< Lamentations 5 >

1 Souviens-toi, Éternel, de ce qui nous est arrivé! Regarde, vois notre opprobre!
Inu Yehova, kumbukirani zimene zinatichitikira; yangʼanani ndipo muone kunyozeka kwathu.
2 Notre héritage a passé à des étrangers, Nos maisons à des inconnus.
Apereka cholowa chathu kwa obwera, nyumba zathu kwa alendo.
3 Nous sommes orphelins, sans père; Nos mères sont comme des veuves.
Takhala amasiye ndi wopanda abambo, amayi athu ali ngati akazi amasiye.
4 Nous buvons notre eau à prix d’argent, Nous payons notre bois.
Tiyenera kugula madzi amene timamwa, nkhuni zathunso nʼzogula.
5 Nous sommes poursuivis, le joug sur le cou; Nous sommes épuisés, nous n’avons point de repos.
Otilondola atigwira pakhosi; tafowoka ndipo sakutilola kupumula.
6 Nous avons tendu la main vers l’Égypte, vers l’Assyrie, Pour nous rassasier de pain.
Tinadzipereka kwa Aigupto ndi kwa Asiriya kuti tipeze chakudya.
7 Nos pères ont péché, ils ne sont plus, Et c’est nous qui portons la peine de leurs iniquités.
Makolo athu anachimwa ndipo anafa kale, koma chilango chawo chili pa ife.
8 Des esclaves dominent sur nous, Et personne ne nous délivre de leurs mains.
Akapolo akutilamulira, ndipo palibe ndi mmodzi yemwe angatimasule mʼdzanja lawo.
9 Nous cherchons notre pain au péril de notre vie, Devant l’épée du désert.
Timapeza chakudya chathu poyika miyoyo yathu pa chiswe chifukwa cha lupanga mʼchipululu.
10 Notre peau est brûlante comme un four, Par l’ardeur de la faim.
Khungu lathu latentha ngati uvuni mʼngʼanjo, chifukwa cha kuwawa kwa njala.
11 Ils ont déshonoré les femmes dans Sion, Les vierges dans les villes de Juda.
Amayi agwiriridwa mu Ziyoni, ndi anamwali mʼmizinda ya Yuda.
12 Des chefs ont été pendus par leurs mains; La personne des vieillards n’a pas été respectée.
Akalonga athu akuwapachika pomangirira manja awo, akuluakulu sakuwalemekeza.
13 Les jeunes hommes ont porté la meule, Les enfants chancelaient sous des fardeaux de bois.
Achinyamata akukakamizidwa kupera tirigu; anyamata akudzandira ndi mitolo ya nkhuni.
14 Les vieillards ne vont plus à la porte, Les jeunes hommes ont cessé leurs chants.
Akuluakulu anachokapo pa chipata cha mzinda; achinyamata aleka nyimbo zawo.
15 La joie a disparu de nos cœurs, Le deuil a remplacé nos danses.
Chimwemwe chachoka mʼmitima yathu; kuvina kwathu kwasanduka maliro.
16 La couronne de notre tête est tombée! Malheur à nous, parce que nous avons péché!
Chipewa chathu chaufumu chagwa pamutu pathu. Tsoka kwa ife, chifukwa tachimwa!
17 Si notre cœur est souffrant, Si nos yeux sont obscurcis,
Mitima yathu yakomoka chifukwa cha zimenezi, chifukwa cha zinthu zimenezi maso athu sakuona bwino,
18 C’est que la montagne de Sion est ravagée, C’est que les renards s’y promènent.
pakuti phiri la Ziyoni, limene lasanduka bwinja, nkhandwe zikungoyendayendapo.
19 Toi, l’Éternel, tu règnes à jamais; Ton trône subsiste de génération en génération.
Inu Yehova, lamulirani kwamuyaya; mpando wanu waufumu udzakhalabe ku mibadomibado.
20 Pourquoi nous oublierais-tu pour toujours, Nous abandonnerais-tu pour de longues années?
Chifukwa chiyani mumatiyiwala nthawi zonse? Chifukwa chiyani mwatitaya nthawi yayitali chotere?
21 Fais-nous revenir vers toi, ô Éternel, et nous reviendrons! Donne-nous encore des jours comme ceux d’autrefois!
Yehova mutitembenuzire kwa Inu, kuti tibwerere; mukonzenso masiku athu akhale monga akale,
22 Nous aurais-tu entièrement rejetés, Et t’irriterais-tu contre nous jusqu’à l’excès?
pokhapokha ngati mwatitaya kotheratu, ndi kuti mwatikwiyira kobzola muyeso.

< Lamentations 5 >