< Josué 21 >

1 Les chefs de famille des Lévites s’approchèrent du sacrificateur Éléazar, de Josué, fils de Nun, et des chefs de famille des tribus des enfants d’Israël.
Tsono atsogoleri a mabanja a fuko la Levi anabwera kwa wansembe Eliezara, Yoswa mwana wa Nuni, ndi kwa atsogoleri a mabanja a mafuko onse a Aisraeli,
2 Ils leur parlèrent à Silo, dans le pays de Canaan, et dirent: L’Éternel a ordonné par Moïse qu’on nous donnât des villes pour habitation, et leurs banlieues pour notre bétail.
ku Silo mʼdziko la Kanaani ndipo anati, “Yehova analamula kudzera mwa Mose kuti atipatse mizinda kuti tikhalemo, pamodzi ndi malo odyetseramo ziweto zathu.”
3 Les enfants d’Israël donnèrent alors aux Lévites, sur leur héritage, les villes suivantes et leurs banlieues, d’après l’ordre de l’Éternel.
Choncho, Aisraeli anapereka kwa fuko la Levi mizinda iyi pamodzi ndi malo owetera ziweto zawo kuchokera ku madera awo, monga Yehova analamulira:
4 On tira le sort pour les familles des Kehathites; et les Lévites, fils du sacrificateur Aaron, eurent par le sort treize villes de la tribu de Juda, de la tribu de Siméon et de la tribu de Benjamin;
Maere oyamba anagwera mabanja a Kohati, Alevi amene anali zidzukulu za wansembe Aaroni anapatsidwa mizinda 13 kuchokera ku mafuko a Yuda, Simeoni ndi Benjamini.
5 les autres fils de Kehath eurent par le sort dix villes des familles de la tribu d’Éphraïm, de la tribu de Dan et de la demi-tribu de Manassé.
Ndipo mabanja otsala a Kohati anapatsidwa mizinda khumi kuchokera ku mafuko a Efereimu, Dani ndi theka la fuko la Manase.
6 Les fils de Guerschon eurent par le sort treize villes des familles de la tribu d’Issacar, de la tribu d’Aser, de la tribu de Nephthali et de la demi-tribu de Manassé en Basan.
Zidzukulu za Geresoni zinapatsidwa mizinda 13 kuchokera ku mabanja a mafuko a Isakara, Aseri, Nafutali ndi theka la fuko la Manase ku Basani.
7 Les fils de Merari, selon leurs familles, eurent douze villes de la tribu de Ruben, de la tribu de Gad et de la tribu de Zabulon.
Mabanja a Merari anapatsidwa mizinda khumi ndi iwiri kuchokera ku mafuko a Rubeni, Gadi ndi Zebuloni.
8 Les enfants d’Israël donnèrent aux Lévites, par le sort, ces villes et leurs banlieues, comme l’Éternel l’avait ordonné par Moïse.
Choncho Aisraeli anapereka kwa fuko la Levi mizindayi pamodzi ndi malo odyetserako ziweto pogwiritsa ntchito maere, monga Yehova analamula kudzera mwa Mose.
9 Ils donnèrent de la tribu des fils de Juda et de la tribu des fils de Siméon les villes qui vont être nominativement désignées,
Awa ndi mayina a mizinda ya mafuko a Yuda ndi Simeoni imene inaperekedwa kwa zidzukulu za Aaroni,
10 et qui furent pour les fils d’Aaron d’entre les familles des Kehathites et des fils de Lévi, car le sort les avait indiqués les premiers.
ku banja la Kohati amene anali Alevi. Paja maere oyamba anagwera mabanja a Kohati kuti alandira mizinda.
11 Ils leur donnèrent Kirjath-Arba, qui est Hébron, dans la montagne de Juda, et la banlieue qui l’entoure: Arba était le père d’Anak.
Anapatsidwa mzinda wa Kiriati Ariba. (Paja Ariba ndiye kholo la Anaaki). Dzina lina la mzindawu ndi Hebroni, ndipo unali mʼdziko la mapiri la Yuda. Pamodzi ndi mzindawu anapatsidwanso mabusa ake onse ozungulira.
12 Le territoire de la ville et ses villages furent accordés à Caleb, fils de Jephunné, pour sa possession.
Komabe minda ndi midzi yozungulira mizindayi inali itaperekedwa kale kwa Kalebe, mwana wa Yefune kuti ikhale cholowa chake.
13 Ils donnèrent donc aux fils du sacrificateur Aaron la ville de refuge pour les meurtriers, Hébron et sa banlieue, Libna et sa banlieue,
Choncho zidzukulu za Aaroni wansembe, zinapatsidwa Hebroni (mzinda wopulumukirako amene wapha munthu), Libina,
14 Jatthir et sa banlieue, Eschthemoa et sa banlieue,
Yatiri, Esitemowa,
15 Holon et sa banlieue, Debir et sa banlieue,
Holoni, Debri,
16 Aïn et sa banlieue, Jutta et sa banlieue, et Beth-Schémesch et sa banlieue, neuf villes de ces deux tribus;
Aini, Yuta, ndi Beti-Semesi pamodzi ndi mabusa odyetseramo ziweto ozungulira mizindayi. Yonse pamodzi inali mizinda isanu ndi inayi yochokera ku mafuko awiriwa.
17 et de la tribu de Benjamin, Gabaon et sa banlieue, Guéba et sa banlieue,
Fuko la Benjamini linapereka Gibiyoni, Geba,
18 Anathoth et sa banlieue, et Almon et sa banlieue, quatre villes.
Anatoti ndi Alimoni, pamodzi ndi mabusa odyetsera ziweto ozungulira mizindayi. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
19 Total des villes des sacrificateurs, fils d’Aaron: treize villes, et leurs banlieues.
Choncho mizinda 13 pamodzi ndi malo odyetsera ziweto anapatsidwa kwa ansembe, zidzukulu za Aaroni.
20 Les Lévites appartenant aux familles des autres fils de Kehath eurent par le sort des villes de la tribu d’Éphraïm.
Mabanja ena otsalira a Kohati a fuko la Levi anapatsidwa mizinda iyi kuchokera ku fuko la Efereimu:
21 On leur donna la ville de refuge pour les meurtriers, Sichem et sa banlieue, dans la montagne d’Éphraïm, Guézer et sa banlieue,
Mizinda ya Sekemu ndi Gezeri ndiye inali mizinda wopulumukirako munthu aliyense wopha mnzake mwangozi. Mizindayi inali ku mapiri a Efereimu.
22 Kibtsaïm et sa banlieue, et Beth-Horon et sa banlieue, quatre villes;
Analandiranso mizinda ya Gezeri, Kibuzaimu, Beti-Horoni pamodzi ndi malo odyetsera ziweto ozungulira mizindayi. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
23 de la tribu de Dan, Eltheké et sa banlieue, Guibbethon et sa banlieue,
Fuko la Dani linapereka mizinda ya Eliteke, Gibetoni,
24 Ajalon et sa banlieue, et Gath-Rimmon et sa banlieue, quatre villes;
Ayaloni, Gati-Rimoni pamodzi ndi mabusa odyetsera ziweto ozungulira mizindayi. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
25 et de la demi-tribu de Manassé, Thaanac et sa banlieue, et Gath-Rimmon et sa banlieue, deux villes.
Kuchokera ku theka la fuko la Manase analandira Taanaki ndi Gati-Rimoni pamodzi ndi malo awo owetera ziweto, mizinda iwiri.
26 Total des villes: dix, et leurs banlieues, pour les familles des autres fils de Kehath.
Mizinda khumi yonseyi pamodzi ndi malo odyetsera ziweto, zinapatsidwa ku mabanja ena onse a Akohati.
27 On donna aux fils de Guerschon, d’entre les familles des Lévites: de la demi-tribu de Manassé, la ville de refuge pour les meurtriers, Golan en Basan et sa banlieue, et Beeschthra et sa banlieue, deux villes;
Mabanja a Ageresoni a fuko la Levi anapatsidwa mizinda iwiri kuchokera ku theka la Manase wa kummawa, Golani ku Basani (mzinda wopulumukirako amene wapha munthu mwangozi) ndi Beesitera, pamodzi ndi malo awo odyetserako ziweto.
28 de la tribu d’Issacar, Kischjon et sa banlieue, Dabrath et sa banlieue,
Fuko la Isakara linapereka mizinda ya Kisoni, Daberati,
29 Jarmuth et sa banlieue, et En-Gannim et sa banlieue, quatre villes;
Yarimuti ndi Eni Ganimu, pamodzi ndi malo awo odyetsera ziweto. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
30 de la tribu d’Aser, Mischeal et sa banlieue, Abdon et sa banlieue,
Fuko la Aseri linapereka mizinda ya Misali, Abidoni,
31 Helkath et sa banlieue, et Rehob et sa banlieue, quatre villes;
Helikati ndi Rehobu pamodzi ndi malo awo odyetsera ziweto. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
32 et de la tribu de Nephthali, la ville de refuge pour les meurtriers, Kédesch en Galilée et sa banlieue, Hammoth-Dor et sa banlieue, et Karthan et sa banlieue, trois villes.
Fuko la Nafutali linapereka mizinda ya Kedesi wa ku Galileya, mzinda umene unali wopulumukiramo munthu wopha mnzake mwangozi. Analandiranso mizinda ya Hamoti-Dori ndi Karitani. Kuphatikizira apa, analandira malo odyetsera ziweto a mizindayi. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
33 Total des villes des Guerschonites, selon leurs familles: treize villes et leurs banlieues.
Mabanja onse a Ageresoni analandira mizinda 13 pamodzi ndi malo awo odyetsera a ziweto.
34 On donna au reste des Lévites, qui appartenaient aux familles des fils de Merari: de la tribu de Zabulon, Jokneam et sa banlieue, Kartha et sa banlieue,
Mabanja a Merari amene anali otsala a fuko la Levi, anapatsidwa mizinda iyi kuchokera ku fuko la Zebuloni: Yokineamu, Karita,
35 Dimna et sa banlieue, et Nahalal et sa banlieue, quatre villes;
Dimuna ndi Nahalali, pamodzi ndi malo awo odyetsera ziweto. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
36 de la tribu de Ruben, Betser et sa banlieue, Jahtsa et sa banlieue,
Kuchokera ku fuko la Rubeni analandira Bezeri, Yahaza,
37 Kedémoth et sa banlieue, et Méphaath et sa banlieue, quatre villes;
Kedemoti ndi Mefaati, pamodzi ndi malo awo odyetsera ziweto. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
38 et de la tribu de Gad, la ville de refuge pour les meurtriers, Ramoth en Galaad et sa banlieue, Mahanaïm et sa banlieue,
Kuchokera ku fuko la Gadi analandira mzinda wa Ramoti ku Giliyadi. Mzinda umene unali wopulumukiramo munthu wopha mnzake mwangozi.
39 Hesbon et sa banlieue, et Jaezer et sa banlieue, en tout quatre villes.
Analandiranso mizinda ya Mahanaimu, Hesiboni, Yazeri pamodzi ndi malo odyetserako ziweto ozungulira mizinda yonseyi. Yonse pamodzi inali mizindayi anayi.
40 Total des villes qui échurent par le sort aux fils de Merari, selon leurs familles, formant le reste des familles des Lévites: douze villes.
Choncho mabanja onse a Merari, amene anali otsala a fuko la Levi analandira mizinda khumi ndi iwiri pogwiritsa ntchito maere.
41 Total des villes des Lévites au milieu des propriétés des enfants d’Israël: quarante-huit villes, et leurs banlieues.
Motero mizinda 48 ya mʼdziko limene Aisraeli analanda inapatsidwa kwa Alevi, kuphatikizapo malo ake odyetsera ziweto.
42 Chacune de ces villes avait sa banlieue qui l’entourait; il en était de même pour toutes ces villes.
Iliyonse mwa mizindayi inali ndi malo owetera ziweto oyizungulira.
43 C’est ainsi que l’Éternel donna à Israël tout le pays qu’il avait juré de donner à leurs pères; ils en prirent possession et s’y établirent.
Motero Yehova anapereka kwa Israeli dziko limene analumbira kulipereka kwa makolo awo. Atalilandira anadzakhalamo.
44 L’Éternel leur accorda du repos tout alentour, comme il l’avait juré à leurs pères; aucun de leurs ennemis ne put leur résister, et l’Éternel les livra tous entre leurs mains.
Yehova anawapatsa mtendere mʼdziko lonse monga momwe analonjezera makolo awo. Palibe ndi mmodzi yemwe mwa adani awo amene anatha kuwagonjetsa chifukwa Yehova anapereka adani awo onse mʼmanja mwawo.
45 De toutes les bonnes paroles que l’Éternel avait dites à la maison d’Israël, aucune ne resta sans effet: toutes s’accomplirent.
Yehova anakwaniritsa zonse zimene analonjeza kwa Aisraeli.

< Josué 21 >