< Job 35 >
Ndipo Elihu anawonjeza kunena kuti,
2 Imagines-tu avoir raison, Penses-tu te justifier devant Dieu,
“Kodi mukuganiza kuti mukukhoza? Mukunena kuti, ‘Ndine wolungama pamaso pa Mulungu.’
3 Quand tu dis: Que me sert-il, Que me revient-il de ne pas pécher?
Komanso inu mukufunsa kuti, ‘Kodi phindu langa nʼchiyani, ndipo ndimapeza chiyani ndikapanda kuchimwa?’
4 C’est à toi que je vais répondre, Et à tes amis en même temps.
“Ine ndikufuna ndikuyankheni inu pamodzi ndi abwenzi anu omwe.
5 Considère les cieux, et regarde! Vois les nuées, comme elles sont au-dessus de toi!
Yangʼanani kumwamba ndipo muone mitambo imene ili kutali ndi inuyo.
6 Si tu pèches, quel tort lui causes-tu? Et quand tes péchés se multiplient, que lui fais-tu?
Inuyo mukachimwa, Iye zimamukhudza motani? Ngati machimo anu ndi ochuluka, zimenezo zimachita chiyani kwa Iye?
7 Si tu es juste, que lui donnes-tu? Que reçoit-il de ta main?
Ngati inu ndinu wolungama, mumamupatsa Iyeyo chiyani? Kapena Iye amalandira chiyani chochokera mʼdzanja lanu?
8 Ta méchanceté ne peut nuire qu’à ton semblable, Ta justice n’est utile qu’au fils de l’homme.
Kuyipa kwanu kumangokhudza anthu ngati inuyo, ndipo chilungamo chanu chimakhudza anthu anzanu.
9 On crie contre la multitude des oppresseurs, On se plaint de la violence d’un grand nombre;
“Anthu akufuwula chifukwa cha kuzunzidwa; akufuna chithandizo kuti achoke pansi pa ulamuliro wa anthu amphamvu.
10 Mais nul ne dit: Où est Dieu, mon créateur, Qui inspire des chants d’allégresse pendant la nuit,
Koma palibe amene akunena kuti, ‘Kodi ali kuti Mulungu, Mlengi wanga, amene amatisangalatsa nthawi ya usiku,
11 Qui nous instruit plus que les bêtes de la terre, Et nous donne l’intelligence plus qu’aux oiseaux du ciel?
amene amatiphunzitsa kupambana nyama za dziko lapansi ndipo amatipatsa nzeru kupambana mbalame zowuluka?’
12 On a beau crier alors, Dieu ne répond pas, A cause de l’orgueil des méchants.
Iye sayankha pamene anthu akufuwulira kwa Iye chifukwa cha kudzikuza kwa anthu oyipa.
13 C’est en vain que l’on crie, Dieu n’écoute pas, Le Tout-Puissant n’y a point égard.
Ndithu, Mulungu samva kupempha kwawo kopanda pake; Wamphamvuzonse sasamalira zimenezi.
14 Bien que tu dises que tu ne le vois pas, Ta cause est devant lui: attends-le!
Ndipo ndi bodza lalikulu kunena kuti Iye saona zimene zikuchitika. Iye adzaweruza molungama ngati inu mutamudikira
15 Mais, parce que sa colère ne sévit point encore, Ce n’est pas à dire qu’il ait peu souci du crime.
ndiye tsono popeza kuti ukali wake sukupereka chilango, zoyipa zambiri zimene anthu amachita,
16 Ainsi Job ouvre vainement la bouche, Il multiplie les paroles sans intelligence.
abambo Yobu mumangoyankhula zopandapake, mukungochulukitsa mawu opanda nzeru.”