansi pogwiritsa ntchito nzeru. Anagwiritsanso ntchito nzeru zakudziwa bwino zinthu pamene ankakhazikitsa zakumwamba.
20 C’est par sa science que les abîmes se sont ouverts, Et que les nuages distillent la rosée.
Mwa nzeru zake Yehova anatumphutsa madzi kuchokera mʼnthaka ndiponso mitambo inagwetsa mvula.
21 Mon fils, que ces enseignements ne s’éloignent pas de tes yeux, Garde la sagesse et la réflexion:
Mwana wanga usunge nzeru yeniyeni ndi khalidwe lomalingarira zinthu bwino. Zimenezi zisakuchokere.
22 Elles seront la vie de ton âme, Et l’ornement de ton cou.
Zimenezi zidzakupatsa moyo, moyo wake wosangalatsa ndi wabwino ngati mkanda wa mʼkhosi.
23 Alors tu marcheras avec assurance dans ton chemin, Et ton pied ne heurtera pas.
Choncho udzayenda pa njira yako mosaopa kanthu, ndipo phazi lako silidzapunthwa;
24 Si tu te couches, tu seras sans crainte; Et quand tu seras couché, ton sommeil sera doux.
pamene ugona pansi, sudzachita mantha; ukadzagona pansi tulo tako tidzakhala tokoma.
25 Ne redoute ni une terreur soudaine, Ni une attaque de la part des méchants;
Usaope tsoka lobwera mwadzidzidzi kapena chiwonongeko chimene chidzagwera anthu oyipa,
26 Car l’Éternel sera ton assurance, Et il préservera ton pied de toute embûche.
pakuti Yehova adzakulimbitsa mtima ndipo adzasunga phazi lako kuti lisakodwe mu msampha.
27 Ne refuse pas un bienfait à celui qui y a droit, Quand tu as le pouvoir de l’accorder.
Usaleke kuchitira zabwino amene ayenera kulandira zabwino, pamene uli nazo mphamvu zochitira zimenezi.
28 Ne dis pas à ton prochain: Va et reviens, Demain je donnerai! Quand tu as de quoi donner.
Usanene kwa mnansi wako kuti, “Pita, uchite kubweranso. Ndidzakupatsa mawa” pamene uli nazo tsopano.
29 Ne médite pas le mal contre ton prochain, Lorsqu’il demeure tranquillement près de toi.
Usamukonzere chiwembu mnansi wako, amene anakhala nawe pafupi mokudalira.
30 Ne conteste pas sans motif avec quelqu’un, Lorsqu’il ne t’a point fait de mal.
Usakangane ndi munthu wopanda chifukwa pamene iye sanakuchitire zoyipa.
31 Ne porte pas envie à l’homme violent, Et ne choisis aucune de ses voies.
Usachite naye nsanje munthu wachiwawa kapena kutsanzira khalidwe lake lililonse.
32 Car l’Éternel a en horreur les hommes pervers, Mais il est un ami pour les hommes droits;
Pakuti Yehova amanyansidwa ndi munthu woyipa koma amayanjana nawo anthu olungama.
33 La malédiction de l’Éternel est dans la maison du méchant, Mais il bénit la demeure des justes;
Yehova amatemberera nyumba ya munthu woyipa, koma amadalitsa nyumba ya anthu olungama.
34 Il se moque des moqueurs, Mais il fait grâce aux humbles;
Anthu onyoza, Iye amawanyoza, koma amakomera mtima anthu odzichepetsa.
35 Les sages hériteront la gloire, Mais les insensés ont la honte en partage.
Anthu anzeru adzalandira ulemu, koma zitsiru adzazichititsa manyazi.

< Proverbes 3 >