< Nombres 28 >

1 L’Éternel parla à Moïse, et dit: Donne cet ordre aux enfants d’Israël, et dis-leur:
Yehova anawuza Mose kuti,
2 Vous aurez soin de me présenter, au temps fixé, mon offrande, l’aliment de mes sacrifices consumés par le feu, et qui me sont d’une agréable odeur.
“Lamula Aisraeli kuti, ‘Onetsetsani kuti mukupereka kwa Ine pa nthawi yoyikika, chopereka cha chakudya chotentha pa moto monga fungo lokoma kwa Ine.’
3 Tu leur diras: Voici le sacrifice consumé par le feu que vous offrirez à l’Éternel: chaque jour, deux agneaux d’un an sans défaut, comme holocauste perpétuel.
Awuze kuti, ‘Nsembe ya chakudya imene muzipereka pa moto kwa Yehova tsiku ndi tsiku ndi iyi: Ana ankhosa a chaka chimodzi awiri, wopanda chilema.
4 Tu offriras l’un des agneaux le matin, et l’autre agneau entre les deux soirs,
Mmawa muzipereka mwana wankhosa mmodzi ndipo winayo madzulo.
5 et, pour l’offrande, un dixième d’épha de fleur de farine pétrie dans un quart de hin d’huile d’olives concassées.
Muziperekanso kilogalamu imodzi ya ufa wosalala wosakaniza ndi lita imodzi ya mafuta a olivi.
6 C’est l’holocauste perpétuel, qui a été offert à la montagne de Sinaï; c’est un sacrifice consumé par le feu, d’une agréable odeur à l’Éternel.
Iyi ndi nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku imene analamula pa phiri la Sinai kuti ikhale fungo lokoma, nsembe yopsereza pa moto yopereka kwa Yehova.
7 La libation sera d’un quart de hin pour chaque agneau: c’est dans le lieu saint que tu feras la libation de vin à l’Éternel.
Chopereka chachakumwa chikhale lita imodzi yachakumwa chaukali pa nkhosa iliyonse. Muzithira pamalo opatulika, kupereka kwa Yehova.
8 Tu offriras le second agneau entre les deux soirs, avec une offrande et une libation semblables à celles du matin; c’est un sacrifice consumé par le feu, d’une agréable odeur à l’Éternel.
Muzipereka mwana wankhosa winayo madzulo, pamodzi ndi chopereka chachakudya monga poyamba paja ndi chopereka chachakumwa monga mmawa. Ichi ndi chopereka chachakudya, fungo lokoma kwa Yehova.’”
9 Le jour du sabbat, vous offrirez deux agneaux d’un an sans défaut, et, pour l’offrande, deux dixièmes de fleur de farine pétrie à l’huile, avec la libation.
“‘Pa tsiku la Sabata, muzipereka nsembe ana ankhosa awiri a chaka chimodzi wopanda chilema, pamodzi ndi chopereka chachakumwa ndi chopereka chachakudya chokwana makilogalamu awiri a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta.
10 C’est l’holocauste du sabbat, pour chaque sabbat, outre l’holocauste perpétuel et la libation.
Iyi ndi nsembe yopsereza ya pa Sabata iliyonse, kuwonjezera pa nsembe yopsereza ya nthawi zonse ndi chopereka chake chachakumwa.’”
11 Au commencement de vos mois, vous offrirez en holocauste à l’Éternel deux jeunes taureaux, un bélier, et sept agneaux d’un an sans défaut;
“Pa tsiku loyamba la mwezi uliwonse muzipereka kwa Yehova nsembe yopsereza ya ana angʼombe aamuna awiri, nkhosa yayimuna imodzi, ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri a chaka chimodzi, onse wopanda chilema.
12 et, comme offrande pour chaque taureau, trois dixièmes de fleur de farine pétrie à l’huile; comme offrande pour le bélier, deux dixièmes de fleur de farine pétrie à l’huile;
Pa ngʼombe yayimuna iliyonse pakhale chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; ndi nkhosa yayimuna, chopereka cha chakudya cha makilogalamu awiri a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta;
13 comme offrande pour chaque agneau, un dixième de fleur de farine pétrie à l’huile. C’est un holocauste, un sacrifice consumé par le feu, d’une agréable odeur à l’Éternel.
ndipo pa mwana wankhosa aliyense, chopereka cha ufa wa kilogalamu imodzi ya ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, izi ndi za nsembe yopsereza, fungo lokoma, nsembe yotentha pa moto ya kwa Yehova.
14 Les libations seront d’un demi-hin de vin pour un taureau, d’un tiers de hin pour un bélier, et d’un quart de hin pour un agneau. C’est l’holocauste du commencement du mois, pour chaque mois, pour tous les mois de l’année.
Pa ngʼombe yayimuna iliyonse pakhale chopereka cha chakumwa cha malita awiri a vinyo; ndipo pa nkhosa yayimuna, lita limodzi ndi theka, ndipo pa mwana wankhosa, lita limodzi. Iyi ndi nsembe yopsereza ya mwezi ndi mwezi yoperekedwa pa mwezi watsopano mʼkati mwa chaka.
15 On offrira à l’Éternel un bouc, en sacrifice d’expiation, outre l’holocauste perpétuel et la libation.
Powonjezera pa nsembe yopsereza ya nthawi zonse ndi chopereka chake cha chakumwa, mbuzi yayimuna imodzi iperekedwe kwa Yehova ngati nsembe yopepesera machimo.
16 Le premier mois, le quatorzième jour du mois, ce sera la Pâque de l’Éternel.
“‘Pa tsiku la 14 la mwezi woyamba muzichita Paska wa Yehova.
17 Le quinzième jour de ce mois sera un jour de fête. On mangera pendant sept jours des pains sans levain.
Pa tsiku la 15 la mwezi womwewo pazikhala chikondwerero. Muzidya buledi wopanda yisiti kwa masiku asanu ndi awiri.
18 Le premier jour, il y aura une sainte convocation: vous ne ferez aucune œuvre servile.
Pa tsiku loyamba muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse.
19 Vous offrirez en holocauste à l’Éternel un sacrifice consumé par le feu: deux jeunes taureaux, un bélier, et sept agneaux d’un an sans défaut.
Koma muzipereka kwa Yehova nsembe yotentha pa moto, nsembe yopsereza ya ana angʼombe aamuna awiri, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa asanu ndi awiri aamuna a chaka chimodzi, onsewo wopanda chilema.
20 Vous y joindrez l’offrande de fleur de farine pétrie à l’huile, trois dixièmes pour un taureau, deux dixièmes pour un bélier,
Pamodzi ndi ngʼombe yayimuna iliyonse, muzikonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; makilogalamu awiri pa nkhosa yayimuna iliyonse.
21 et un dixième pour chacun des sept agneaux.
Kilogalamu imodzi pa mwana wankhosa aliyense mwa ana ankhosa asanu ndi awiri aja.
22 Vous offrirez un bouc en sacrifice d’expiation, afin de faire pour vous l’expiation.
Muziphatikizapo mbuzi yayimuna monga nsembe yopepesera machimo anu.
23 Vous offrirez ces sacrifices, outre l’holocauste du matin, qui est un holocauste perpétuel.
Muzikonza zimenezi nthawi zonse, powonjezera pa nsembe yopsereza ya mmawa.
24 Vous les offrirez chaque jour, pendant sept jours, comme l’aliment d’un sacrifice consumé par le feu, d’une agréable odeur à l’Éternel. On les offrira, outre l’holocauste perpétuel et la libation.
Motere muzikonza chakudya cha nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pa masiku asanu ndi awiri ngati fungo lokomera Yehova. Zimenezi ziziperekedwa kuwonjezera pa nsembe yopsereza ya nthawi zonse pamodzi ndi nsembe yachakumwa.
25 Le septième jour, vous aurez une sainte convocation: vous ne ferez aucune œuvre servile.
Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse.
26 Le jour des prémices, où vous présenterez à l’Éternel une offrande, à votre fête des semaines, vous aurez une sainte convocation: vous ne ferez aucune œuvre servile.
“‘Pa tsiku la zipatso zoyambirira kucha, pamene mukupereka chopereka cha chakudya chatsopano kwa Yehova, pa nthawi ya chikondwerero cha Masabata, muzichita msonkhano wopatulika ndipo musagwire ntchito zolemetsa.
27 Vous offrirez en holocauste, d’une agréable odeur à l’Éternel, deux jeunes taureaux, un bélier, et sept agneaux d’un an.
Muzipereka nsembe zopsereza za ana angʼombe aamuna awiri, nkhosa imodzi yayimuna ndi ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri a chaka chimodzi monga fungo lokomera Yehova.
28 Vous y joindrez l’offrande de fleur de farine pétrie à l’huile, trois dixièmes pour chaque taureau, deux dixièmes pour le bélier,
Pa ngʼombe yayimuna iliyonse pazikhala chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, pa nkhosa yayimuna iliyonse makilogalamu awiri.
29 et un dixième pour chacun des sept agneaux.
Ndipo pa mwana wankhosa aliyense mwa asanu ndi awiri aja, kilogalamu imodzi.
30 Vous offrirez un bouc, afin de faire pour vous l’expiation.
Muziperekanso mbuzi yayimuna imodzi kuti izikhala nsembe yopepesera machimo anu.
31 Vous offrirez ces sacrifices, outre l’holocauste perpétuel et l’offrande. Vous aurez des agneaux sans défaut, et vous joindrez les libations.
Muzipereka zimenezi pamodzi ndi zopereka za zakumwa ndi nsembe yake ya chakudya. Onetsetsani kuti nyamazo zilibe chilema.

< Nombres 28 >