< Deutéronome 32 >

1 Cieux! Prêtez l’oreille, et je parlerai; Terre! Écoute les paroles de ma bouche.
Mverani, inu mayiko a mmwamba ndipo ine ndidzayankhula; imva, iwe dziko lapansi, mawu a pakamwa panga.
2 Que mes instructions se répandent comme la pluie, Que ma parole tombe comme la rosée, Comme des ondées sur la verdure, Comme des gouttes d’eau sur l’herbe!
Chiphunzitso changa chigwe ngati mvula ndipo mawu anga atsike ngati mame, ngati mvumbi pa udzu watsopano, ngati mvula yochuluka pa zomera zanthete.
3 Car je proclamerai le nom de l’Éternel. Rendez gloire à notre Dieu!
Ndidzalalikira dzina la Yehova. Aa, tamandani ukulu wa Mulungu wathu!
4 Il est le rocher; ses œuvres sont parfaites, Car toutes ses voies sont justes; C’est un Dieu fidèle et sans iniquité, Il est juste et droit.
Iye ndi Thanthwe, ntchito zake ndi zangwiro, njira zake zonse ndi zolungama. Mulungu wokhulupirika amene salakwitsa, Iye ndiye wolungama ndi wosalakwa.
5 S’ils se sont corrompus, à lui n’est point la faute; La honte est à ses enfants, Race fausse et perverse.
Koma iwo achita mosakhulupirika pamaso pake, iwo si ana akenso, koma iwo ndi mʼbado wachinyengo ndi wokhotakhota.
6 Est-ce l’Éternel que vous en rendrez responsable, Peuple insensé et dépourvu de sagesse? N’est-il pas ton père, ton créateur? N’est-ce pas lui qui t’a formé, et qui t’a affermi?
Kodi mukumubwezera Yehova chotere, inu anthu opusa ndi opanda nzeru? Kodi Iye si Atate anu, Mlengi wanu, amene anakupangani ndi kukuwumbani?
7 Rappelle à ton souvenir les anciens jours, Passe en revue les années, génération par génération, Interroge ton père, et il te l’apprendra, Tes vieillards, et ils te le diront.
Kumbukirani masiku amakedzana; ganizirani za mibado yakalekale. Funsa abambo ako ndipo adzakuwuza, akuluakulu ako, ndipo adzakufotokozera.
8 Quand le Très-Haut donna un héritage aux nations, Quand il sépara les enfants des hommes, Il fixa les limites des peuples D’après le nombre des enfants d’Israël,
Pamene Wammwambamwamba anapereka mayiko kwa anthu a mitundu ina kukhala cholowa chawo, pamene analekanitsa anthu onse, anayikira malire anthu onse molingana ndi chiwerengero cha ana a Israeli.
9 Car la portion de l’Éternel, c’est son peuple, Jacob est la part de son héritage.
Pakuti gawo la Yehova ndi anthu ake, Yakobo ndiye cholowa chake.
10 Il l’a trouvé dans une contrée déserte, Dans une solitude aux effroyables hurlements; Il l’a entouré, il en a pris soin, Il l’a gardé comme la prunelle de son œil,
Anamupeza mʼchipululu, ku malo owuma ndi kopanda kanthu. Anamuteteza ndi kumusamalira; anamutchinjiriza ngati mwanadiso wake,
11 Pareil à l’aigle qui éveille sa couvée, Voltige sur ses petits, Déploie ses ailes, les prend, Les porte sur ses plumes.
ngati chiwombankhanga chimene chimasasula chisa chake nʼkumazungulira pamwamba pa ana ake, chimene chimatambalalitsa mapiko ake kuti chigwire anawo ndi kuwanyamula pa mapiko ake otambalalawo.
12 L’Éternel seul a conduit son peuple, Et il n’y avait avec lui aucun dieu étranger.
Yehova yekha ndiye anamutsogolera; popanda thandizo la mulungu wachilendo.
13 Il l’a fait monter sur les hauteurs du pays, Et Israël a mangé les fruits des champs; Il lui a fait sucer le miel du rocher, L’huile qui sort du rocher le plus dur,
Anamuyendetsa pamwamba pa mapiri a mʼdziko ndi kumudyetsa zipatso za mʼminda. Anamudyetsa uchi wofula pa thanthwe, ndiponso mafuta ochokera mʼnthaka ya miyala,
14 La crème des vaches et le lait des brebis, Avec la graisse des agneaux, Des béliers de Basan et des boucs, Avec la fleur du froment; Et tu as bu le sang du raisin, le vin.
pamodzi ndi chambiko ndi mkaka wochokera ku ngʼombe ndi nkhosa, ndiponso ana ankhosa onenepa ndi mbuzi, pamodzinso ndi nkhosa zazimuna zabwino za ku Basani ndiponso tirigu wabwino kwambiri. Munamwa vinyo wa thovu lofiira.
15 Israël est devenu gras, et il a regimbé; Tu es devenu gras, épais et replet! Et il a abandonné Dieu, son créateur, Il a méprisé le rocher de son salut,
Yesuruni ananenepa ndi kuyamba kuwukira; atakhuta, ananenepa ndi kukula thupi. Anasiya Mulungu amene anamulenga ndipo anakana Thanthwe ndi Mpulumutsi wake.
16 Ils ont excité sa jalousie par des dieux étrangers, Ils l’ont irrité par des abominations;
Anamuchititsa nsanje ndi milungu yawo yachilendo ndiponso anamukwiyitsa ndi mafano awo onyansa.
17 Ils ont sacrifié à des idoles qui ne sont pas Dieu, A des dieux qu’ils ne connaissaient point, Nouveaux, venus depuis peu, Et que vos pères n’avaient pas craints.
Anapereka nsembe kwa ziwanda zimene si Mulungu, milungu imene sankayidziwa nʼkale lomwe, milungu yongobwera kumene, milungu imene makolo anu sankayiopa.
18 Tu as abandonné le rocher qui t’a fait naître, Et tu as oublié le Dieu qui t’a engendré.
Inu munasiya Thanthwe limene linakulerani; munayiwala Mulungu amene anakubalani.
19 L’Éternel l’a vu, et il a été irrité, Indigné contre ses fils et ses filles.
Yehova anaona zimenezi ndipo anawakana chifukwa ana ake aamuna ndi aakazi anamukwiyitsa.
20 Il a dit: Je leur cacherai ma face, Je verrai quelle sera leur fin; Car c’est une race perverse, Ce sont des enfants infidèles.
Iye anati, “Ndidzawabisira nkhope yanga, ndi kuona kuti mathero awo adzakhala otani; pakuti ndi mʼbado wopotoka, ana amene ndi osakhulupirika.
21 Ils ont excité ma jalousie par ce qui n’est point Dieu, Ils m’ont irrité par leurs vaines idoles; Et moi, j’exciterai leur jalousie par ce qui n’est point un peuple, Je les irriterai par une nation insensée.
Anandichititsa kukhala wansanje pamene ankapembedza chimene si mulungu ndi kundikwiyitsa chifukwa cha mafano awo achabechabe. Ine ndidzawachititsa kuti achite nsanje ndi mtundu wina wopandapake; ndidzawakwiyitsa ndi mtundu wina wachabechabe.
22 Car le feu de ma colère s’est allumé, Et il brûlera jusqu’au fond du séjour des morts; Il dévorera la terre et ses produits, Il embrasera les fondements des montagnes. (Sheol h7585)
Pakuti mkwiyo wanga wayaka ngati moto, umene umayaka mpaka ku dziko la anthu akufa. Motowo udzanyeketsa dziko lapansi ndi zokolola zake ndipo udzapsereza maziko a mapiri. (Sheol h7585)
23 J’accumulerai sur eux les maux, J’épuiserai mes traits contre eux.
“Ndidzawawunjikira masautso ndipo mivi yanga yonse idzathera pa iwo.
24 Ils seront desséchés par la faim, consumés par la fièvre Et par des maladies violentes; J’enverrai parmi eux la dent des bêtes féroces Et le venin des serpents.
Ndidzawatumizira njala yoopsa, malungo woopsa ndi nthenda zofa nazo; ndidzawatumizira zirombo zakuthengo zowavuta, ululu wa njoka ya mʼphiri imene imakwawa pa fumbi.
25 Au-dehors, on périra par l’épée, Et au-dedans, par d’effrayantes calamités: Il en sera du jeune homme comme de la jeune fille, De l’enfant à la mamelle comme du vieillard.
Mʼmisewu lupanga lidzawasandutsa kukhala wopanda ana; mantha adzalamulira nyumba zawo. Anyamata ndi atsikana adzafa, ngakhalenso makanda ndi okalamba.
26 Je voudrais dire: Je les emporterai d’un souffle, Je ferai disparaître leur mémoire d’entre les hommes!
Ine ndinanena kuti ndidzawamwaza ndi kuwafafaniza kuti anthu asawakumbukirenso,
27 Mais je crains les insultes de l’ennemi, Je crains que leurs adversaires ne se méprennent, Et qu’ils ne disent: Notre main a été puissante, Et ce n’est pas l’Éternel qui a fait toutes ces choses.
koma sindinafune kuti adani anga adzandinyoze, mwina adani anga sadzandimvetsetsa ndipo adzanena kuti, ‘Tagonjetsa anthuwa ndife; Yehova sanachite zonsezi.’”
28 C’est une nation qui a perdu le bon sens, Et il n’y a point en eux d’intelligence.
Iwo ndi mtundu wopanda maganizo, iwo alibe nzeru nʼpangʼono pomwe.
29 S’ils étaient sages, voici ce qu’ils comprendraient, Et ils penseraient à ce qui leur arrivera.
Ngati iwo akanakhala anzeru akanamvetsetsa izi ndi kuzindikira kuti mathero awo adzakhala otani!
30 Comment un seul en poursuivrait-il mille, Et deux en mettraient-ils dix mille en fuite, Si leur Rocher ne les avait vendus, Si l’Éternel ne les avait livrés?
Kodi munthu mmodzi akanathamangitsa bwanji anthu 1,000 kapena anthu awiri kuthamangitsa anthu 10,000, kuti awagonjetse, Thanthwe lawo likanapanda kuwagulitsa, Yehova akanapanda kuwataya?
31 Car leur rocher n’est pas comme notre Rocher, Nos ennemis en sont juges.
Pakuti thanthwe lawo silofanana ndi Thanthwe lathu, ngakhale adani athu amavomereza zimenezi.
32 Mais leur vigne est du plant de Sodome Et du terroir de Gomorrhe; Leurs raisins sont des raisins empoisonnés, Leurs grappes sont amères;
Mpesa wawo umachokera ku mpesa wa ku Sodomu ndiponso ku minda ya ku Gomora. Mphesa zawo zili ndi ululu wakupha ndipo maphava ake ndi owawa.
33 Leur vin, c’est le venin des serpents, C’est le poison cruel des aspics.
Vinyo wawo ndi wa ululu wa njoka, ululu woopsa wa mphiri.
34 Cela n’est-il pas caché près de moi, Scellé dans mes trésors?
“Kodi zimenezi sindinazisunge ndi kuzitsekera mʼkatikati mwa chuma changa?
35 A moi la vengeance et la rétribution, Quand leur pied chancellera! Car le jour de leur malheur est proche, Et ce qui les attend ne tardera pas.
Kubwezera chilango nʼkwanga; ndidzawalanga ndine. Pa nthawi yake phazi lawo lidzaterera; tsiku lawo la masautso layandikira ndipo chiwonongeko chawo chikubwera pa iwo mofulumira.”
36 L’Éternel jugera son peuple; Mais il aura pitié de ses serviteurs, En voyant que leur force est épuisée, Et qu’il n’y a plus ni esclave ni homme libre.
Yehova adzaweruza anthu ake ndipo adzachitira atumiki ake chifundo pamene adzaona kuti mphamvu zawo zatha ndipo kuti palibe amene watsala, kapolo kapena mfulu.
37 Il dira: Où sont leurs dieux, Le rocher qui leur servait de refuge,
Iye adzanena kuti, “Nanga ili kuti milungu yawo, thanthwe limene ankabisalamo,
38 Ces dieux qui mangeaient la graisse de leurs victimes, Qui buvaient le vin de leurs libations? Qu’ils se lèvent, qu’ils vous secourent, Qu’ils vous couvrent de leur protection!
milungu imene inkadya mafuta a nsembe zawo ndi kumwa vinyo wa chopereka chawo cha chakumwa?” Iwuzeni ibwere kuti idzakuthandizeni! Ibwere kuti idzakutetezenitu!
39 Sachez donc que c’est moi qui suis Dieu, Et qu’il n’y a point de dieu près de moi; Je fais vivre et je fais mourir, Je blesse et je guéris, Et personne ne délivre de ma main.
“Onani tsopano kuti Ine ndine Iyeyo! Palibe mulungu wina koma Ine ndekha. Ine ndimapha ndiponso kupereka moyo, ndavulaza ndipo ndidzachiritsa, ndipo palibe angathe kupulumutsa munthu mʼmanja mwanga.
40 Car je lève ma main vers le ciel, Et je dis: Je vis Éternellement!
Ndikweza dzanja langa kumwamba ndi kulumbira kuti, ‘Pali Ine wamoyo wamuyaya,
41 Si j’aiguise l’éclair de mon épée Et si ma main saisit la justice, Je me vengerai de mes adversaires Et je punirai ceux qui me haïssent;
pamene ndidzanola lupanga langa lonyezimira ndipo dzanja liligwira pakubweretsa chiweruzo, ndidzabwezera chilango adani anga ndi kulanga onse odana nane.
42 Mon épée dévorera leur chair, Et j’enivrerai mes flèches de sang, Du sang des blessés et des captifs, De la tête des chefs de l’ennemi.
Mivi yanga idzakhuta magazi awo pamene lupanga langa lidzawononga mnofu: magazi a anthu ophedwa ndi ogwidwa ukapolo, mitu ya atsogoleri a adani.’”
43 Nations, chantez les louanges de son peuple! Car l’Éternel venge le sang de ses serviteurs, Il se venge de ses adversaires, Et il fait l’expiation pour son pays, pour son peuple.
Kondwerani, inu mitundu yonse ya anthu pamodzi ndi anthu ake, pakuti Iye adzabwezera chilango anthu amene anapha atumiki ake; adzabwezera chilango adani ake ndipo adzakhululukira dziko lake ndi la anthu ake.
44 Moïse vint et prononça toutes les paroles de ce cantique en présence du peuple; Josué, fils de Nun, était avec lui.
Mose anabwera ndi Yoswa mwana wa Nuni ndipo anayankhula mawu onsewa mʼnyimbo anthu akumva.
45 Lorsque Moïse eut achevé de prononcer toutes ces paroles devant tout Israël,
Mose atatsiriza kunena mawu onsewa pamtima kwa Aisraeli,
46 il leur dit: Prenez à cœur toutes les paroles que je vous conjure aujourd’hui de recommander à vos enfants, afin qu’ils observent et mettent en pratique toutes les paroles de cette loi.
iye anawawuza kuti, “Muwasunge bwino mu mtima mwanu, mawu onse amene lero lino ndikukuwuzani kuti mudzawuze ana anu, kuti adzamvere mosamalitsa mawu onse a malamulo amenewa.
47 Car ce n’est pas une chose sans importance pour vous; c’est votre vie, et c’est par là que vous prolongerez vos jours dans le pays dont vous aurez la possession, après avoir passé le Jourdain.
Mawuwa sikuti ndi mawu achabe kwa inu. Mawuwa ndi moyo wanu. Mukawamvera mudzakhala ndi moyo wautali mʼdziko limene mukukalitenga kukhala lanu mukawoloka Yorodani.”
48 Ce même jour, l’Éternel parla à Moïse, et dit:
Tsiku lomwelo Yehova anawuza Mose kuti,
49 Monte sur cette montagne d’Abarim, sur le mont Nebo, au pays de Moab, vis-à-vis de Jéricho; et regarde le pays de Canaan que je donne en propriété aux enfants d’Israël.
“Pita ku mapiri a ku Abarimu ukakwere pa Phiri la Nebo ku Mowabu, moyangʼanana ndi Yeriko, ndipo ukaone dziko la Kanaani, dziko limene ndikulipereka kwa Aisraeli kukhala lawo.
50 Tu mourras sur la montagne où tu vas monter, et tu seras recueilli auprès de ton peuple, comme Aaron, ton frère, est mort sur la montagne de Hor et a été recueilli auprès de son peuple,
Iwe udzafera pa phiri limenelo ndipo udzapita kumene makolo ako anapita, monga mʼbale wako Aaroni anafera pa phiri la Hori ndipo anakakhala ndi anthu a mtundu wake.
51 parce que vous avez péché contre moi au milieu des enfants d’Israël, près des eaux de Meriba, à Kadès, dans le désert de Tsin, et que vous ne m’avez point sanctifié au milieu des enfants d’Israël.
Chifukwa chake nʼchakuti inu nonse awiri simunakhulupirike kwa Ine pamaso pa Aisraeli pa madzi a Meriba ku Kadesi mʼchipululu cha Zini chifukwa simunandilemekeze kokwanira pakati pa Aisraeli.
52 Tu verras le pays devant toi; mais tu n’entreras point dans le pays que je donne aux enfants d’Israël.
Choncho udzalionera kutali dziko limene ndikupereka kwa Aisraeli. Sudzalowa mʼdziko limene ndi kulipereka kwa Aisraeli.”

< Deutéronome 32 >