< 1 Chroniques 25 >
1 David et les chefs de l’armée mirent à part pour le service ceux des fils d’Asaph, d’Héman et de Jeduthun qui prophétisaient en s’accompagnant de la harpe, du luth et des cymbales. Et voici le nombre de ceux qui avaient des fonctions à remplir.
Davide ndi atsogoleri a asilikali anapatula ena mwa ana a Asafu, Hemani ndi Yedutuni ku utumiki wa uneneri pogwiritsa ntchito apangwe, azeze ndi ziwaya zamalipenga. Tsopano nawu mndandanda wa anthu amene ankagwira ntchito imeneyi:
2 Des fils d’Asaph: Zaccur, Joseph, Nethania et Aschareéla, fils d’Asaph, sous la direction d’Asaph qui prophétisait suivant les ordres du roi.
Kuchokera kwa ana a Asafu: Zakuri, Yosefe, Netaniya ndi Asareli. Ana a Asafu amalamulidwa ndi Asafu ndipo amanenera moyangʼaniridwa ndi mfumu.
3 De Jeduthun, les fils de Jeduthun: Guedalia, Tseri, Ésaïe, Haschabia, Matthithia et Schimeï, six, sous la direction de leur père Jeduthun qui prophétisait avec la harpe pour louer et célébrer l’Éternel.
Kwa Yedutuni, kuchokera kwa ana ake: Gedaliya, Zeri, Yesaya, Simei, Hasabiya ndi Matitiya. Onse analipo 9 ndipo amayangʼaniridwa ndi Yedutuni abambo awo, amene amanenera pogwiritsa ntchito apangwe poyamika ndi kutamanda Yehova.
4 D’Héman, les fils d’Héman: Bukkija, Matthania, Uziel, Schebuel, Jerimoth, Hanania, Hanani, Éliatha, Guiddalthi, Romamthi-Ézer, Joschbekascha, Mallothi, Hothir, Machazioth,
Kwa Hemani, kuchokera kwa ana ake: Bukiya, Mataniya, Uzieli, Subaeli ndi Yerimoti; Hananiya, Hanani, Eliata, Gidaliti ndi Romamiti-Ezeri; Yosibakasa, Maloti, Hotiri ndi Mahazioti.
5 tous fils d’Héman, qui était voyant du roi pour révéler les paroles de Dieu et pour exalter sa puissance; Dieu avait donné à Héman quatorze fils et trois filles.
Onsewa anali ana a Hemani mlosi wa mfumu. Iye anapatsidwa anawa potsata mawu a Mulungu akuti adzamukweza. Mulungu anapatsa Hemani ana aamuna 14 ndi ana aakazi atatu.
6 Tous ceux-là étaient sous la direction de leurs pères, pour le chant de la maison de l’Éternel, et avaient des cymbales, des luths et des harpes pour le service de la maison de Dieu. Asaph, Jeduthun et Héman recevaient les ordres du roi.
Anthu onsewa ankayangʼaniridwa ndi makolo awo pa mayimbidwe a mʼNyumba ya Yehova. Iwowatu ankayimba ndi ziwaya zamalipenga, azeze ndi apangwe potumikira mʼNyumba ya Mulungu. Koma Asafu, Yedutuni ndi Hemani amayangʼaniridwa ndi mfumu.
7 Ils étaient au nombre de deux cent quatre-vingt-huit, y compris leurs frères exercés au chant de l’Éternel, tous ceux qui étaient habiles.
Iwo pamodzi ndi abale awo onse ophunzitsidwa ndi aluso loyimbira Yehova chiwerengero chawo chinali 288.
8 Ils tirèrent au sort pour leurs fonctions, petits et grands, maîtres et disciples.
Angʼonoangʼono ndi akulu omwe, mphunzitsi ndi wophunzira yemwe anachita maere pa ntchito zawo.
9 Le premier sort échut, pour Asaph, à Joseph; le second, à Guedalia, lui, ses frères et ses fils, douze;
Maere woyamba amene anali a Asafu, anagwera Yosefe, ana ndi abale ake. 12 Maere achiwiri anagwera Gedaliya, ndi abale ake ndi ana ake. 12
10 le troisième, à Zaccur, ses fils et ses frères, douze;
Maere achitatu anagwera Zakuri, ana ake ndi abale ake. 12
11 le quatrième, à Jitseri, ses fils et ses frères, douze;
Maere achinayi anagwera Iziri, ana ake ndi abale ake. 12
12 le cinquième, à Nethania, ses fils et ses frères, douze;
Maere achisanu anagwera Netaniya, ana ake ndi abale ake. 12
13 le sixième, à Bukkija, ses fils et ses frères, douze;
Maere achisanu ndi chimodzi anagwera Bukiya, ana ake ndi abale ake. 12
14 le septième, à Jesareéla, ses fils et ses frères, douze;
Maere achisanu ndi chiwiri anagwera Yesarela, ana ake ndi abale ake. 12
15 le huitième, à Ésaïe, ses fils et ses frères, douze;
Maere achisanu ndi chitatu anagwera Yeshaya, ana ake ndi abale ake. 12
16 le neuvième, à Matthania, ses fils et ses frères, douze;
Maere achisanu ndi chinayi anagwera Mataniya, ana ake ndi abale ake. 12
17 le dixième, à Schimeï, ses fils et ses frères, douze;
Maere a khumi anagwera Simei, ana ake ndi abale ake. 12
18 le onzième, à Azareel, ses fils et ses frères, douze;
Maere a 11 anagwera Azareli, ana ake ndi abale ake. 12
19 le douzième, à Haschabia, ses fils et ses frères, douze;
Maere a 12 anagwera Hasabiya, ana ake ndi abale ake. 12
20 le treizième, à Schubaël, ses fils et ses frères, douze;
Maere a 13 anagwera Subaeli, ana ake ndi abale ake. 12
21 le quatorzième, à Matthithia, ses fils et ses frères, douze;
Maere a 14 anagwera Matitiya, ana ake ndi abale ake. 12
22 le quinzième, à Jerémoth, ses fils et ses frères, douze;
Maere a 15 anagwera Yeremoti, ana ake ndi abale ake. 12
23 le seizième, à Hanania, ses fils et ses frères, douze;
Maere a 16 anagwera Hananiya, ana ake ndi abale ake. 12
24 le dix-septième, à Joschbekascha, ses fils et ses frères, douze;
Maere a 17 anagwera Yosibakasa, ana ake ndi abale ake. 12
25 le dix-huitième, à Hanani, ses fils et ses frères, douze;
Maere a 18 anagwera Hanani, ana ake ndi abale ake. 12
26 le dix-neuvième, à Mallothi, ses fils et ses frères, douze;
Maere a 19 anagwera Maloti, ana ake ndi abale ake. 12
27 le vingtième, à Élijatha, ses fils et ses frères, douze;
Maere a 20 anagwera Eliyata, ana ake ndi abale ake. 12
28 le vingt et unième, à Hothir, ses fils et ses frères, douze;
Maere a 21 anagwera Hotiri, ana ake ndi abale ake. 12
29 le vingt-deuxième, à Guiddalthi, ses fils et ses frères, douze;
Maere a 22 anagwera Gidaliti, ana ake ndi abale ake. 12
30 le vingt-troisième, à Machazioth, ses fils et ses frères, douze;
Maere a 23 anagwera Mahazioti, ana ake ndi abale ake. 12
31 le vingt-quatrième, à Romamthi-Ézer, ses fils et ses frères, douze.
Maere a 24 anagwera Romamiti-Ezeri, ana ake ndi abale ake 12.