< Job 12 >
1 Job prit la parole et dit:
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 On dirait, en vérité, que le genre humain c’est vous, Et qu’avec vous doit mourir la sagesse.
“Ndithudi inuyo ndinu anthu ndipo nzeru zanu zidzafera nanu pamodzi!
3 J’ai tout aussi bien que vous de l’intelligence, moi, Je ne vous suis point inférieur; Et qui ne sait les choses que vous dites?
Koma inenso ndili nazo nzeru ngati inu; ineyo sindine munthu wamba kwa inu. Ndani amene sadziwa zonse zimene mwanenazi?
4 Je suis pour mes amis un objet de raillerie, Quand j’implore le secours de Dieu; Le juste, l’innocent, un objet de raillerie!
“Ndasanduka chinthu choseketsa kwa abwenzi anga, ngakhale ndinkapemphera kwa Mulungu ndipo Iye ankandiyankha. Ine ndasanduka chinthu chongoseketsa, ngakhale ndili wolungama ndi wosalakwa!
5 Au malheur le mépris! C’est la devise des heureux; A celui dont le pied chancelle est réservé le mépris.
Anthu amene ali pabwino amanyoza anzawo amene ali pa tsoka. Tsokalo limagwa pa amene wayamba kale kugwa.
6 Il y a paix sous la tente des pillards, Sécurité pour ceux qui offensent Dieu, Pour quiconque se fait un dieu de sa force.
Nyumba za anthu achifwamba zimakhala pa mtendere, ndipo anthu amene amaputa Mulungu amakhala pabwino, amene amanyamula milungu yawo mʼmanja.
7 Interroge les bêtes, elles t’instruiront, Les oiseaux du ciel, ils te l’apprendront;
“Koma funsa nyama zakuthengo ndipo zidzakuphunzitsa, kapena mbalame zamumlengalenga ndipo zidzakuwuza;
8 Parle à la terre, elle t’instruira; Et les poissons de la mer te le raconteront.
kapena uyankhule ndi dziko lapansi ndipo lidzakuphunzitsa, kapena ulole nsomba zamʼnyanja kuti zikufotokozere.
9 Qui ne reconnaît chez eux la preuve Que la main de l’Éternel a fait toutes choses?
Kodi mwa zonsezi ndi chiti chimene sichidziwa kuti lachita zimenezi ndi dzanja la Yehova?
10 Il tient dans sa main l’âme de tout ce qui vit, Le souffle de toute chair d’homme.
Mʼmanja mwake ndi mʼmene muli moyo wa cholengedwa chilichonse, ndiponso moyo wa anthu a mitundu yonse.
11 L’oreille ne discerne-t-elle pas les paroles, Comme le palais savoure les aliments?
Kodi khutu sindiye limene limamva mawu monga mmene lilime limalawira chakudya?
12 Dans les vieillards se trouve la sagesse, Et dans une longue vie l’intelligence.
Kodi nzeru sipezeka pakati pa anthu okalamba? Kodi moyo wautali sumabweretsa nzeru zomvetsa zinthu?
13 En Dieu résident la sagesse et la puissance. Le conseil et l’intelligence lui appartiennent.
“Kwa Mulungu ndiye kuli nzeru ndi mphamvu; uphungu ndi kumvetsa zinthu ndi zake.
14 Ce qu’il renverse ne sera point rebâti, Celui qu’il enferme ne sera point délivré.
Chimene Iye wapasula palibe angachimangenso. Akatsekera munthu mʼndende palibe angamutulutse.
15 Il retient les eaux et tout se dessèche; Il les lâche, et la terre en est dévastée.
Iyeyo akamanga mvula dziko limawuma; akamasula mvulayo, madzi amasefukira pa dziko.
16 Il possède la force et la prudence; Il maîtrise celui qui s’égare ou fait égarer les autres.
Kwa Iye kuli mphamvu ndi kupambana; munthu wopusitsidwa ndiponso wopusitsa onse ali mu ulamuliro wake.
17 Il emmène captifs les conseillers; Il trouble la raison des juges.
Iye amalanda aphungu nzeru zawo ndipo amapusitsa oweruza.
18 Il délie la ceinture des rois, Il met une corde autour de leurs reins.
Iye amachotsa zingwe zimene mafumu anawamanga nazo ndipo amawamanga lamba mʼchiwuno mwawo.
19 Il emmène captifs les sacrificateurs; Il fait tomber les puissants.
Iye amasocheretsa ansembe atawalanda nzeru zawo ndipo amagonjetsa anthu amphamvu amene ndi okhazikika.
20 Il ôte la parole à ceux qui ont de l’assurance; Il prive de jugement les vieillards.
Iye amakhalitsa chete aphungu odalirika ndipo amalanda chidziwitso cha anthu akuluakulu.
21 Il verse le mépris sur les grands; Il relâche la ceinture des forts.
Iye amanyoza anthu otchuka ndipo anthu anyonga amawatha mphamvu.
22 Il met à découvert ce qui est caché dans les ténèbres, Il produit à la lumière l’ombre de la mort.
Iye amatulutsira poyera zinthu zozama za mu mdima ndipo mdima wandiweyaniwo amawusandutsa kuwala.
23 Il donne de l’accroissement aux nations, et il les anéantit; Il les étend au loin, et il les ramène dans leurs limites.
Iye amakuza mitundu ya anthu ndipo amayiwononganso; amachulukitsa mitundu ya anthu ndipo amayimwazanso.
24 Il enlève l’intelligence aux chefs des peuples, Il les fait errer dans les déserts sans chemin;
Iye amalanda nzeru za atsogoleri a dziko lapansi; amawayendetsa mʼthengo mopanda njira.
25 Ils tâtonnent dans les ténèbres, et ne voient pas clair; Il les fait errer comme des gens ivres.
Iwo amafufuzafufuza njira mu mdima wopanda chowunikira; Iye amawayendetsa dzandidzandi ngati oledzera.