< Job 5 >

1 Crie maintenant! Qui te répondra? Auquel des saints t’adresseras-tu?
“Itana ngati ungathe, koma ndani adzakuyankhe? Kodi ndi kwa mngelo uti ungapezeko thandizo?
2 L’insensé périt dans sa colère, Le fou meurt dans ses emportements.
Mkwiyo umapha chitsiru, ndipo njiru imawononga wopusa.
3 J’ai vu l’insensé prendre racine; Puis soudain j’ai maudit sa demeure.
Ine ndinaona chitsiru chitamera mizu, koma mwadzidzidzi nyumba yake inatembereredwa.
4 Plus de prospérité pour ses fils; Ils sont foulés à la porte, et personne qui les délivre!
Ana ake alibe ndi chitetezo chomwe; amaponderezedwa mʼbwalo la milandu popanda owateteza.
5 Sa moisson est dévorée par des affamés, Qui viennent l’enlever jusque dans les épines, Et ses biens sont engloutis par des hommes altérés.
Anthu anjala amamudyera zokolola zake, amamutengera ndi za pa minga pomwe, ndipo anthu akhwinthi amafunkha chuma chake.
6 Le malheur ne sort pas de la poussière, Et la souffrance ne germe pas du sol;
Pakuti masautso satuluka mʼfumbi, ndipo kuwukira sikuchokera mʼdothi.
7 L’homme naît pour souffrir, Comme l’étincelle pour voler.
Komatu munthu amabadwira kuti azunzike monga momwe mbaliwali zimathethekera mlengalenga.
8 Pour moi, j’aurais recours à Dieu, Et c’est à Dieu que j’exposerais ma cause.
“Koma ndikanakhala ine, ndikanamudandawulira Mulungu; ndikanapereka mlandu wanga kwa Iye.
9 Il fait des choses grandes et insondables, Des merveilles sans nombre;
Iye amachita zozizwitsa zimene sizimvetsetseka, zodabwitsa zimene sizingatheke kuwerengedwa.
10 Il répand la pluie sur la terre, Et envoie l’eau sur les campagnes;
Iye amagwetsa mvula pa dziko lapansi, ndipo amathirira minda ya anthu.
11 Il relève les humbles, Et délivre les affligés;
Iye amakweza anthu wamba, ndipo iwo amene akulira amawayika pa malo otetezedwa.
12 Il anéantit les projets des hommes rusés, Et leurs mains ne peuvent les accomplir;
Iyeyo amalepheretsa chiwembu cha anthu ochenjera, kotero kuti cholinga chawo sichipindula kanthu.
13 Il prend les sages dans leur propre ruse, Et les desseins des hommes artificieux sont renversés:
Iye amakola anthu ochenjera mu msampha wa kuchenjera kwawo, ndipo zolinga za atambwali amazithetsa msangamsanga.
14 Ils rencontrent les ténèbres au milieu du jour, Ils tâtonnent en plein midi comme dans la nuit.
Mdima umawagwera nthawi yamasana; nthawi yamasana amayenda moyambasayambasa monga nthawi ya usiku.
15 Ainsi Dieu protège le faible contre leurs menaces, Et le sauve de la main des puissants;
Mulungu amapulumutsa amphawi ku lupanga la mʼkamwa mwawo; amawapulumutsa mʼmanja mwa anthu amphamvu.
16 Et l’espérance soutient le malheureux, Mais l’iniquité ferme la bouche.
Choncho osauka ali ndi chiyembekezo, ndipo anthu opanda chilungamo amawatseka pakamwa.
17 Heureux l’homme que Dieu châtie! Ne méprise pas la correction du Tout-Puissant.
“Wodala munthu amene Mulungu amamudzudzula; nʼchifukwa chake usanyoze chilango cha Wamphamvuzonse.
18 Il fait la plaie, et il la bande; Il blesse, et sa main guérit.
Pakuti Iye amavulaza koma amamanganso mabalawo; Iye amakantha munthu, komanso manja ake amachiritsa.
19 Six fois il te délivrera de l’angoisse, Et sept fois le mal ne t’atteindra pas.
Pakuti adzakupulumutsa ku masautso nthawi ndi nthawi, mavuto angachuluke bwanji, sadzakukhudza ndi pangʼono pomwe.
20 Il te sauvera de la mort pendant la famine, Et des coups du glaive pendant la guerre.
Pa nthawi ya njala adzakulanditsa ku imfa, ndipo nthawi ya nkhondo adzakupulumutsa ku lupanga.
21 Tu seras à l’abri du fléau de la langue, Tu seras sans crainte quand viendra la dévastation.
Adzakuteteza kwa anthu osinjirira, ndipo palibe chifukwa chochitira mantha pamene chiwonongeko chafika.
22 Tu te riras de la dévastation comme de la famine, Et tu n’auras pas à redouter les bêtes de la terre;
Uzidzaseka pa nthawi ya chiwonongeko ndi ya njala, ndipo palibe chifukwa chochitira mantha ndi zirombo za mʼdziko lapansi.
23 Car tu feras alliance avec les pierres des champs, Et les bêtes de la terre seront en paix avec toi.
Pakuti udzachita pangano ndi miyala ya mʼmunda mwako, ndipo nyama zakuthengo zidzakhala nawe mwamtendere.
24 Tu jouiras du bonheur sous ta tente, Tu retrouveras tes troupeaux au complet,
Udzadziwa kuti nyumba yako ndi malo otetezedwa; udzawerengera katundu wako ndipo sudzapeza kanthu kamene kasowapo.
25 Tu verras ta postérité s’accroître, Et tes rejetons se multiplier comme l’herbe des champs.
Udzadziwa kuti ana ako adzakhala ambiri, ndipo zidzukulu zako zidzakhala ngati udzu wa mʼdziko lapansi.
26 Tu entreras au sépulcre dans la vieillesse, Comme on emporte une gerbe en son temps.
Udzafika ku manda utakalamba, monga mitolo ya zokolola pa nyengo yake.
27 Voilà ce que nous avons reconnu, voilà ce qui est; A toi d’entendre et de mettre à profit.
“Ife tafufuza zimenezi ndipo ndi zoona, choncho uzimvere ndi kuzitsata.”

< Job 5 >