< Zacharie 9 >

1 Paroles du Seigneur contre la terre de Sedrach; et celle de Damas sera sacrifiée comme elle; car le Seigneur surveille les hommes et toutes les tribus d'Israël.
Mawu a Yehova odzudzula dziko la Hadiraki ndi mzinda wa Damasiko pakuti maso a anthu ndiponso mafuko onse a Israeli ali pa Yehova—
2 Et cette parole est contre la terre d'Émath qui contient Tyr et Sidon, parce qu'elles ont trop connu la sagesse.
ndiponso mzinda wa Hamati, umene ukuchita malire ndi dzikoli, komanso pa Turo ndi Sidoni, ngakhale kuti iwo ndi anzeru kwambiri.
3 Or Tyr s'est bâti des forteresses, et elle a thésaurisé de l'argent par monceaux comme de la poussière, et des amas d'or comme la boue des chemins.
Ndipo Turo anadzimangira linga; wadziwunjikira siliva ngati fumbi, ndi golide ngati zinyalala za mʼmisewu.
4 Et à cause de cela le Seigneur en prendra possession, et Il jettera ses forces à la mer, et elle-même sera dévorée par le feu.
Taonani Ambuye adzamulanda chuma chakecho ndi kuwononga mphamvu zake mʼnyanja, ndipo adzapserera ndi moto.
5 Ascalon le verra et en tremblera; Gaza le verra et en souffrira cruellement; Ascaron le verra et sera confondue de sa chute; et le roi de Gaza périra, et Ascalon ne sera plus habitée.
Mzinda wa Asikeloni udzaona zimenezi, nʼkuchita mantha; Gaza adzanjenjemera ndi ululu, chimodzimodzinso Ekroni, chifukwa chiyembekezo chake chidzatheratu. Mfumu ya ku Gaza idzaphedwa ndipo Asikeloni adzakhala opanda anthu.
6 Et des étrangers repeupleront Azot; et J'abattrai l'orgueil des Philistins.
Mu Asidodi mudzakhala mlendo, ndipo ndidzathetsa kunyada kwa Afilisti.
7 Et J'ôterai de leur bouche le sang des victimes, et l'abomination d'entre leurs dents; et ils seront aussi délaissés par notre Dieu, et ils seront comme un chef de mille hommes en Juda, et Ascaron sera comme un Jébuséen.
Ndidzachotsa nyama ya magazi mʼkamwa mwawo, chakudya choletsedwa mʼmano mwawo. Amene atsala adzakhala anthu a Mulungu wathu, adzasanduka atsogoleri mu Yuda, ndipo Ekroni adzakhala ngati Ayebusi.
8 Et J'élèverai un rempart autour de Ma maison, pour qu'on ne puisse plus la traverser et y revenir, et que nul envahisseur n'y pénètre désormais; car maintenant Je la vois de Mes yeux.
Koma Ine ndidzalondera Nyumba yanga ndi kuyiteteza kwa ankhondo osakaza. Palibenso mdani amene adzagonjetse anthu anga, pakuti tsopano ndikuwayangʼanira.
9 Réjouis-toi grandement, Sion, Ma fille, annonce à haute voix, Jérusalem, Ma fille: Voilà que ton Roi vient à toi, juste et sauveur, et Il est plein de douleur, Il est monté sur un âne, et sur un ânon, petit de l'ânesse.
Sangalala kwambiri, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni! Fuwula, mwana wamkazi wa Yerusalemu! Taona, mfumu yako ikubwera kwa iwe, yolungama ndi yogonjetsa adani, yodzichepetsa ndi yokwera pa bulu, pa mwana wamphongo wa bulu.
10 Et Il détruira les chars d'Éphraïm et la cavalerie de Jérusalem; et l'arc des batailles sera brisé, et il y aura paix et abondance parmi les nations; et Il régnera depuis les eaux jusqu'à la mer, depuis les fleuves jusqu'aux confins de la terre.
Ndidzachotsa magaleta ankhondo ku Efereimu ndi akavalo ankhondo ku Yerusalemu, ndipo uta wankhondo udzathyoka. Mfumuyo idzabweretsa mtendere pakati pa mitundu ya anthu. Ulamuliro wake udzayambira ku nyanja ina mpaka ku nyanja ina, ndipo kuchokera ku Mtsinje (Yufurate) mpaka ku malekezero a dziko lapansi.
11 Et toi, à cause du sang de ton alliance, tu as retiré tes captifs d'une citerne sans eau.
Tsono kunena za iwe, chifukwa cha magazi a pangano lako ndi Ine, ndidzamasula amʼndende ako, ndidzawatulutsa mʼdzenje lopanda madzi.
12 Et vous, captifs de la Synagogue, établissez-vous en des forteresses; et, pour un jour de captivité, Je vous rétribuerai doublement.
Bwererani ku malo anu otetezedwa, inu amʼndende achiyembekezo; ngakhale tsopano ndikulengeza kuti ndidzakubwezerani zabwino mowirikiza.
13 Juda, tu es Mon arc, et Je t'ai tendu; J'ai rempli Éphraïm; J'exciterai tes enfants, ô Sion, contre les enfants des Hellènes, et Je te manierai comme le glaive des combattants.
Ndidzakoka Yuda monga ndimakokera uta wanga, ndipo Efereimu ndiye muvi wake. Ndidzadzutsa ana ako iwe Ziyoni, kulimbana ndi ana ako iwe Grisi, ndipo ndidzakusandutsa iwe lupanga la munthu wankhondo.
14 Et le Seigneur sera près d'eux; Son trait partira comme un éclair; et le Seigneur tout-puissant sonnera de la trompette, et Il S'avancera dans le tumulte de Ses menaces.
Pamenepo Yehova adzaonekera kwa anthu ake; mivi yake idzangʼanima ngati chingʼaningʼani. Ambuye Yehova adzaliza lipenga; ndipo adzayenda mu mkuntho wochokera kummwera,
15 Mais le Seigneur tout-puissant protégera les siens; ils extermineront leurs ennemis; ils les couvriront de pierres de leurs frondes; ils boiront leur sang comme du vin, et ils en rempliront leurs coupes, comme l'autel.
ndipo Yehova Wamphamvuzonse adzawateteza. Iwo adzawononga ndipo adzagonjetsa ndi miyala ya legeni. Adzamwa magazi ndi kubangula ngati amwa vinyo; magazi adzayenderera ngati a mʼmbale yowazira magazi pa ngodya za guwa lansembe.
16 Et en ce jour le Seigneur leur Dieu les sauvera; Il sauvera Son peuple, comme un troupeau de brebis, parce que des pierres saintes sont roulées sur Sa terre.
Tsiku limenelo Yehova Mulungu wawo adzawapulumutsa pakuti anthu ake ali ngati nkhosa. Adzanyezimira mʼdziko lake ngati miyala yokongola pa chipewa chaufumu.
17 Car si quelque chose est Son bien, si quelque chose est Sa beauté, c'est le pain pour les jeunes hommes, et le vin d'odeur de suavité pour les vierges.
Taonani chikoka ndi kukongola kwawo! Tirigu adzasangalatsa anyamata, ndi vinyo watsopano anamwali.

< Zacharie 9 >