< Ézéchiel 12 >
1 La parole de l’Éternel me fut adressée, en ces mots:
Yehova anayankhula nane kuti,
2 Fils de l’homme, tu habites au milieu d’une famille de rebelles, qui ont des yeux pour voir et qui ne voient point, des oreilles pour entendre et qui n’entendent point; car c’est une famille de rebelles.
“Iwe mwana wa munthu, ukukhala pakati pa anthu owukira, iwowo maso openyera ali nawo, koma sakuona ndipo makutu omvera ali nawo, koma sakumva chifukwa choti ndi anthu owukira.
3 Et toi, fils de l’homme, prépare tes effets de voyage, et pars de jour, sous leurs yeux! Pars, en leur présence, du lieu où tu es pour un autre lieu: peut-être verront-ils qu’ils sont une famille de rebelles.
“Choncho, iwe mwana wa munthu, longedza katundu wako wopita naye ku ukapolo. Unyamuke nthawi yamasana iwo akuona. Uchite ngati wanyamuka kuchoka kumene ukukhala kupita ku dziko lachilendo iwowo akuona. Mwina adzamvetsetsa, paja ndi anthu aupandu.
4 Sors tes effets comme des effets de voyage, de jour sous leurs yeux; et toi, pars le soir, en leur présence, comme partent des exilés.
Utulutse katundu wako wopita naye ku ukapolo nthawi ya masana iwo akuona. Ndipo nthawi ya madzulo, iwo akuona, uchoke monga ngati ukupita ku ukapolo.
5 Sous leurs yeux, tu perceras la muraille, et tu sortiras tes effets par là.
Iwo akuona, ubowole pa khoma ndipo utulutsirepo katundu wako.
6 Sous leurs yeux, tu les mettras sur ton épaule, tu les sortiras pendant l’obscurité, tu te couvriras le visage, et tu ne regarderas pas la terre; car je veux que tu sois un signe pour la maison d’Israël.
Usenze katundu wako pa phewa iwo akuona, ndipo upite kunja ku mdima. Uphimbe nkhope yako kuti usaone pansi, pakuti ndakusandutsa iwe chizindikiro chochenjeza Aisraeli.”
7 Je fis ce qui m’avait été ordonné: je sortis de jour mes effets comme des effets de voyage, le soir je perçai la muraille avec la main, et je les sortis pendant l’obscurité et les mis sur mon épaule, en leur présence.
Choncho ine ndinachita monga momwe anandilamulira. Nthawi yamasana ndinatulutsa zinthu zanga nditazimanga ngati ndikupita ku ukapolo. Ndipo nthawi yamadzulo ndinabowola khoma ndi manja anga. Pamene chisisira chinkayamba, ndinasenza katundu wanga pa phewa kutuluka naye iwo akuona.
8 Le matin, la parole de l’Éternel me fut adressée, en ces mots:
Mmawa mwake Yehova anandiyankhula nati:
9 Fils de l’homme, la maison d’Israël, cette famille de rebelles ne t’a-t-elle pas dit: Que fais-tu?
“Iwe mwana wa munthu, kodi anthu aupandu a Israeli sanakufunse kuti ukuchita chiyani?
10 Dis-leur: Ainsi parle le Seigneur, l’Éternel: Cet oracle concerne le prince qui est à Jérusalem, et toute la maison d’Israël qui s’y trouve.
“Uwawuze kuti, ‘zimene ndikunena Ine Ambuye Wamphamvuzonse ndi izi: Uthengawu ndi wonena za kalonga wa ku Yerusalemu pamodzi ndi banja lonse la Israeli amene akukhala kumeneko.’
11 Dis: Je suis pour vous un signe. Ce que j’ai fait, c’est ce qui leur sera fait: Ils iront en exil, en captivité.
Uwawuze kuti, ‘Ndiwe chizindikiro chowachenjeza.’ “Zidzakuchitikirani monga momwe zakuchitikira iwemu. Iwo adzatengedwa kupita ku ukapolo.”
12 Le prince qui est au milieu d’eux Mettra son bagage sur l’épaule pendant l’obscurité et partira; On percera la muraille pour le faire sortir; Il se couvrira le visage, Pour que ses yeux ne regardent pas la terre.
“Kalonga wawo adzatenga katundu wake nʼchisisira nʼkunyamuka. Adzatulukira pa bowo limene anthu anabowola pa khoma. Adzaphimba nkhope yake kuti asaone kumene akupita.
13 J’étendrai mon rets sur lui, Et il sera pris dans mon filet; Je l’emmènerai à Babylone, dans le pays des Chaldéens; Mais il ne le verra pas, et il y mourra.
Ndidzayala ukonde wanga pa iye ndi kumukola mu msampha wanga. Ndidzabwera naye ku Babuloni, dziko la Akaldeya, koma sadzaliona dzikolo, ndipo adzafera kumeneko.
14 Tous ceux qui l’entourent et lui sont en aide, Et toutes ses troupes, je les disperserai à tous les vents, Et je tirerai l’épée derrière eux.
Ine ndidzabalalitsa kumbali zonse zinayi onse okhala naye pafupi, ndiwo omuthandiza ake pamodzi ndi ankhondo ake. Ndidzawalondola ndi lupanga losolola.
15 Et ils sauront que je suis l’Éternel, Quand je les répandrai parmi les nations, Quand je les disperserai en divers pays.
“Iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, ndikadzawamwaza pakati pa anthu a mitundu ina ndi kuwabalalitsira ku mayiko ena.
16 Mais je laisserai d’eux quelques hommes Qui échapperont à l’épée, à la famine et à la peste, Afin qu’ils racontent toutes leurs abominations Parmi les nations où ils iront. Et ils sauront que je suis l’Éternel.
Koma ndidzasiyako ena pangʼono amene adzapulumuke ku lupanga, njala ndi mliri, kuti akafotokoze ntchito zawo zonse zonyansa pakati pa anthu achilendo kumene akupitako. Pamenepo adzadziwa kuti ndine Yehova.”
17 La parole de l’Éternel me fut adressée, en ces mots:
Pambuyo pake Yehova anandiyankhulanso nati,
18 Fils de l’homme, tu mangeras ton pain avec tremblement, Tu boiras ton eau avec inquiétude et angoisse.
“Iwe mwana wa munthu, uzinjenjemera ukamadya chakudya chako, ndipo uzinthunthumira ndi mantha ukamamwa madzi ako.
19 Dis au peuple du pays: Ainsi parle le Seigneur, l’Éternel, Sur les habitants de Jérusalem dans la terre d’Israël! Ils mangeront leur pain avec angoisse, Et ils boiront leur eau avec épouvante; Car leur pays sera dépouillé de tout ce qu’il contient, A cause de la violence de tous ceux qui l’habitent.
Uwawuze anthu a mʼdzikomo kuti izi ndi zimene Ambuye Wamphamvuzonse akunena za anthu okhala mu Yerusalemu ndi dziko la Israeli: Iwo adzadya chakudya chawo ndi mantha ndi kumwa madzi awo ndi nkhawa. Zonse za mʼdziko lawo zidzalandidwa chifukwa cha ziwawa za anthu onse okhala mʼmenemo.
20 Les villes peuplées seront détruites, Et le pays sera ravagé. Et vous saurez que je suis l’Éternel.
Mizinda imene ili ndi anthu idzasakazika ndipo dziko lidzasanduka chipululu. Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
21 La parole de l’Éternel me fut adressée, en ces mots:
Yehova anayankhulanso nane kuti,
22 Fils de l’homme, que signifient ces discours moqueurs Que vous tenez dans le pays d’Israël: Les jours se prolongent, Et toutes les visions restent sans effet?
“Iwe mwana wa munthu, kodi mwambi umene ukunenedwa mu Israeli ndi wotani: ‘Masiku akupita koma masomphenya onse sakukwaniritsidwa?’
23 C’est pourquoi dis-leur: Ainsi parle le Seigneur, l’Éternel: Je ferai cesser ces discours moqueurs; On ne les tiendra plus en Israël. Dis-leur, au contraire: Les jours approchent, Et toutes les visions s’accompliront.
Choncho uwawuze anthuwo kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndidzawuthetsa mwambi umenewu ndipo sadzawunenanso mu Israeli.’ Uwawuze kuti, ‘masiku ayandikira oti zonse zimene ndinanena mʼmasomphenya zichitikedi.
24 Car il n’y aura plus de visions vaines, Ni d’oracles trompeurs, Au milieu de la maison d’Israël.
Pakuti masiku amenewo sikudzakhalanso masomphenya abodza kapena kuwombeza kwa chinyengo pakati pa anthu a Israeli.
25 Car moi, l’Éternel, je parlerai; Ce que je dirai s’accomplira, Et ne sera plus différé; Oui, de vos jours, famille de rebelles, Je prononcerai une parole et je l’accomplirai, Dit le Seigneur, l’Éternel.
Koma Ine Ambuye ndidzayankhula chimene ndikufuna, ndipo chidzachitikadi, osachedwa ayi. Pakuti mʼmasiku anu omwe ano, inu anthu opanduka, ndidzakwaniritsa chilichonse chimene ndidzanena. Ndikutero Ine Yehova.’”
26 La parole de l’Éternel me fut adressée, en ces mots:
Yehova anandiyankhula nati:
27 Fils de l’homme, voici, la maison d’Israël dit: Les visions qu’il a ne sont pas près de s’accomplir; Il prophétise pour des temps éloignés.
“Iwe mwana wa munthu, Aisraeli akunena kuti, ‘masomphenya amene ukuona sadzachitika kwa zaka zambiri. Iwo akuti ukulosa za zinthu zimene zidzachitika ku tsogolo kwambiri.’
28 C’est pourquoi dis-leur: Ainsi parle le Seigneur, l’Éternel: Il n’y aura plus de délai dans l’accomplissement de mes paroles; La parole que je prononcerai s’accomplira, Dit le Seigneur, l’Éternel.
“Choncho uwawuze kuti, ‘zimene Ine Ambuye Yehova ndikunena ndi izi: Zonena zanga sizidzachedwanso; chilichonse chimene ndikunena chidzachitikadi. Ndikutero Ine Yehova.’”